< Hosea 4 >

1 You Israeli people, listen to this message from Yahweh! He is accusing you people who live in this country, [saying] “The people are not faithfully [doing what pleases me], they are not kind [to others], and they do not [even] know me!
Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
2 Everywhere in this land they curse [others], they murder [others], they steal, and they commit adultery. They act violently toward others and commit one murder after another.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
3 It is because of their doing those things that there is no rain [MTY], the land has become dry, the people are mourning, and the people are dying [from hunger]. Even the wild animals and the birds and the fish in the sea are dying.
Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4 But no one should accuse someone else and say it is his fault. It is you priests whom I am accusing.
“Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
5 So I will punish [MTY] you priests, night and day, and I will punish the prophets with you. I am going to destroy [Israel, the nation that is like] [MET] a mother to you.
Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
6 It is because my people do not know [about me] that they will be destroyed. And their not knowing about me is because you priests have refused [to teach them about me]; so I will no longer allow you to be my priests. You have forgotten the things that I taught you, so I will forget [to bless] your children.
Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
7 As there are more and more priests, they have sinned against me more and more. So I will no longer allow them to be honored; instead, I will cause them to be disgraced.
Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8 The priests get food from [the offerings that the] people [bring in order to be forgiven for having sinned], [so] the priests want the people to sin more and more [in order that the people will bring them more and more offerings].
Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9 The priests [are as sinful] as the [other] people, and I will punish [all of] them for what they have done; I will pay them back for the [evil] things that they have done.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10 [The priests] will eat, but they will still be hungry; they will have sex with prostitutes, but they will not have any children, because they have abandoned [me], Yahweh,
“Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
11 and they are devoting themselves to sleeping with prostitutes, and to [drinking] old wine and new wine, which results in their not being able to think clearly.”
ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 “[You] my people request wooden idols [to tell you what you should do]! Like prostitutes who have left/abandoned their husbands,
za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 you have abandoned [me] your God, and you are chasing after [other gods] on the tops of hills and mountains; you burn incense under oak [trees], poplar [trees], and other trees where there is nice/pleasing shade. So your daughters have become prostitutes, and your daughters-in-law have committed adultery.
Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14 But it is not [only] your daughters [whom I will punish] for having become prostitutes, and it is not [only] your daughters-in-law whom I will punish for committing adultery, because the men also are having sex with prostitutes, and they offer sacrifices with the prostitutes [who search for men at the] shrines [of the idols]. [They are all] foolish people, and they will [all] be ruined.
“Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15 You Israeli [people] have abandoned me like [MET] those who commit adultery have abandoned their spouses. But do not cause [the people of] Judah to sin [also]. Do not go to Gilgal or go up to Beth-Aven [towns] [to worship idols there]. Do not make solemn promises [there, saying ‘Just as surely] as Yahweh lives, [I will do what I am promising].’
“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 You [people of Israel] are as stubborn as [SIM] a young cow. So there is no way [RHQ] that [I], Yahweh, will [provide food for them] [like a shepherd provides food for his] lambs [by leading them] to a nice meadow.
Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 The people of Israel have chosen to worship idols [MET], [so] allow them [to do what they want to do].
Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
18 When their rulers finish drinking [their wine], they go to find prostitutes; they love their disgraceful behavior.
Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 But they will disappear [as though] [MET] they were blown away by a whirlwind. They will become [very] ashamed because of their offering sacrifices [to idols].”
Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

< Hosea 4 >