< Jeremiah 22 >

1 This is another message that Yahweh gave [to me]: “Go down to the palace of the king of Judah and say this to him:
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
2 ‘You are the king of Judah. You are the ruler [MTY], like King David was. You and your officials and your people must listen
‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
3 to what Yahweh says: “Act fairly and justly. Do what is right. Help those who have been robbed. Rescue people from those who oppress them. Stop doing evil things. Do not mistreat those who have come here from other countries, and do not mistreat orphans and widows. Stop murdering here [in Jerusalem] [MTY] those who (are innocent/have not done things that are wrong).
Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
4 If you obey those commands carefully, there will [always] be some descendant of King David who will be ruling here [MTY] [in Jerusalem]. The king and his officials and other people will ride through the gates of the city in chariots and on horses.
Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
5 But if you refuse to pay attention to those commands, I, Yahweh, solemnly declare, with myself [MTY] as a witness, that this palace will become a pile of rubble.”’”
Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
6 And this is what Yahweh says about the king’s palace: “[I like] this palace, like I like the forests in the Gilead [region] and the mountains in Lebanon. But I will cause this palace to become a desert, a place that no one lives in.
Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
7 I will summon enemy troops who will destroy this palace; each of their soldiers will use his own tools [to wreck the building]. They will cut into pieces the beautiful big cedar [beams] and throw them into a fire.”
Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
8 People from many nations will walk past [the ruins of] this city and say to each other, “Why did Yahweh destroy this city that was [very] great?”
“Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
9 And [other] people will reply, “[He did it] because his people stopped obeying the agreement that they had made with Yahweh their God. Instead, they worshiped [DOU] other gods.”
Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
10 [Yahweh also says, ] “Do not mourn for King [Josiah]; do not cry because he has died. Instead, mourn for [King Jehoahaz, his son], [because] he will be captured and taken to another country, and he will never return to see his own country, [Judah], again.”
Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
11 Jehoahaz became king after his father, King Josiah, [died], but Jehoahaz indeed was captured and taken [to Babylonia]. And this is what Yahweh says about him: “He also will never return [to Judah].
Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
12 He will die in that far-away country and will never see his own country again.”
Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
13 [And Yahweh said to me], “Terrible things will happen to [King Jehoahaz’s brother, King Jehoiakim]. He unjustly [forced men to] build his palace. The rooms on the upper level were built [by men who were forced] unjustly [to do that work]; he forced his neighbors to work for nothing; he did not pay them anything.
“Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
14 He said, ‘I will [force my workers to] build a huge beautiful palace with very large rooms and [many] windows. They will cover the walls with [fragrant] cedar panels/timber and paint them bright red.’”
Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
15 But it is certainly not [RHQ] having a beautiful cedar palace that causes a king to be great! Jehoiakim’s father, Josiah, also had [RHQ] plenty of things to eat and drink. But Josiah always did things that are right and just, and that is why God blessed him.
“Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
16 Josiah acted justly/fairly and helped poor and needy people, so things went well for him. Yahweh says, “That is [RHQ] the way a person should behave who knows me.
Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
17 But [Jehoiakim], you [MTY] are greedy and desire only to obtain things by acting dishonestly. You murder [MTY] innocent people, you oppress poor people, and you treat people cruelly and violently.”
“Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
18 Therefore, this is what Yahweh says about Jehoiakim, the son of King Josiah: “[When he dies], people will not mourn for him. They will not say to each other, ‘It is very sad; we are so sorry!’ The people whom he ruled will not mourn for him, saying, ‘We are sad that our king is dead; we are so sorry that the wonderful things [that happened while he was king are ended].’
Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
19 [When he dies, people will do to] his corpse what they do to a dead donkey; his [corpse] will be dragged out of Jerusalem and dumped outside the gates!
Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
20 [You people of Judah], go to [the mountains in] Lebanon and weep, shout in the [mountains of the] Bashan [region], cry out in [the mountains of] Moab, because all your friends [in those areas] have been destroyed.
“Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
21 When you were prosperous, I warned you, but you replied, ‘We will not pay attention [to what you say].’ You have been acting like that since you were young; you have never obeyed me.
Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
22 [So, now I will punish] all your leaders; [it will be as though] they have been blown away by the wind. They will be captured [by your enemies] and taken to another country. When that happens, you will [truly] be ashamed and disgraced because of all the wicked things [that you have done].
Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
23 [Now, your king] enjoys living in the cedar rooms in his palace, but [soon] he will be punished, and then he will groan like [SIM] a woman who is giving birth to a baby.”
Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
24 Yahweh says this: “Jehoiachin, son of King Jehoiakim of Judah, as surely as I am alive, [I will punish you]. Even if you were the ring on my finger that shows that I am the king, I would pull you off.
“Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
25 You are afraid of King Nebuchadnezzar of Babylon and his huge army, [because] they are wanting to kill you. I will enable them to capture you.
Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
26 I will expel you and your mother [from this land], and you will be taken to another country. Neither of you was born there, but you will both die there.
Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
27 You will never return to this land that you will very much desire to return to.”
Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
28 [Someone said, ] “Jehoiachin will be [RHQ] like a broken pot that is despised and which no one wants. He and his children will be (exiled/forced to go) to a foreign land.
Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
29 [I want] the people in this land to listen carefully to this message from Yahweh.”
Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
30 This is what Yahweh says: “[In the record about the kings of Judah, ] write down that [it will be as though] this man [Jehoiachin] had no children, and that he has not been successful during his life, because none of his children/descendants will [ever] become king to rule over [the people of] Judah.”
Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”

< Jeremiah 22 >