< Isaiah 39 >

1 Soon after that, Baladan’s son Merodach-Baladan, the King of Babylon, heard a report that Hezekiah had been very sick but that he had recovered. So he wrote some notes and gave them to some messengers to take to Hezekiah, along with a gift.
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
2 [When the messengers arrived], Hezekiah welcomed them gladly. [Then] he showed them everything that was in his (treasure houses/places where very valuable things were kept)—the silver, the gold, the spices, and the nice-smelling [olive] oil. He also took them to see the place where they kept their soldiers’ weapons, and he showed them the other valuable things that were in the storehouses. Hezekiah showed them everything [LIT] that was in the palace or in other places [HYP].
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Then I went to King Hezekiah and asked him, “Where did those men come from, and what did they want?” He replied, “They came from the far away land of Babylon.”
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 I asked him, “What did they see in your palace?” Hezekiah replied, “They saw everything. I showed them absolutely everything that I own—all my valuable things.”
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 Then I said to Hezekiah, “Listen to this message from the Commander of the armies of angels:
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
6 'There will be a time when everything in your palace, all the valuable things that your ancestors stored there up until the present time, will be carried away to Babylon. Yahweh says that there will be nothing left.
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
7 Furthermore, some of your sons will be forced to go to Babylon. They will be castrated in order that they can become servants in the palace of the king of Babylon.'”
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 Then Hezekiah replied to me, “That message from Yahweh that you have given to me is good.” He said that because he was thinking, “Even if that happens, there will be peace, and people in this country will be safe during the time that I am alive.”
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”

< Isaiah 39 >