< Jeremiah 52 >
1 Zedekiah was twenty-one years old when he became the King [of Judah]. He ruled in Jerusalem for eleven years. His mother was Hamutal, the daughter of [a man named] Jeremiah from Libnah [town].
Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
2 Zedekiah did [many] things that Yahweh says are evil, like [his father] Jehoiakim had done.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
3 [The events that are summarized here happened] because Yahweh was angry with [the people of] Jerusalem and [of other places in] Judah, and finally he (exiled them/forced them to go to other countries) [and said that he did not want to have anything to do with] them any more. Zedekiah rebelled against the king of Babylon.
Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
4 [So, ] on January 15, when Zedekiah had been ruling for almost nine years, King Nebuchadnezzar of Babylon led his entire army to attack Jerusalem. They surrounded the city and built dirt ramps up to the top of the city walls [to enable them to attack the city].
Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
5 They continued to surround Jerusalem until Zedekiah had been ruling for almost eleven years.
Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
6 When Zedekiah had been ruling for almost eleven years, by July 18 of that year, the (famine/lack of food) in the city had become very severe, and there was no [more] food for the people [to eat].
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
7 Then [the soldiers of Babylonia] broke through [a section of] the city wall, and all the [Israeli] soldiers fled. But because the city was surrounded by soldiers from Babylonia, [Zedekiah and the Israeli] soldiers [waited until] it became dark. Then they left the city through the gate between the two walls behind the king’s garden. Then they ran towards the Jordan River Valley.
Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
8 But the soldiers of Babylonia pursued King Zedekiah, and they caught up with him on the plains near Jericho. [He was alone because] all his men had deserted him and had scattered.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
9 The soldiers of Babylonia took him to the king of Babylon, who was at Riblah in the Hamath [region]. There the king of Babylon told [his soldiers what] they should do to punish Zedekiah.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
10 They forced Zedekiah to watch while they killed his sons and all the officials from Judah.
Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
11 [Then] they gouged out Zedekiah’s eyes. They fastened him with bronze chains and took him to Babylon. They put him in a prison, and he remained there until the day that he died.
Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
12 On August 17 of that year, which was when King Nebuchadnezzar had been ruling for almost 19 years, Nebuzaradan, who was the captain of the king’s bodyguards and one of the king’s officials, arrived in Jerusalem.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
13 He [commanded his soldiers to] burn down the temple of Yahweh, the king’s palace, and all the houses in Jerusalem. They [also] destroyed all the important buildings [in the city].
Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
14 Then he supervised the soldiers from Babylonia while they tore down the walls on all sides of Jerusalem.
Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
15 Then Nebuzaradan (forced to go/exiled) [to Babylon] some of the poorest people, those Israelis who had said they would support the king of Babylon, the rest of the craftsmen, and other people who had remained in Jerusalem.
Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
16 But Nebuzaradan allowed some of the very poor people to remain [in Judah] to take care of the vineyards and fields.
Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
17 The soldiers from Babylonia broke [into pieces] the [huge] bronze pillars that were in front of the temple, and the [large] bronze water tank, and the [ten bronze water] carts, and they took all the bronze to Babylon.
Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
18 They also took away the basins [for holding the ashes from the burned sacrifices], the shovels [for cleaning out the ashes], the tools for snuffing out the wicks of the lamps, the basins [for holding the blood of the sacrificed animals], the dishes [for incense], and all the [other] bronze items that were used when sacrifices were made at the temple.
Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
19 Nebuzaradan also [told his soldiers to] take away the small bowls, the dishes for burning incense, the basins, pots, lampstands, bowls [for incense], and the bowls used for pouring out the wine offerings. They took all the other items that were made of pure gold or silver.
Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
20 The bronze from the two pillars, the [large water] tank and the twelve statues of oxen that were beneath it, and the water carts, was more/heavier than they could weigh. Those things had been made for the temple during the time that Solomon was the king.
Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
21 Each of the pillars was (27 feet/8 meters) tall and (18 feet/5.5 meters) around. They were hollow, and each had sides/walls that were (3 in./8 cm.) thick.
Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
22 The bronze head on the top of each pillar was (7-1/2 feet/over 2 meters) high and was decorated all around with a bronze [network of figures that represented] pomegranates.
Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
23 There was a total of 100 figures of pomegranates on the network at the top, 96 of which could be seen from the ground.
Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
24 When Nebuzaradan [returned to Babylon], he took [with him as prisoners] Seraiah the Supreme Priest, Zephaniah who was Seraiah’s deputy, and the three men who guarded the entrances [to the temple].
Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
25 He found [some other] people who were [hiding] in the city. [So] from them he took a commander of the army [of Judah], seven of the king’s advisors, the army commander’s chief secretary who was in charge of recruiting [soldiers for the army], and 60 [other] soldiers.
Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
26 Nebuzaradan took them all to the king of Babylon, [who was still] at Riblah.
Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
27 There at Riblah in the Hamath region, the king of Babylon commanded that they [all] be executed. [Many of the people of] Judah were (forced to leave/exiled from) their own land.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
28 The number of people who were captured and sent to Babylon at that time, when Nebuchadnezzar had been ruling for almost seven years, was 3,023.
Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
29 Then, when he had been ruling for almost 18 years, his [soldiers] took 832 [more Israeli people to Babylonia].
mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
30 When he had been ruling almost 23 years, he sent Nebuzaradan [to Jerusalem again], and he brought back 745 [more Israelis to Babylonia]. That was a total of 4,600 Israelis [who were taken to Babylonia].
mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
31 After King Jehoiachin of Judah had been in prison [in Babylon] for almost thirty-seven years, Evil-Merodach became the king of Babylon. He was kind to Jehoiachin and ordered that he be released from prison. That was on March 31 of the year that Evil-Merodach became king.
Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
32 He [always] spoke kindly to Jehoiachin and gave him a position in which he was honored more than [all] the other kings [who had been exiled/taken to Babylon].
Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
33 He [supplied new clothes] for Jehoiachin, to replace the clothes that he had been wearing in prison. [He also allowed] Jehoiachin to eat with him every day, all during the rest of his life.
Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
34 Every day, the King [of Babylon] gave him some money [to buy the things that he needed. That continued] until the day that Jehoiachin died.
Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.