< Jeremiah 47 >

1 Yahweh gave to the prophet Jeremiah a message about the people of Philistia. [The message was given to me] before Gaza [city in Philistia] was captured by [the army of] Egypt.
Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:
2 This is what Yahweh said: “[An army] [MET] will be coming from the northeast that will cover the land like a flood. They will destroy the land and everything in it; [they will destroy] people and cities. People will scream; everyone in the land will wail.
Yehova akuti, “Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto; adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo. Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo, mizinda ndi onse okhala mʼmenemo. Anthu adzafuwula; anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
3 [They will hear] the sound of the hooves of the [enemy] horses, and [they will hear] the rumble/noise of the wheels [of their enemies’] chariots. Men [will run away; ] they will not stop to help their children; they will be completely weak and helpless [MTY].
akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga, phokoso la magaleta ake ndi kulira kwa mikombero yake. Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo; manja awo adzangoti khoba.
4 It will be the time for all the people of Philistia to be destroyed, and the time to prevent the remaining soldiers from helping [the people of] Tyre and Sidon [cities]. [I, ] Yahweh, will get rid of the people of Philistia, those whose ancestors [long ago] came from Crete [island].
Pakuti tsiku lafika lowononga Afilisti onse ndi kupha onse otsala, onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni. Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti, otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
5 [The people of] Gaza will be humiliated; they will shave off all the hair on their heads [to indicate that they are ashamed]. The [people of] [city] will all be silent [because they will be mourning]. [All you people who live] along the coast [of the Mediterranean Sea] who are still alive, how long [RHQ] will you gash yourselves [because you are mourning]?”
Anthu a ku Gaza ameta mipala; anthu a ku Asikeloni akhala chete. Inu otsala a ku chigwa, mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?
6 [The people of Philistia say, ] “Yahweh, when [RHQ] will you [tell our enemies to stop killing us with] [PRS] their swords? Tell them to [PRS] put them back into their sheaths and keep them there!”
“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova, kodi udzapumula liti? Bwerera mʼmalo ako; ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
7 But it would not be right [RHQ] for their swords to stay there, because Yahweh has commanded their enemies [to do something more]; Yahweh intends to tell them to attack [all the people living in] Ashkelon and [in other cities] along the coast.
Koma lupangalo lidzapumula bwanji pamene Yehova walilamulira kuti lithire nkhondo Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”

< Jeremiah 47 >