< Jeremiah 26 >

1 Soon after Jehoiakim became the king of Judah, Yahweh gave [me] this message:
Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 “This is what [I], Yahweh, am telling you: Stand in the courtyard [in front] of my temple, and speak to all [the people from] the various towns in Judah who come there to worship me. Tell them everything that I tell you; do not omit anything.
“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
3 [If you do tell them everything], perhaps they will pay attention, and each one of them will turn away from his evil behavior. Then I will change my mind, and not cause them to experience the disaster that I was planning to cause them to experience because of the evil things that they have done.
Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
4 Say to them, ‘This is what Yahweh says: I sent to you the prophets who serve me, to tell you what you should do. I sent them to you many times, but you have not paid attention to what they said. If you will not pay attention to what I say and do not obey the message that I have given to you, and if you do not pay attention to what the prophets say,
Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
5
ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
6 I will destroy this temple like I destroyed Shiloh, [the place where the Sacred Tent was put]. And I will cause Jerusalem to be a place whose name [people in] every nation on the earth will say when they curse someone.’”
ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
7 [When I did what Yahweh told me to do, ] the priests, the [false] prophets, and many [other] people listened to me as I told them that message outside the temple.
Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
8 But as soon as I finished telling them everything that Yahweh had commanded me to say, they all seized me and said, “You must be executed!
Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
9 Why [RHQ] are you prophesying that this temple will be [destroyed] like Shiloh [was destroyed]? Why are you saying that this city will be destroyed, and that no one will live here [any more]? (OR, You should not be prophesying) [RHQ]” All the people surrounded me [as I stood] in [front of] the temple.
Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
10 When the officials of Judah heard about all this [that was happening], they rushed from the palace and sat down at the gate of the temple named The New Gate, [to judge my case].
Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
11 The priests and the [false] told the officials and the other people [who were there], “This man should be executed, because he has prophesied that this city [will be destroyed], and you yourselves [MTY] have heard him say that!”
Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
12 Then I replied to the officials and the other people, saying, “Yahweh sent me to prophesy all the things that you heard me say about [what will happen to] this temple and this city.
Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
13 But if you change your behavior and stop sinning, and [start to] obey Yahweh our God, he will change his mind, and not cause you to experience the disasters that he said that he would send.
Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
14 As for me, I am not able to free myself from your grasp. [So you can] do to me whatever you want to do.
Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
15 [But you need to] know that if you kill me, you will be killing a man [SYN] who (is innocent/has not done anything wrong). And you and everyone else in this city will be guilty, because the truth is that it was Yahweh who sent me to speak every word that you have heard me say.”
Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
16 Then the officials and the other people said to the priests and the [false] prophets, “This man does not deserve to be executed, because he has spoken to us the message [MTY] that Yahweh gave him!”
Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
17 Then some of the elders stood up and spoke to all the people who were gathered [there].
Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
18 They said, “([Remember/Think about) what] Micah, [the prophet] from Moresheth [town], prophesied during the years that Hezekiah was the King of Judah. He told the people of Judah this: ‘This is what the Commander of the armies of angels says: [Some day] Zion [Hill] will be plowed like fields [are plowed]; Jerusalem will become a heap of ruins. There will be a large clump/group of trees on top of the hill where the temple is now.’
“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
19 But did [RHQ] King Hezekiah or anyone else in Judah kill Micah [for saying that]? No! Instead, Hezekiah revered Yahweh, and pleaded that he would (act mercifully toward/not destroy) them. So, Yahweh changed his mind about causing them to experience the terrible disaster that he said he would send. And now [if we kill Jeremiah], we are going to cause ourselves to experience a terrible disaster!”
Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
20 [At that time, ] the son of Shemaiah from Kiriath-Jearim [city] was also prophesying/proclaiming messages [MTY] from Yahweh. He was predicting that the city and the rest of the land would experience the same disasters that I was predicting.
(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
21 When King Jehoiakim and his army officers and officials heard what Uriah was saying, the king sent someone to kill Uriah. But Uriah heard about it, and became [very] afraid, and he (escaped/ran away) to Egypt.
Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
22 Then King Jehoiakim sent Elnathan the son of Acbor along with several other men to Egypt.
Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
23 They captured Uriah and took him [back to Jerusalem] to King Jehoiakim. The king then [had a soldier] kill Uriah with a sword. Then they buried his corpse in a place where poor people are buried.
Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
24 However, Ahikam the son of Shaphan defended me, and persuaded the officials not to allow [MTY] the mob to murder me.
Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.

< Jeremiah 26 >