< Hebrews 1 >

1 Long ago God communicated frequently to our ancestors in various ways by what the prophets [said and wrote].
Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri.
2 But now when this final age [is beginning], God has communicated to us [just once] by means of what (his Son/the man who was also God) [said and did. God] appointed him in order that he would possess everything [that truly belongs to God. God also appointed] him in order that he would create the universe. (aiōn g165)
Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. (aiōn g165)
3 He manifests God’s glory. He exactly represents [what God is like]. He (sustains everything by means of his powerful words. When he had [enabled people to be] freed from the [guilt of] their sins [MET], he sat down in heaven [EUP] [to rule] at the place of greatest honor [MTY] with God [MTY].
Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero.
4 By doing that, he [showed that he] was very much greater than the angels, to the extent that his relationship [MTY] [to God, as his Son], is more excellent than the relationship the angels [have to God].
Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.
5 [We know that] because [in the Scriptures] no one [RHQ] ever reported that God said to any angel [what he said to his Son], You [(sg)] are my Son! Today I have declared to all that I am your Father [DOU]! And he said in another Scripture passage, I will be his Father, and he will be my Son [DOU].
Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati, “Iwe ndiwe mwana wanga; Ine lero ndakhala Atate ako.” Kapena kunenanso kuti, “Ine ndidzakhala abambo ake; iye adzakhala mwana wanga.”
6 And [we know his Son is greater than the angels because in] another [Scripture passage someone wrote this about God’s esteemed Son], when God was about to send him into the world: All God’s angels must worship him.
Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati, “Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”
7 [And in the Scriptures it is written that] someone said this about the angels: [God] makes the [angels] who serve him [to be changeable like] [MET] winds and flames of fire.
Iye ponena za angelo akuti, “Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo, amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”
8 But on the other hand, [in the Scriptures it is written that God said] this to his Son: You [(sg)] who are [also] God will rule forever [MTY], and you will reign righteously over your kingdom [MTY]. (aiōn g165)
Koma za Mwana wake akuti, “Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya, ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu. (aiōn g165)
9 You have loved [people’s] righteous [deeds] and you have hated [people’s] lawless [deeds]. So I, your God, have caused you to be more joyful [MTY] than anyone else.
Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”
10 And [we also know that his Son is superior to angels because in the Scriptures the Psalmist wrote that] someone said to God’s Son, Lord, it was you who created the earth in the beginning. You also made [the rest of] the universe (OR, the [things in] the sky) [MTY].
Mulungu akutinso, “Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi; ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
11 Everything in the universe will disappear, but you will keep on living [forever]. They will wear out as clothing [wears out].
Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire. Izo zidzatha ngati zovala.
12 You will dispose of them as one rolls up an [old] coat [before getting rid of it]. [Then], you will exchange [everything that is in the universe for what is new], as someone puts on a new garment [in exchange for an old garment] [SIM]. But you [are not like what you created]; You stay the same, and you live forever [LIT]!
Mudzazipindapinda ngati chofunda; ndipo zidzasinthidwa ngati chovala. Koma Inu simudzasintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.”
13 [We also know that his Son is superior to angels because no one ever stated] [RHQ] [in the Scriptures] that God said to any angel [what he said to his Son], Sit [in the place of honor] next to me and rule with me [MTY] while I put all of your enemies completely under your control [MET]!
Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti, “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditapanga adani ako kukhale chopondapo mapazi ako.”
14 The angels are [only] spirits who serve [God] [RHQ]. [God] sends them [to earth] in order to help those he has saved (OR, those whom he will save).
Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

< Hebrews 1 >