+ Genesis 1 >
1 Long, long ago God created the heavens and the earth.
Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 When he began to create the earth, it was shapeless and completely desolate/chaotic. Darkness covered the deep water that surrounded the earth. And the Spirit of God was hovering over the water.
Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
3 God said, “I want light to shine!” And light shone.
Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
4 God was pleased with the light. Then he made the light to shine in some places, and in other places there was still darkness.
Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
5 He gave to the light the name ‘day’, and he gave to the darkness the name ‘night’. After that, there was an evening which was followed by a morning. He called that whole period of time ‘the first day’.
Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
6 Then God said, “I command that there be an empty space like a huge dome to separate the water that is above it from the water on the earth that is below it!”
Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
7 And that is what happened. God gave to the space the name ‘sky’.
Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
8 Then there was another evening, which was followed by another morning. He called that period of time ‘the second day’.
Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
9 Then God said, “I want the water that is below the sky to come together, and dry ground to appear and rise above the water.” And that is what happened.
Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
10 God gave to the ground the name ‘earth’, and he gave to the water that came together the name ‘oceans’. God was pleased with the earth and the oceans.
Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
11 Then God said, “I want the earth to produce plants, including plants that will produce seeds and trees that will produce fruit. Each kind of tree will bear its own kind of fruit.”
Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
12 Then plants grew on the earth; each kind of plant began to produce its own kind of seed.
Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
13 Then there was another evening which was followed by another morning. God called that period of time ‘the third day’.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
14 Then God said, “I want a sun, a moon, and many stars to shine in the sky. The sun will shine in the daytime and the moon and stars will shine during the nighttime. By the changes in their appearance they will indicate the various seasons (OR, the times for special celebrations), and will enable people to know when days and years begin.
Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
15 I want them also to be like lights in the sky that will shine on the earth.” And that is what happened.
zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
16 God made two of them that were like big lights. The bigger one, the sun, shines during the day and the smaller one, the moon, shines during the night. He also made the stars.
Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
17 God set all of them in the sky to shine on the earth,
Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
18 to rule the day and the night, and to separate the light of the daytime from the darkness of the nighttime. God was pleased with these things he had made.
kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
19 Then there was another evening which was followed by another morning. He called that period of time ‘the fourth day’.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
20 Then God said, “I want many creatures to live in all the oceans, and I also want birds to fly in the sky above the earth.”
Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
21 So God created huge sea creatures and every other kind of creature that moves in the water, and caused them to live in all the oceans. He also created many kinds of birds. God was pleased with all those creatures.
Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
22 God blessed them. He said, “Produce offspring and become very numerous. I want the creatures in the water to live in all the oceans, and birds also to become very numerous.” And that is what happened.
Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
23 Then there was another evening that was followed by another morning. He called that period of time ‘the fifth day’.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
24 Then God said, “I want various kinds of creatures to appear on the earth. There will be many kinds of (livestock/domestic animals), creatures that scurry across the ground, and large wild animals.” And that is what happened.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
25 God made all kinds of wild animals and (livestock/domestic animals) and all kinds of creatures that scurry across the ground. God was pleased with all these creatures.
Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
26 Then God said, “Now we will make human beings that will be like us in many ways. I want them to rule over the fish in the sea, over the birds, over all the (livestock/domestic animals), and over all the other creatures that scurry across the ground.”
Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
27 So God created human beings that were like him in many ways. He made them to be like himself. He created some to be male and some to be female.
Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
28 God blessed them, saying, “Produce many children, who will live all over the earth and rule over it. I want them to rule over the fish and the birds and over all creatures that scurry across the ground.”
Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
29 God said to the humans, “Listen! I have given you all the plants that produce seeds, all over the earth, and all the trees that have seeds in their fruit. All these things are for you to eat.
Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
30 I have given all the green plants to all the wild animals and to the birds and to all the creatures that scurry across the ground, to everything that breathes, for them to eat.” And that is what happened.
Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
31 God was pleased with everything that he had made. Truly, it was all very good. Then there was another evening, that was followed by another morning. He called that period of time ‘the sixth day’.
Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.