< Isaiah 49 >

1 All you people who live on islands [in the ocean] and in other distant areas, pay attention [DOU] to what I will say! Yahweh called/chose me before I was born; he chose/appointed me when I was still in my mother’s womb.
Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
2 [When I grew up], he caused my messages to be like [SIM] a sharp sword. He has protected me with his hand [SYN]. [He protects me] [MET] like someone protects sharp arrows in a quiver.
Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
3 He said to me, “You will serve my Israeli [people], and you will cause people to honor me.”
Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
4 I replied, “My work has been useless; I have used my strength, but I have accomplished nothing worthwhile; everything that I have done has been (in vain/useless). However, Yahweh can honor me as he pleases; my God is the one who will reward me [as I deserve].”
Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
5 Yahweh formed me when I was in [my mother’s] womb in order that I would serve him; he appointed me to bring [the people of] Israel back to himself [DOU]. Yahweh has honored me, and he is the one who has caused me to be strong.
Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
6 He says to me, “It is not enough for you to serve me by bringing the descendants of Jacob back to worship me again [DOU]; I also want you to be like [MET] a light for the non-Jews; I want you to take my [my message] about how to be saved to [people] all over the world.”
Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
7 Yahweh, the one who saves us, the Holy God of us Israeli [people], says to the one who was despised and rejected by the [people of many] nations, the one who is the slave of rulers, “[Some day] kings will stand up to respect you when they see you, and princes will bow down before you because [you serve] me, Yahweh, the one who faithfully [does what I promise]. I am the Holy God to whom you Israelis belong, the one who has chosen you.”
Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
8 This is also what Yahweh says: “At a time when it pleases me, I will answer your prayers. On the day when you will be rescued [from your oppressors], I will help you. I will protect you and enable you to establish an agreement with other nations. And by what you do, I will re-establish your nation of Israel and allow you to live/settle again in your land that was abandoned.
Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
9 I will say to those who were captured [and (exiled/taken to Babylonia)], ‘Leave [Babylonia] and return to your own country!’ And I will say to those who are in dark prisons, ‘Come out into the light!’ When that happens, they will again be like [MET] sheep that eat grass in green pastures, on hills where [previously] there was no grass.
Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
10 They will not be hungry or thirsty [any more]; the hot sun will not beat upon them again [DOU]. I, Yahweh, will act mercifully toward them and lead them; I will lead them to where there are springs of cool water.
Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
11 And I will cause the mountains to become [as though they were] level roads, and I will prepare good highways [for my people to travel on, to return to Jerusalem].
Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
12 My people will return from far away; some will come from the north, some from the west, some from southern Egypt.”
Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
13 [Because of what Yahweh has promised to do], everything should shout joyfully— the sky and the earth and the mountains should sing, because Yahweh comforts his people, and he will pity those who are suffering.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
14 [The people of] Jerusalem say, “Yahweh has abandoned us; he has forgotten about us.”
Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
15 But [Yahweh replies], “That is not true! (Can a woman forget the infant that she is nursing?/A woman certainly cannot forget the infant that she is nursing!) [RHQ] (Can she stop being kind to the child to whom she has given birth?/She certainly cannot stop being kind to the child to whom she has given birth!) [RHQ] But even if a woman would do that, I will not forget you!
“Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
16 Note that I have written your [names] on the palms of my hands; in my mind I can always see the walls of your city.
Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
17 Soon your children will be returning there (OR, Those who rebuild your city will work more quickly than those who destroyed it), and all those who destroyed your city will leave.
Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
18 You will look around and see all of your children coming back to you. As surely as I live, they will be around you [for you to show to people] like [SIM] a bride shows her wedding ornaments!
Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
19 Your land has been ruined and caused to become desolate/abandoned [DOU], but [some day] it will be filled with people, and those who conquered you will be far away.
“Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
20 The children who were born while you were (exiled/in Babylonia) [MET] will return [to Jerusalem] and say, ‘This city is too small for us; We need more space to live in!’
Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
21 Then you will think to yourselves [MTY], ‘It is amazing that we have [RHQ] all these children! Most of our children were dead, and the rest were exiled. We were left here alone; so we do not know [RHQ] where all these children have come from! Who raised them?'”
Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
22 This is what Yahweh our God says: “Watch! [It is as though] I will lift up my hand to signal to those who are not Israelis. And they will carry your little sons and daughters on their shoulders and bring them back to you.
Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
23 Kings will serve you and will tutor/teach your children, and their queens will take care of your young children. They will prostrate themselves in front of you and [humble themselves by] licking the dust off your feet. When that happens, you will know that I, Yahweh, [have the power to do what I say that I will do]; and those who trust in me will never be disappointed.”
Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
24 There is no one [RHQ] who can snatch valuable things from a soldier who has captured those things [in a war]; there is no one [RHQ] who can force a (tyrant/cruel man) to free the people whom he has captured.
Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
25 But Yahweh says this: “[Some day], those who have been captured will be freed, and the valuable things that (tyrants/cruel men) have snatched from others will be returned, because I will fight against those who fight against you, and I will rescue your children.
Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
26 And I will cause your enemies to destroy themselves [MET] instead of murdering others. When that happens, everyone [in the world] will know that I, Yahweh, am the one who saves you, the one who rescues you from your enemies; everyone will know that I am the mighty God to whom [you descendants of] [MTY] Jacob belong.”
Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”

< Isaiah 49 >