< Isaiah 62 >

1 Because I am very concerned about [the people of] Jerusalem [DOU], I will do something to help them. I will not stop praying for them until they are rescued/freed [from their oppressors], until that becomes as apparent to everyone as the dawn [every morning], until people can see it as clearly as [SIM] they see a torch shining brightly [at night].
Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
2 [Some day] the [people of many] nations will know that Yahweh has rescued you, [his people]. Their kings will see that your city is [very] great/glorious. And Yahweh [MTY] will give your [city] a new name.
Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
3 [It will be as though] Yahweh will hold you up in his hands in order that everyone can see you. Under his authority [MTY], you will be [like] a glorious headband/turban worn by a king.
Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
4 Your [city] will never again be called “the deserted/abandoned city” and your country will never again be called “the desolate land”; it will be called “the land that Yahweh delights in”, and [it will also be called] “married to Yahweh”. It will be called that because Yahweh will be delighted with you, [and it will be as though] you are his bride [MET].
Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
5 You people will live in all the country of Judah like [SIM] a young man lives with his bride. And our God will be happy that you [belong to] him like [SIM] a bridegroom is happy that his bride [belongs to him].
Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
6 [You people of] Jerusalem, I have placed watchmen on your walls; they will [LIT] earnestly pray to Yahweh day and night. You watchmen, you must not stop [praying] [and] reminding Yahweh [about what he has promised to do]!
Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
7 And tell Yahweh that he should not rest until he causes Jerusalem to be [a city that is] famous throughout the world.
Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
8 Yahweh has raised his right hand to solemnly promise [to the people of Jerusalem], “I will use my power [MTY] and never again allow your enemies to defeat you; [soldiers from other nations will never come again] to take away your grain and the wine that you worked hard [to produce].
Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
9 You yourselves grew the grain, and you will be the ones who will praise [me], Yahweh, while you eat [the bread made from] that grain. Inside the courtyards of my temple you yourselves will drink the wine made from the grapes [that you harvested].”
Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
10 Go out through the [city] gates! Prepare the highway on which people [will return from other countries]! Cause the road to become smooth; clear off [all] the stones; set up signal flags to help the people-groups to see [where the road to Jerusalem is].
Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
11 This is the message that Yahweh has sent to [the people of] every nation: “Tell the people of Israel, ‘The one who will rescue/save you is coming! Look! He will be bringing to you (your reward/what you deserve [for the good things that you have done]); those whom he is setting free will be going ahead of him.’”
Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
12 They will be called “Yahweh’s own people, the ones whom he rescued”. And Jerusalem will be known as the city that [Yahweh] loves, the city that is no [longer] abandoned.
Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”

< Isaiah 62 >