< Jeremiah 9 >

1 I wish that my head was [like] [MET] a spring of water, and that my eyes were [like] a fountain of tears. Then I would cry night and day for all of my people who have been killed [by our enemies].
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 I wish that I could leave my people and forget them, and go and live in a shack/shelter in the desert, because they have not remained faithful [MET] [to Yahweh]; they are a mob of people who deceive others.
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 [Yahweh replied to me], “They use their tongues [to tell] [MET] lies like people shoot [arrows] with bows. It is because they tell lies that they have become more powerful in this land, and they do not know me.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 Do not trust your neighbors and [even] your brothers! They all are as deceitful [as Jacob was]. They slander [each other] and tell lies [about each other].
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 They deceive their friends and never tell the truth. They lie continually and, because of that, they have become skilled liars; they do one oppressive thing after another, and are unable to stop doing it.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 They habitually lie and deceive [each other], and no one will admit/say that I am God.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 Therefore [I], the Commander of the armies of angels, say this: Listen carefully to what I say: I will [cause my people to experience great afflictions, ] [like a metalworker puts metal in a hot fire] [MET] to completely burn out the impure bits. Because of all [the evil things] that my people have done, there is absolutely nothing else [RHQ] that I can do.
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 What they say [MTY] [injures people like] [MET] poisoned arrows do. They say to their neighbors, ‘I hope things will go well for you,’ while they are planning to kill them.
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Should I not punish them for doing that [RHQ]? Yes, I should certainly (get revenge on/give what they deserve to) [the people of] a nation that does things like that!”
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 So, I will weep and wail for [the people who live in] the mountains and in the (pastures/places where the livestock eat the grass), because those areas will be desolate, and no one will live there. There will be no cattle there to call to each other, and all the birds and wild animals will have fled [to other places].
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 [Yahweh also says], “I will cause Jerusalem to become a heap of ruins, and [only] jackals/wolves will live there. I will destroy the towns of Judah, with the result that they will be completely deserted; no one will live there.”
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 [I said], “Only people who are very wise [RHQ] can understand these things. Only those who have been taught by Yahweh can [RHQ] explain these things to others. The wise people are [RHQ] the only ones who can explain why the land will be completely ruined with the result that everyone [RHQ] will be afraid to travel through it.”
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 Yahweh replied, “[These things will happen] because my people have rejected my laws which I gave to them; they have not obeyed me or my instructions.
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 Instead, they have stubbornly done the things that they wanted to do. They have worshiped the idols that represent the god Baal, which is what their ancestors did.
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 So now listen to what [I], the Commander of the armies of angels, the God of the Israelis, say: [What I will do will be like] [MET] giving these people bitter things to eat and poison to drink:
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 I will scatter them to many nations which neither they nor their ancestors have known [anything about]; I will [enable their enemies to] strike them with swords until I have destroyed them.”
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 This is also what the Commander of the armies of angels says: “Think [about what is happening], [then] summon those women who mourn [when someone has died].
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Tell them to come quickly and start to wail, with the result that tears will stream down from your(pl) eyes.
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 Listen to [the people of] Jerusalem crying/lamenting, saying, ‘We have been ruined/destroyed! We have experienced a terrible disaster! Now we are very ashamed, because our houses have been destroyed [by our enemies], and we [are being forced to] leave our land.’”
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 You women, listen to what Yahweh says [MTY]. Pay attention to his words [DOU]. Teach your daughters to wail. Teach each other how to sing funeral songs,
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 because people will be dying [PRS] in your houses and in palaces. There will be no more children playing in the streets, there will be no more young men [gathering] in the city squares/marketplaces.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 There will be corpses scattered across the fields like dung; their dead bodies will lie there like [SIM] grain that has been cut by reapers/farmers, and there will be no one [still alive] to bury them.
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 Yahweh says this: “Wise men should not boast about their being wise, strong men should not boast about their being strong; and rich people should not boast about their being rich.
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 Instead, those who want to boast should boast about their knowing me and about understanding that I am Yahweh, that I am kind and just and righteous, that I faithfully love [people], and that I am delighted with [people who act] that way.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 There will be a time when I will punish all those people of Egypt and of the Moab people-group and of the Edom [people-group] and of the Ammon [people-group], all those people who live close to desert areas (OR, who cut their hair short [to please their gods]) far from Judah, all those people who have [changed their bodies by] circumcising them [MET] but who have not [changed] their inner beings. I will punish the people of Judah also, because they have not changed their inner beings, [either].”
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”

< Jeremiah 9 >