< Jeremiah 43 >
1 [So] I finished telling to the people that message from Yahweh our God.
Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze,
2 But then Johanan and Azariah and some other insolent/arrogant men said to me, “You are lying! Yahweh our God has not told [us] that we should not go to Egypt!
Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’
3 [We think that] Baruch has urged/persuaded you to say this, in order that [if we stay here], the soldiers from Babylonia will seize us and kill us or take us to Babylonia.”
Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”
4 So Johanan and the other leaders of the [Israeli] soldiers and [many of] [HYP] the other people [who were there] refused to obey Yahweh’s command to stay in Judah.
Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda.
5 Johanan and all the [other] leaders gathered together all the people who had returned from the other countries to which they had been scattered.
Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako.
6 [They included] men, women, children, the king’s daughters, and all those whom Nebuzaradan had left with Gedaliah, and they also took Baruch and me.
Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
7 They refused to obey Yahweh, and they took us all [to Egypt], as far as Tahpenes [city].
Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.
8 [While we were] at Tahpenes, Yahweh gave me another message. He said,
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti,
9 “While the people of Judah are watching you, take some large rocks and bury them under the brick pavement at the entrance to the king’s palace there at Tahpenes.
“Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona.
10 Then say to the people of Judah, ‘This is what the Commander of the armies of angels, the God whom [you] Israelis [say you belong to], says: “I will summon Nebuchadnezzar the King of Babylon, who does my work, to come [with his army] to Egypt. I will set up his throne over these stones that I told Jeremiah to bury. And Nebuchadnezzar will set up his tent there [to show that he has become] the King [of Egypt].
Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi.
11 When his [army] comes, they will attack Egypt. Then those will die who [I have determined] must die, those who [I have determined] must be captured will be captured, and those who [I have determined] must be killed by swords will be killed by swords.
Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
12 Nebuchadnezzar’s [soldiers] will burn down the temples of the gods of Egypt. [But before they burn the temples], they will take away their idols [as souvenirs]. His [troops] will clean Egypt like a shepherd cleans lice from his cloak. They will tear down the sacred pillars that are in the temple of their sun god. And then Nebuchadnezzar’s [troops] will leave there, without having been harmed.”’”
Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere.
Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’”