< Isaiah 54 >
1 Yahweh says, “You [people of Jerusalem] [MET], start to sing! You [who are like] [MET] women who have never given birth to children, sing loudly and shout joyfully, because you, [who are like] [MET] childless women who have been abandoned [by their husbands], will [soon] have more children than women who have never had any children.
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 Make your tents larger; make them wider, and fasten them firmly with tent pegs.
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 [You will need to make your city much larger] because [soon] you and your descendants will spread all over the land. They will force the people of [other] nations [who now live in your cities] to leave, and you will live [again] in those cities [that were previously abandoned].
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 Do not be afraid; you will no [longer] be ashamed. Previously you were ashamed [because your enemies conquered you] and caused many of your women to become widows, but [soon] you will not even remember that.
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 [I], the Commander of the armies of angels, the Holy one of Israel, who rules over the whole earth, the one who created you, will be [like] [MET] a husband to you.
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 You were like a woman whose husband left her, and caused you to be very sad; you were like a young woman who got married when she was [very] young, and then her husband abandoned her.
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 I abandoned you [people of Jerusalem] for a while, but [now] I am saying, ‘I will take you back.’
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 I was very angry with you for a while, and I turned away from you. But I will act mercifully toward you and I will faithfully love you forever. That is what [I], Yahweh, your protector, say to you.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 During the time that Noah lived, I solemnly promised that I would never again allow a flood to cover the earth. So [now] I solemnly promise that I will not be angry with you again and (rebuke you/threaten to punish you).
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 Even if the mountains and hills shake and collapse, I will not stop faithfully loving you, and I will not cancel my agreement to cause things to go well for you. That is what [I], Yahweh, who act mercifully, say.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 You [people of Jerusalem] [APO], [your enemies acted very violently toward you]; [it was as though] your city was battered by a severe storm, and no one helped you. But [now] I will cause your city to be rebuilt with stones made of (turquoise/valuable stones), and I will cause the foundations of the city to be made of (sapphires/valuable blue stones).
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 I will cause the towers on the city wall to be made of (rubies/valuable red stones), and all the gates of the city will be made of [other] very valuable stones.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 I will be the one who will teach you people and cause things to go well with you.
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Your [government] will be strong because of acting justly/fairly; no one will (oppress you/cause you to suffer); you will not be afraid, because there will be nothing [PRS] that will (terrorize you/cause you to become extremely afraid).
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 If any army attacks you, it will not be because I have incited them to do that, and you will defeat any group that attacks you.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 Think about this: (Blacksmiths/Men who make things from metal) fan the coals to make a very hot flame in order to produce weapons that can be used [in battles], but I am the one who has produced blacksmiths! And I am also the one who created people who destroy [other people and cities].
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 [But I am promising you that I will] not allow you to be defeated/injured by soldiers using weapons that have been made to attack you, and when others try to accuse you, you will (refute them/show that they are wrong). That is the reward that I will give to the people who serve me; I will defend them; that is what [I], Yahweh, promise.”
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.