< Hebrews 2 >
1 So, [since that is true], we must pay very careful attention to what we have heard [about God’s Son], in order that we do not drift away from it, [as a boat drifts off its course when people do not guide it] [MET].
Nʼchifukwa chake, ife tiyenera kusamalira kwambiri zimene tinamva, kuopa kuti pangʼono ndi pangʼono tingazitaye.
2 [God’s laws that] were given by angels were valid, and God justly punished all who rejected them and all who disobeyed [DOU] them.
Popeza uthenga umene unayankhulidwa kudzera mwa angelo unali okhazikika ndithu, choncho aliyense amene ananyozera ndi kusamvera analandira chilango choyenera.
3 So, we will certainly not escape [God punishing us] if we ignore such a great [message about how God] [MTY] saves us! [RHQ] This [new message] was first spoken by the Lord [Jesus] {The Lord [Jesus] first spoke this [message]}. Then it was confirmed to us by those who heard [what the Lord told them] {those who heard [what the Lord told them] confirmed it to us}.
Nanga ife tidzapulumuka bwanji tikapanda kusamala chipulumutso chachikulu chotere? Ambuye ndiye anayamba kuyankhula za chipulumutsochi, kenaka amenenso anamvawo anatitsimikizira.
4 God also confirmed to us [that this message was true] by [enabling believers to do] many things that showed God’s power, to do other miraculous things [DOU], and [to do other things] by the gifts that the Holy Spirit distributed to them according to what [God] desired.
Mulungu anachitiranso umboni pochita zizindikiro, zinthu zodabwitsa ndi zamphamvu zamitundumitundu ndi powapatsa mphatso za Mzimu Woyera monga mwachifuniro chake.
5 God has determined that the angels will not rule over everything. [Instead, he has determined that Christ] will rule in the new world that [God] will [create]. [That is the new world] about which I am writing.
Mulungu sanapereke kwa angelo ulamuliro wa dziko limene likubwerali, limene ife tikulinena.
6 Someone spoke to [God about this] somewhere [in the Scriptures], saying, (No one is worthy enough for you to think about him!/Who is [worthy enough] for you to think about him?) [RHQ] (No human is [worthy enough] for you to care for him!/Is any human [worthy enough] for you to care for him?) [RHQ]
Koma palipo pena pamene wina anachitira umboni kuti, “Kodi munthu ndani kuti muzimukumbukira, kapena mwana wa munthu kuti muzimusamalira?
7 [So it is surprising that] you have caused people to be for a little while inferior in rank to angels. You have greatly honored [DOU] them [MET], as [kings are honored with] a crown.
Munamuchepetsa pangʼono kusiyana ndi angelo; munamupatsa ulemerero ndi ulemu.
8 You have put everything under people’s control [MET]. God has determined that people will rule over absolutely everything [LIT]. But now, at this present time, we perceive that people do not yet have authority over everything.
Munamupatsa ulamuliro pa zinthu zonse.” Poyika zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, Mulungu sanasiye kanthu kamene sikali mu ulamuliro wake. Koma nthawi ino sitikuona zinthu pansi pa ulamuliro wake.
9 But we do know about Jesus, [who truly has authority over everything]! Hebrews 2:9b-13 Jesus, for a little while, became inferior [in rank] to angels in order to die on behalf of [MET] everyone. He became inferior when he suffered [and] died, as God kindly [planned]. But now he has been greatly [honored] [DOU] [by being] crowned [as kings are].
Koma tikuona Yesu, amene kwa kanthawi kochepa anamuchepetsa pangʼono kwa angelo, koma tsopano wavala ulemerero ndi ulemu chifukwa anamva zowawa za imfa, kuti mwachisomo cha Mulungu, Iye afere anthu onse.
10 It was fitting that [God] make [Jesus] (perfect/all that God intended him to be). God was enabling many people who would belong to him [MET] to share his glory. God [is the one who] created all things, and [he is the one] for whom all things [exist]. [He perfected Jesus] by causing him to suffer [and die]. [Jesus] is the one whom [God] uses to save people.
Mulungu amene analenga zinthu zonse ndipo zinthu zonse zilipo chifukwa cha Iye ndi mwa Iye, anachiona choyenera kubweretsa ana ake ambiri mu ulemerero. Kunali koyenera kudzera mʼnjira ya zowawa, kumusandutsa Yesu mtsogoleri wangwiro, woyenera kubweretsa chipulumutso chawo.
11 [Jesus] is the one who (makes people holy/sets people apart for God), and they all belong to God’s family. [As a result, Christ] gladly [LIT] proclaims them to be [like] his own brothers [and sisters].
Popeza iye amene ayeretsa ndi oyeresedwa onse ndi abanja limodzi. Nʼchifukwa chake Yesu sachita manyazi kuwatcha iwo abale ake.
12 [The Psalmist wrote what Christ said to God about us becoming] his brothers, in these words: I will proclaim to my brothers how awesome you are (OR, what you ([are like/have done])) [MTY]. I will sing praise to you in the presence of the congregation!
Iye akuti, “Ine ndidzawuza abale anga za dzina lanu. Ndidzakuyimbirani nyimbo zamatamando pamaso pa mpingo.”
13 And a prophet wrote [in] another [Scripture passage what Christ said about God], I will trust him. And in another [Scripture passage, Christ said about those who are like his] children, I and the ones that God has given me are here.
Ndiponso, “Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.” Ndiponso Iye akuti, “Ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Mulungu wandipatsa.”
14 So, since those [whom God calls his] children are all human beings [MTY], Jesus also became a human being [just like them]. The devil has the power to cause people [to be afraid] to die, but Christ became human in order that by his dying he might make the devil powerless.
Tsono popeza kuti anawo ndi anthu, okhala ndi mnofu ndi magazi, Yesu nayenso anakhala munthu ngati iwowo kuti kudzera mu imfa yake awononge Satana amene ali ndi mphamvu yodzetsa imfa.
15 [Jesus did that] to free all of us who are like slaves [MET] all the time we live, because we are [forced to] be afraid to die.
Pakuti ndi njira yokhayi imene Iye angamasule amene pa moyo wawo wonse anali ngati akapolo chifukwa choopa imfa.
16 Because [Jesus became a human being], it is not angels whom he wants to help. No, it is we who trust God as Abraham did whom he wants to help.
Pakuti tikudziwanso kuti sathandiza angelo, koma zidzukulu za Abrahamu.
17 So, [since he came to help humans, not angels], he had to be made exactly like [us whom he calls] his own brothers [and sisters]. He wants to be a Supreme Priest who [acts] mercifully [to all people] and who faithfully does what God wants, so that people who had sinned would be declared no longer guilty.
Chifukwa cha zimenezi, Iye anayenera kukhala wofanana ndi abale ake pa zonse, kuti akhale mkulu wa ansembe wachifundo ndi wokhulupirika potumikira Mulungu, kuti potero achotse machimo a anthu.
18 [Specifically], he is able to help those/us who are tempted [to sin]. He can do that because he suffered, and he was also tempted [to sin like we are tempted to sin].
Popeza Iye mwini anamva zowawa pamene anayesedwa, Iyeyo angathe kuthandiza amene akuyesedwanso.