< Isaiah 7 >

1 Ahaz was the son of Jotham and grandson of Uzziah. During the time that Ahaz was the king of Judah, King Rezin of Syria and King Pekah of Israel marched [with their armies] to attack Jerusalem. But they could not conquer it.
Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
2 [But before they attacked], everyone in the palace heard a report that the armies of Syria and Israel were [now] (allies/joined [to attack Jerusalem)]. So Ahaz and the people over whom he ruled were extremely afraid; they were shaking from fear like trees shake in a windstorm.
Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
3 Then Yahweh said to me, “Take your son Shear-Jashub, and go to talk with [King] Ahaz. He is at the end of the (aqueduct/water channel) that brings water into the upper reservoir, near the road to the place where women wash clothes.
Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
4 Tell Ahaz to stop worrying [DOU]. Tell him that he does not need to be afraid of those two kings, Rezin and Pekah. They are very angry [with Judah], but they are [unable to harm his country any more than] completely burned-out coals [can harm him].
Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
5 Yes, they are planning to attack this land and saying,
Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
6 ‘We will attack Judah and conquer it. Then we will appoint Tabeel’s son to be the king of Judah.’
‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
7 But this is what Yahweh, the Lord, says: ‘It will not happen; they will not [conquer Jerusalem]!
Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
8 The capital of Syria is Damascus, but Damascus is ruled [only] by its [unimportant/insignificant] king king Rezin. And as for Israel, within 65 years it will be conquered and completely destroyed.
pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
9 Israel’s capital is Samaria, and Samaria is ruled only by its [insignificant/unimportant] king king Pekah. [So you do not need to be afraid of those two countries]! [But you must trust me, because] if you do not trust me fully, you will be defeated.’”
Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
10 [Later], Yahweh gave [me another message to tell to] King Ahaz.
Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
11 [He said to tell him], “Request me, Yahweh your God, to do something that will enable you to be sure [that I will help/protect you]. What you request can be [from a place that is] as high as the sky or as low as the place where the dead people are.” (Sheol h7585)
“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
12 But [when I told that to the king, he refused]. He said, “[No], I will not request Yahweh to do something to prove [that he will help/protect us]!”
Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
13 Then I said [to him], “You people who are descendants of King David, listen! You are causing me to be tired of being patient. Are you also going to cause my God to stop being patient with you [RHQ]?
Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
14 Yahweh himself will do something for you [to prove that he will help/protect you]. Listen to this: A young woman will become pregnant and give birth to a son. She will name him Immanuel, [which means ‘God is with us’].
Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
15 And by the time that child is old enough to eat curds/yogurt and honey, he will be able to reject what is evil and choose what is good.
Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
16 And before that child is old enough to do that, the lands of the two kings that you(sg) are very (afraid of/worried about) will be deserted.
Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
17 [But then] Yahweh will cause you and your family and your entire nation to experience [terrible disasters]. Those disasters will be worse than any disasters that have occurred since the country of Israel separated from Judah. Yahweh will cause [the army of] the king of Assyria to attack you!”
Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
18 At that time, [it will be as though] Yahweh will whistle to summon the army from the south of Egypt as well as the army of Assyria. They will [come and surround your country like] [MET] flies and bees.
Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
19 They will all come and settle/live [everywhere]—in the narrow valleys and caves in the rock cliffs, on land where there are thornbushes as well as on the fertile land.
Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
20 At that time Yahweh will hire the king of Assyria to come [with his army] from east of the [Euphrates] River. [They will get rid of everything in your land—the crops and the people. They will destroy everything thoroughly]; it will be like [MET] a barber shaving not only a man’s hair but his beard and the hair on his legs.
Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
21 When that happens, a farmer will be able to have only one cow and two goats/sheep.
Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
22 [However], those animals will give plenty of milk, with the result that the farmer will have curds/yogurt to eat. And [because there will not be many people left] in the land, all the people who remain there will have plenty of milk and honey.
Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
23 Now there are many areas where there are vineyards that are worth 1,000 pieces of silver, but at that time there will be only briers and thorns [DOU] in those fields.
Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
24 There will be only briers and thorns in the entire land, [and wild animals], with the result that men will take their bows and arrows and go there [to hunt and kill animals].
Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
25 No one will go to where there previously were gardens on fertile hillsides, because briers and thorns will cover those hillsides. They will be areas where [only a few] cattle and sheep and goats wander around [searching for something to eat].
Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.

< Isaiah 7 >