< Isaiah 21 >

1 [I received] this message [from Yahweh about Babylonia], [a land that is] near the [Persian] Gulf [but which will soon be] a desert. [An army] will soon come from the desert to invade that land; it is an army that causes its enemies to be terrified, an army that will come like a whirlwind from the south.
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 Yahweh showed me a terrifying vision. [In the vision I saw an army] that will betray/deceive people and steal their possessions [after they conquer them]. [Yahweh said], “You armies from Elam and Media, surround [Babylon] and prepare to attack it! I will cause the groaning [and suffering] that Babylon caused to cease!”
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 Because of that, my body is full of pain; my pain is like the pain that women who are giving birth experience. When I hear about and see [what God is planning to do], I am shocked.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 I cannot think straight/correctly, and I tremble. I was eager for it to be nighttime, but now it is night, and I am horrified.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 [In the vision I saw that the leaders of Babylonia] were preparing a great feast. They had spread rugs [for people to sit on]; everyone was eating and drinking. [But] they should get up and prepare their shields, [because they are about to be attacked]!
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 Then Yahweh said to me, “Put a watchman [on the wall of Jerusalem], and tell him to shout/proclaim what he sees.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 Tell him to watch for chariots pulled by pairs of horses, and [men riding] camels and donkeys, [coming from Babylon]. Tell the watchman to watch and listen carefully!”
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 [So I did that], and one day the watchman called out, “Day after day I have stood on this watchtower, and I have continued to watch during the day and during the night.
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 Now, I saw a man riding in a chariot pulled by two horses. [I called out to him], and he answered/shouted, ‘Babylon has been destroyed! All the idols in Babylon lie in pieces on the ground!’”
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 My people [in Judah], [the army of Babylon has caused] you to suffer greatly [as though] [MET] you were grain that was threshed and (winnowed/thrown up into the air for the wind to blow away the chaff). [But now] I have told you what the Commander of the armies of angels the God whom we Israelis [worship], told me [about Babylon].
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 [I received] this message [from Yahweh] about Edom: Someone from Edom has been calling/shouting to me saying, “Watchman, how long will it be before the night is ended? [DOU]”
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 [I], the watchman, replied, “It will [soon] be morning, but after that, it will [soon] be night again. If you want to inquire [again about what will happen in our country], come back and inquire again.”
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 [I received] this message about Arabia: Give this message to people traveling in caravans from Dedan [town in northwest Arabia], who camp in the scrub there. Tell them to bring water for those who are thirsty.
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 And you people who live in Tema [city in northwest Arabia], must bring food for the (refugees/people who are fleeing from their enemies).
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 They are fleeing in order not to be killed by [their enemies’] swords and not to be shot in battles by arrows.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 Yahweh said to me, “Exactly one year from now, all the greatness of the Kedar [area in Arabia] will end.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 Only a few of their soldiers who know well how to shoot arrows will remain alive. [That will surely happen] because [I], Yahweh, have said it.”
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.

< Isaiah 21 >