< Job 11 >
1 Then Zophar, from [the] Naamah [area], said this to Job:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2 “(Should no one answer all that you have said?/Someone should certainly answer all that you have said.) [RHQ] Just because you talk a lot, (should that cause us to declare that you (are innocent/have done nothing wrong)?/that should not cause us to declare that you (are innocent/have done nothing wrong).) [RHQ]
“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
3 Job, (should your babbling cause us to be silent?/your babbling should certainly not cause us to be silent.) [RHQ] When you make fun of us, shall no one [rebuke you and] cause you to be ashamed?
Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
4 You say, ‘What I say is true; God knows that I am (innocent/without guilt).’
Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
5 But I wish/desire that God would talk and say something [MTY] to answer you!
Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
6 God knows everything about everything, so I wish/desire that he would tell you the secrets that he knows because he is wise. But you need to know that God is punishing you less than you deserve!
ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
7 [“Tell me], will you ever be able to find out the things about God that are very difficult to understand? Will you be able to find out everything that there is to know about Almighty God?
“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
8 [What there is to know about God] is greater than [the distance from earth to] heaven; so there is no way [RHQ] that you can [understand it all]. It is greater than [the distance from here to] the place of the dead; so it is impossible for you [RHQ] to know it all. (Sheol )
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol )
9 What there is to know about God is wider than the earth and wider than the ocean.
Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
10 “If God comes to you and puts you in prison and then brings you to a court, (who can stop him?/no one can stop him.) [RHQ]
“Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
11 He knows which people are worthless; and when he sees people doing wicked things, (will he ignore it?/he will certainly not ignore it!) [RHQ]
Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
12 Stupid people [like you] will start to become wise [SAR] when wild donkeys [stop giving birth to wild donkeys and] start giving birth to tame donkeys.
Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
13 “Job, repent [IDM]; reach out your hands to seek God’s help.
“Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
14 If you have done evil things, stop doing them; and do not allow any people in your house to do wicked things.
ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
15 If you do what I have said, surely you will lift up your head because you will not be ashamed; you will be strong, and not afraid [of anything].
udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
16 You will forget all your troubles; they will be like [the] water [of a flood] that has all disappeared.
Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
17 [Your troubles will be ended, like the darkness ends] at the dawn; [it will be as though] [MET] the sun is shining brightly on you, like [it shines] at noon.
Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
18 You will feel safe/secure, because you will confidently expect [that good things will happen to you]; God will protect you and enable you to rest safely [each night].
Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
19 You will lie down, and no one will cause you to be afraid. And many people will come and request you to do things for them.
Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
20 But wicked people [SYN] will not be able to understand [why bad things are happening to them]; they will not have any way to escape [from their troubles]. The only thing that they will want to do is to die. [EUP]”
Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”