< Isaiah 28 >
1 Terrible things will happen to [Samaria city, the capital of Israel]! It is on a hill above a fertile valley; the people who live there, who get drunk by drinking too much wine, are very proud; it is a beautiful and glorious city, but some day that beauty will disappear like [MET] a flower that wilts and dries up.
Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
2 Listen to this: Yahweh will cause a great army to attack Samaria. Their soldiers will be like [SIM] a huge hailstorm [or] a very strong wind; they will be everywhere, like the water of a huge flood, and they will smash to the ground [the buildings in Samaria].
Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
3 The people of Samaria are proud, but everything that the drunks who live there think is wonderful/glorious will be trampled on by their enemies.
Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
4 [Yes], Samaria is beautiful, set on a hill above a fertile valley, but that beauty will disappear like [MET] a flower that wilts and dries up. Whenever someone sees a good fig at the beginning of the season [when figs become ripe], he quickly picks and eats it; [similarly, when the enemies of Israel see all the beautiful things in Samaria], [they will quickly conquer the city and take away all those things].
Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
5 At that time, the Commander of the armies of angels will be [like] a glorious wreath of flowers for [us] Israeli people who are still alive [after being exiled].
Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
6 He will cause our judges to want to do what is fair/just when they decide people’s cases. He will enable the soldiers who stand at the city gates to strongly defend [the city when our enemies attack it].
Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
7 [But now, ] our leaders stagger/stumble because they have drunk a lot of wine and [other] alcoholic drinks. The priests and prophets also stagger because of drinking a lot of wine and other alcoholic drinks. They are not able to think right; they see visions but they cannot understand what they mean; they are unable to decide things correctly.
Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
8 All their tables are covered with [their] vomit; filth is everywhere.
Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
9 They ridicule Yahweh saying, “Who does he think that he is teaching? Why is he talking to us like this? [Does he think that] we are little children who have recently been weaned?
Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 [He continually tells us], ‘Do this, do that;’ first he tells us one rule, then another rule, he tells us only one line at a time.”
Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
11 So now, Yahweh will need to force them to listen to [Assyrians] speaking to them in a language that they do not understand.
Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 Yahweh told his people [long ago], “[This is] a place where you can rest; you are exhausted [from all your travels through the desert], but you will be able to rest [in this land].” But they refused to pay attention to what he said.
anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
13 So Yahweh continues to tell the people of Samaria, one line at a time, “Do this, do that,” first one rule and then another rule. But because [of their ignoring what God said], they will be attacked and defeated; they will be wounded and snared and captured.
Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
14 Because of [what will happen in Samaria], you rulers in Jerusalem who make fun of me, listen to this message from Yahweh:
Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 You [boast] saying, “We have made an alliance with [the leaders of Egypt], so we will not be killed [in battles]; we will never go to the place where the dead people are. When the [army of Assyria] attacks us, they will never defeat us, because we have made [an agreement with Egypt] to protect us!” [But that agreement consists of] a lot of lies [DOU]. (Sheol )
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol )
16 Therefore, Yahweh [our] Lord says this: “Listen to this! I am going to place in Jerusalem [someone who is like] [MET] a foundation stone, [he is like] a stone that has been tested [to determine if it is solid]. [He will be like] a valuable cornerstone around which it will be safe to build a house; and whoever trusts in him will never be disappointed.
Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 I will test you [people of Jerusalem] to find out if you will act justly and righteously [like] [MET] someone uses a plumb line [to determine if a wall is straight and vertical]. But because your agreement [with Egypt] to protect you [was made by leaders] lying to each other and deceiving each other, you will be defeated and taken away [from your country] by [an army that will come against you like] [MET] a flood.
Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 I will annul/destroy the agreement that you made [with the leaders of Egypt]. You thought that [because of that agreement] you would not be killed, and you would not go to the place where the dead are. [But] when the vast [army of Assyria] overwhelms you like a flood, they will trample you into the ground. (Sheol )
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol )
19 Their soldiers will come during the morning, at noontime, and at night, and they will carry you all away.” And when you understand this message, you will be terrified.
Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
20 [You have heard people say], “Your bed is very short, you will not be able to sleep in it; your blankets are very narrow; they will not cover you!” [That means for you that your agreement with Egypt is not going to save you].
Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 Yahweh will come [and cause you to be defeated]; he will do to you like he did to the army of Philistia at Perizim Mountain and like he did to the Amor people-group at Gibeon Valley. What he will do will be [very] strange and unusual [DOU].
Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 The Commander of the armies of angels has told me that he is going to destroy the entire land. So do not ridicule [what I say any more], because if you do that he will punish you [even] more severely.
Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
23 Listen [IDM] to what I say; pay attention carefully.
Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 When a farmer plows some ground, does he never plant seeds [RHQ]? Does he continue to plow it and never plant anything [RHQ]?
Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 No, he makes the ground very level, and then he plants seeds— dill and cumin and wheat and barley. He plants each kind of seed in the correct manner.
Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 [He does that] because God has taught him the correct way to do it.
Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
27 [Farmers] never thresh caraway/dill with a heavy sledge/club; instead, they beat it only with a stick. [Farmers] never thresh cumin by driving a cart over it; instead, they hit it [only] with a rod.
Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 And grain for baking bread is crushed easily, so the farmers do not continue to pound it for a long time. They sometimes cause their horses to pull a cart over it [to thresh it], [but] doing that does not grind the grain.
Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 The Commander of the armies of angels gives [us] wonderful advice [about how to do things]; he causes [us] to be very wise. [So what the farmers do is very smart/wise, but what your leaders are doing is very stupid].
Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.