< Jeremiah 7 >

1 Yahweh gave me another message. He said to me,
Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
2 “Go to the entrance of my temple, and give this message to the people: You people of Judah who worship here, listen to this message from Yahweh!
“Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
3 The Commander of the armies of angels says to you, ['If you] stop doing evil things and start doing what is right, I will allow you to remain living in your land.'
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
4 [But some people] are repeatedly saying to you, ‘The temple of Yahweh is here, [so we will be safe]; [he will not allow us and the temple to be destroyed].’ But do not pay attention to what they say, because they are deceiving you.
Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
5 [I will act mercifully to you only] if you change your behavior and stop doing evil things, and if you [start to] act fairly/justly toward others,
Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
6 and if you stop oppressing foreigners [who live in your country], and orphans and widows, and if you stop murdering people, and if you stop worshiping (foreign gods/idols). However, if you continue to do those things, you will be destroyed.
ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
7 If you do what I have told you, I will allow you to stay in this land that I promised to your ancestors that it would belong to them [and their descendants] forever.
Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
8 [People are repeatedly] telling you, [‘The temple is here, so we are safe]’, and you are trusting/believing [that what they are saying is true], but it is a lie. [Those people are deceiving you, and what they say is] worthless.
Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
9 You think that [RHQ] you can steal things, murder people, commit adultery, tell lies in court, and worship Baal and all those other gods that you did not know about previously,
“Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
10 and then come here and stand in front of this temple, which is my temple, and say ‘Nothing bad will happen to us!’, while you continue to do all those abominable things.
ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
11 Do you realize that you are causing this temple, which is my temple, to become like [MET] a den where bandits hide [RHQ]? Do you not know that I see [all the evil things that you people do there]?
Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
12 [Long ago] I put my Sacred Tent at Shiloh [city], to be a place where people would worship me [MTY]. Think about how I [destroyed it] because my people, the Israeli people, did [many] wicked things there.
“‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
13 And while you were continually doing those wicked things, I told you about it many times, but you refused to listen. I called out to you, but you refused to answer [me].
Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
14 Therefore, just like I destroyed Shiloh, I will [now] destroy this temple that was built for people to worship me [MTY], this temple that you trust in, that is in this place that I gave to you and your ancestors.
choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
15 And I will expel you from this land and send you [to other countries] far away from me, just like I did to your relatives, the people of Israel.”
Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
16 [Yahweh said to me, “Jeremiah], do not pray for these people [any longer]. Do not cry for them or plead for [me to help] them, because I will not pay any attention to you.
“Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
17 Do you see [the wicked things] that they are doing in the streets of Jerusalem and in the [other] towns in Judah?
Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
18 The children gather firewood and their fathers use it to make fires [on the altars to burn sacrifices]. The women knead/make dough to make cakes to offer to [their goddess Astarte who is called] the Queen of Heaven. And [on their altars] they pour out offerings of wine to [their] other idols. All of those things cause me to become extremely angry!
Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
19 But I am not [RHQ] the one whom they are hurting; they are really [RHQ] hurting themselves [by doing these things for which they should be] very ashamed!”
Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
20 So Yahweh the Lord says this: “Because I am extremely angry with [what happens at] this place, I will punish these people severely [MTY]; my being very angry will be [like] [MET] a fire that will not be extinguished, and I will destroy the people, [their] animals, [their] fruit trees, and [their] crops.”
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
21 Therefore, this is what the Commander of the armies of angels says: “Take away [IRO] your offerings that you bring to burn completely on your altars and your [other] sacrifices; [don’t give them to me]; eat them [yourselves]!
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
22 When I led your ancestors out of Egypt, it was not offerings to be completely burned on the altar or [other] sacrifices that I wanted from them.
Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
23 What I told them was, ‘Obey me; [if you do that], I will be your God and you will be my people. If you do the things that I want you to do, everything will go well for you.’
koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
24 But your ancestors would not pay any attention [DOU] to me. They continued to do [the evil things] that they wanted to do, everything that in their stubborn inner beings they desired to do. Instead of coming closer to me, they went further away from me.
Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
25 From the day that your ancestors left Egypt until now, I have continued to send my prophets to you.
Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
26 But you, [my people], have not listened to me or paid attention to what I said; you have been stubborn, and you have done more sinful things than your ancestors did.”
Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
27 [Then Yahweh said to me], “When you tell all this to my people, they will not listen to you. When you call to them, they will not answer.
“Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
28 Say to them, ‘You people [of Judah] have not obeyed Yahweh, your God; you have not accepted it when he tried to correct you. No one among you is truthful; you do not say anything that is true; [you speak only lies].’
Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
29 [So, tell them to] cut off their hair [to show that they are mourning]; tell them to go up into the hills and sing a sad funeral song, because I have completely rejected [DOU] this generation [of people] who have made me angry.”
“Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
30 Yahweh says this: “The people of Judah have done many things that I say are evil. They have set up their disgusting idols in my temple, causing it to become an unacceptable [place to worship me].
“Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
31 They have built altars at Topheth in Ben-Hinnom Valley [outside Jerusalem], and they sacrifice their sons and daughters on those altars. I never commanded them to do that; I never even thought that anyone would do that.
Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
32 So they should beware! There will be a time when that place will no longer be called Topheth or the Hinnom Valley; instead, it will be called the Valley of Slaughter. There will be a huge number of people who will be buried there, with the result that there will be no space to bury more bodies.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
33 The corpses of my people that are [not buried and are] left on the ground will be eaten by vultures and wild animals, and there will be no one to shoo/chase them away.
Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
34 There will be no one singing and laughing any more in the streets of Jerusalem; there will be no more joyful voices of bridegrooms and brides in Judah, because the land will be completely destroyed.”
Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”

< Jeremiah 7 >