< Jeremiah 11 >
1 This is [another] message that Yahweh told me:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 “Listen to the agreement that I made with [the ancestors of] the people of Jerusalem and [the other cities in] Judah. Then remind them of [that agreement].
“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
3 Then tell them that [I], Yahweh, the God whom the Israeli [people worship], said that I will curse everyone who does not obey what was written in that agreement that I made with them.
Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
4 It is the same agreement that I made with their ancestors when I brought them out of Egypt. [What happened to them in Egypt was terrible; it was as though they were] living in a hot furnace [MET]. When I brought them out of Egypt, I told them to obey me, and to do everything that I had commanded them to do. [I also told them] that if they obeyed me, they would be my people and I would be their God.
Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
5 [Now tell these people that if they obey me], I will do what I promised to do for their ancestors. I will enable them to continue living in this very fertile [IDM] land in which they now live.” I replied, “Yahweh, I hope that what you said will happen.”
Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
6 Then Yahweh said to me, “Go into the streets of Jerusalem and to the [other] cities in Judah. Proclaim my message to the people. Tell them to listen to the agreement [that I made with their ancestors], and to obey it.
Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
7 When I brought their ancestors out of Egypt, I solemnly pleaded with them many times to obey me, and I am still pleading with them now.
Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
8 But they did not obey me or [even] pay any attention to me. Everyone continued to be stubborn and to do the evil things that they wanted to do. I commanded them to do what was written in the agreement, but they refused. So I punished them in all the ways that I promised that I would.”
Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
9 Then Yahweh said to me, “The people of Jerusalem and [the other cities in] Judah are rebelling against me.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
10 Their ancestors refused to do what I told them to do, and [now] these people have returned to committing the sins that their ancestors committed. They are worshiping other gods. The people of Israel disobeyed the agreement that I made with their ancestors, and [now] the people of Judah have done the same thing.
Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
11 So now I, Yahweh, am warning them that I will cause them to experience disasters, and they will not escape them. And when they cry out for me [to help them], I will not pay attention.
Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
12 When that happens, the people in Jerusalem and [other] cities in Judah will [offer sacrifices and] burn incense to their gods and ask for their help, but those gods will not be able to save them when those disasters come to them.
Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
13 There are more gods in Judah than there are towns in Judah, and the people of Jerusalem have erected as many altars to burn incense [to those gods] as there are streets in Jerusalem.
Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
14 Jeremiah, do not pray for these people, and do not plead with me to rescue them. If you plead with me, I will not pay attention; and if they cry out to me for help when they are in distress, I will not listen to them.”
“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
15 Then Yahweh said, “The people [of Judah] whom I love certainly no longer have [RHQ] a right to come to my temple, because they continually do many evil things. [They think that] continually making sacrifices of meat to me certainly will [RHQ] protect them from disasters, with the result that they will be able to rejoice.
“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
16 I previously said that they were like an olive tree full of green leaves with a lot of good olives on it, but [now I will send their enemies to attack] them furiously; [it is as though] I will break off their branches, and [their city] will be destroyed by fire.
Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
17 [It is as though] the people of Judah and Israel were a beautiful olive tree that I, the Commander of the armies of angels, planted, but [now], by burning incense to [their god] Baal, they have caused me to become [very] angry. So [now] I have decided to destroy them.”
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
18 Yahweh revealed to me that [my enemies] were planning to kill me.
Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
19 [Before he did that], I was like a lamb that was being led away to be slaughtered; I did not know what they were planning to do. I did not know that they were saying, “Let’s get rid of this tree and its fruit,” so [I did not know] that they intended to kill me, in order that no one would remember me [MTY].
Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
20 [Then I prayed], “Commander of the armies of angels, you judge people justly/fairly, and you examine everything that we are thinking [DOU]. Allow me to watch you getting revenge on the people [who want to kill me], because I trust that you will do for me what is right.”
Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
21 It was the men of [my own town], Anathoth, who wanted to kill me, and they told me that they would kill me if I did not stop prophesying what Yahweh told me to say.
“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
22 So the Commander of the armies of angels said [about them], “I will punish them. Their young men will be killed in wars, and their children will die because they have no food.
koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
23 I have set a time when I will bring disasters to the people of Anathoth, and when that happens, none of them will remain alive.”
Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”