< Isaiah 44 >

1 But now, you people of Israel whom Yahweh has chosen to serve him, listen to me.
Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
2 Yahweh, the one who created you and helps you, says this: “You dear people of Israel whom I have chosen, you who serve me, do not be afraid.
Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
3 I will pour water on your dry land and cause streams to flow. And I will pour out my Spirit on your descendants and greatly bless them.
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
4 They will grow up like [SIM] grass grows along the water, like [SIM] willow/poplar [trees] grow well along a riverbank.
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
5 Some of them will say, ‘I belong to Yahweh,’ and others will say, ‘We are descendants of Jacob,’ and others will write on their hands, ‘We belong to Yahweh,’ and others will say, ‘We are Israelis.’”
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
6 Yahweh, the King of Israel, the one who saves us, the Commander of the armies of angels, says this: “I am the one who begins everything and who ends everything; there is no other God.
“Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
7 If there is anyone like me [RHQ], he should proclaim it! He should speak and tell me [now]! He should tell what has happened since I caused my people [of Israel] to become a nation long ago, and he should also tell what things will happen; he should predict what will happen in the future.
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
8 [My people], do not be afraid. Long ago I told you things that would happen [RHQ]; I predicted them, and you can testify that I did that. There certainly is not [RHQ] any other God. There is no other God who is able to protect you [MET]; I know that there is no other God!”
Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
9 All those who make idols are foolish, and the idols that they (think highly of/greatly respect) are worthless. And the people who worship those idols— [it is as though] they are blind, and they will be ashamed [for having worshiped those idols].
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
10 Only [foolish people] [RHQ] would make idols in a mold, idols that would never help them at all.
Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
11 Those who make idols and those who worship them will be ashamed. Those who make idols are only human beings, [but they claim that they are making gods]! They should stand in front of God in a court, and [when they hear what he says], they will be terrified, and they will all be disgraced.
Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
12 Metalworkers stand in front of hot coals in order to make idols. They pound them strongly with hammers, and shape them. Because they work very hard, they become hungry and weak; they become very thirsty and feel exhausted.
Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 Then a woodcarver takes a big block/piece of wood and he measures it; then he marks it to show where he will cut it. He uses a chisel and other tools to carve it to resemble a human. He causes it to become a very beautiful [idol], and then he puts it in a shrine.
Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 [Before he carves an idol from that block of wood], he has cut down a cedar tree, or he has selected a cypress tree or an oak tree and allowed it to grow tall in the forest. Or, he has planted a pine/evergreen tree and the rain has watered it [and caused it to grow tall].
Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 [And after he uses part of the tree to make an idol], he uses the other part of the tree to make a fire, either to warm himself or to bake bread. But he uses [part of the same tree] to make for himself an idol to worship! He makes an idol and then he bows down to worship it.
Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 He burns part of the wood of the tree to cook his meat and eats the meat and his stomach becomes full, and he burns part of the wood to warm his body, and he says, “I feel warm while I am watching the flames in the fire.”
Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 Then he takes the rest of the wood and makes an idol which is his god. He bows down to it and worships it, and prays to it and says, “You are my god, so save me!”
Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 Those people are very stupid and ignorant [SAR]. [It is as though] they are blind and cannot see, and their minds are closed and they cannot think well.
Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 They do not think about what they are doing, that they are taking a block of wood and burning half of it to warm themselves and using some of the rest to bake bread and roast some meat! [They do not say to themselves], “It is stupid [RHQ] to take the rest of the wood to make a detestable idol! It does not make sense to bow down to a block of wood!”
Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 They are very stupid to [worship something that if you burn it, it becomes] ashes! They trust in something that cannot save them; they do not admit, “In my hand I hold something that is not really a god! [RHQ]”
Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
21 [Yahweh says, “You descendants of] [MTY] Jacob, you people of Israel who should be serving me, I created you, and I will not forget you.
Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 I have gotten rid of your sins like [SIM] [the wind blows away] a cloud. [It is as though] your transgressions were a morning mist [SIM] that I have blown away. Return to me because I have rescued you.”
Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
23 [The sun and moon and stars] in the sky should sing, and all the things that are beneath the ground should shout joyfully! All the mountains and forests, and all you trees, should sing loudly, because Yahweh has rescued [the descendants of] [MTY] Jacob; [the people of] Israel will praise/honor him.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
24 Yahweh, who saved you and created you, says this: “I am Yahweh, the one who created everything. I am the only one who stretched out the sky. There was [RHQ] no one who (was with/helped) me when I created the earth.
Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
25 I show that the false prophets are liars, and I show that those who perform rituals to predict the future are fools. Some people who [falsely think that they] are [IRO] wise [say that they] know a lot, but I show that they are foolish.
Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
26 But I always cause to happen what my prophets predict [DOU]. [I tell them to] say to [the people of] [MTY] Jerusalem, ‘[Some day] people will live here again.’ [And I tell them to] say to [the people in other] towns in Judah [that Yahweh says], ‘Your towns will be rebuilt; I will cause the places that are only ruins to be rebuilt.’
Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
27 When I say to the rivers, ‘Dry up!’, they will become dry.
Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
28 When I say about King Cyrus, ‘He will [take care of my people like] [MET] a shepherd [takes care of his sheep], he will do what I want him to do,’ he will say about Jerusalem, ‘We must rebuild it!’, and he will also say, ‘We must rebuild the temple!’”
Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”

< Isaiah 44 >