< Genesis 31 >
1 Someone told Jacob that Laban’s sons were complaining and saying, “Jacob has become very rich by taking everything [HYP] that belonged to our father.”
Yakobo anamva zimene ana aamuna a Labani ankanena kuti, “Yakobo watenga chilichonse cha abambo athu ndipo wapeza chuma chonsechi pogwiritsa ntchito chuma cha abambo athu.”
2 And Jacob noticed that Laban was not acting friendly toward him as he had done before.
Choncho Yakobo anaona kuti Labani sankamuonetsanso nkhope yabwino monga kale.
3 Then Yahweh said to Jacob, “Go back to your country and your relatives, and I will help you there.”
Pamenepo Yehova anati kwa Yakobo, “Bwerera ku dziko la makolo ako ndi kwa abale ako, ndipo Ine ndidzakhala nawe.”
4 So Jacob sent a message to Rachel and Leah, telling them to come out to the pastures where his flocks of sheep and goats were.
Choncho Yakobo anatumiza mawu kukayitana Rakele ndi Leya kuti abwere ku busa kumene ankaweta ziweto zake.
5 When they arrived, he said to them, “I see that your father does not act friendly toward me as he did previously. But God, whom my father worshiped, has helped me.
Iye anawawuza kuti, “Abambo anu sakundionetsanso nkhope yabwino monga kale, koma Mulungu wa makolo anga wakhala ali nane.
6 You two know that I have worked very hard for your father,
Inu mukudziwa kuti ndagwirira ntchito abambo anu ndi mphamvu zanga zonse,
7 but many times [HYP] he has cheated me by decreasing my wages. But God has not allowed him to harm me.
chonsecho abambo anu akhala akundinyenga posintha malipiro anga kakhumi konse. Komabe Mulungu sanalole kuti andichitire choyipa
8 When Laban said, ‘The speckled animals are the ones that I will give you to be your wages,’ then all the animals gave birth to young ones that were speckled. When he changed and said, ‘The ones that have black and white stripes on them will be your wages,’ then all the animals gave birth to young ones that were striped.
Pamene abambo anu anati, ‘Zamawangamawanga zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana amawangamawanga; ndipo pamene anati, ‘Zamichocholozi zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana a michocholozi.
9 In that way, God has taken away the livestock that belonged to your father and has given them to me.
Motero Mulungu walanda abambo anu ziweto zawo ndi kundipatsa.
10 “One time, when the animals were mating, I had a dream. In my dream I [looked up and was surprised to] see that some of the male goats that were mating with the female goats had black and white stripes on them, some were speckled, and some were spotted.
“Pa nthawi imene ziweto zimatenga mawere ndinalota maloto, ndipo ndinaona kuti atonde onse amene ankakwerawo anali amichocholozi, amawangamawanga kapena amathothomathotho
11 An angel who was sent by God said to me in the dream, ‘Jacob!’ I replied, ‘I am here!’
Kutulo komweko, mngelo wa Mulungu anati, ‘Yakobo.’ Ine ndinayankha, ‘Ee, Ambuye.’
12 He said to me, ‘Look up and you will see that all the male goats that are mating have black and white stripes on them, or are speckled or spotted. This is happening because I have seen all that Laban has done to you.
Ndipo iye anati, ‘Tayangʼana ndipo taona kuti atonde onse okwerana ndi ziweto ali amichocholozi, amawangamawanga kapena a mathothomathotho, popeza ndaona zonse zimene Labani wakhala akukuchitira.
13 I am God who appeared to you at Bethel, where you set up a stone to show that the place was holy, and you poured [olive] oil on the stone and made a solemn promise to me. So now leave this land immediately, and return to the land where you were born.’”
Ine ndine Mulungu amene ndinadza kwa iwe pa Beteli paja. Beteli ndi kumalo kuja kumene unayimika mwala ndi kuwudzoza mafuta, komanso kulumbira kwa Ine. Tsopano choka mʼdziko lino msanga ndi kubwerera ku dziko la kwanu.’”
14 Rachel and Leah replied, “Our father will not give us anything more when he dies [RHQ].
Pamenepo Rakele ndi Leya anayankha, “Kodi ngati ife tilinso ndi gawo ngati cholowa pa chuma cha abambo athu?
15 He treats us as though we were foreigners [RHQ]! [Your working for him all these years was like a payment] that you gave him as a price for us, but we will not inherit any of that money that he got as a price for us. He has spent it all!
Kodi abambo athu samationa ife ngati alendo? Iwo anatigulitsa ndi kuwononga ndalama zonse anazipeza pa ifezo.
16 Surely all of the wealth that God took away from our father belongs to us and to our children. So do whatever God has told you to do!”
Chuma chonse chimene Mulungu walanda abambo athu, ndi chathu ndi ana athu. Tsono inu chitani zimene Mulungu wakuwuzani.”
17 Then Jacob put his children and his wives on camels.
Pamenepo Yakobo anakonzeka nakweza ana ake ndi akazi ake pa ngamira,
18 He made all his livestock go ahead of him. Besides the livestock, he took along all the other things that he had acquired while living in Paddan-Aram. And they prepared to return to his father Isaac, in the Canaan region.
anakusa ziweto zake zonse patsogolo natenga katundu wake yense amene anamupeza ku Padanaramu, ndipo ananyamuka kupita ku Kanaani, ku dziko la abambo ake, Isake.
19 Before they left, while Laban was shearing his sheep, Rachel stole the [small wooden] idols [that were in her father’s tent].
Labani atachoka pa khomo kupita kukameta nkhosa, mʼmbuyomu Rakele anaba timafano ta milungu ta abambo ake.
20 Furthermore, Jacob deceived Laban, who belonged to the Aram people-group, by not telling him that they were planning to leave.
Komanso nthawi iyi nʼkuti Yakobo atamunamiza Labani Mwaramu posamuwuza zoona kuti afuna kuthawa.
21 So Jacob and his family fled with all their possessions, and they crossed the Euphrates River, and then started traveling south toward the hilly Gilead region.
Choncho anathawa ndi zonse anali nazo. Ananyamuka nawoloka mtsinje wa Yufurate kupita cha ku Giliyadi, dziko la mapiri.
22 On the third day after they left, someone told Laban that Jacob and his family had left.
Patapita masiku atatu, Labani anawuzidwa kuti Yakobo wathawa.
23 So he took some of his relatives with him and started to pursue Jacob. They continued walking for seven days.
Pomwepo anatengana ndi abale ake namulondola Yakobo kwa masiku asanu ndi awiri ndipo anakamupezera ku Giliyadi, dziko la mapiri.
24 Then God appeared to Laban in a dream at night, and said to him, “When you catch up to Jacob, be sure that you do not say anything at all [HYP] to him in an angry manner!”
Koma Mulungu anabwera kwa Labani, Mwaramu kutulo usiku nati kwa iye, “Samala kuti usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.”
25 The next day, by the time Laban caught up with Jacob, Jacob and his household had set up their tents in the hilly Gilead region. So Laban and his relatives set up their tents there, too.
Pamene Labani amamupeza Yakobo, nʼkuti Yakobo atamanga matenti ake ku mapiri a dziko la Giliyadi. Nayenso Labani ndi abale ake anamanga matenti awo komweko.
26 Then Laban went to Jacob and said to him, “Why have you done this? You have deceived me by carrying away my daughters as though you had captured them in a war [MTY]!
Tsono Labani anati kwa Yakobo, “Kodi ndakuchita chiyani kuti iwe undinamize ndi kutenga ana anga ngati anthu ogwidwa ku nkhondo?
27 Why did you run away and deceive me? Why did you not tell me that you were going to leave, so that we could have rejoiced and sung while people played music on tambourines and harps before I said ‘goodbye’ to you?
Chifukwa chiyani unandinamiza ndi kuthawa mozemba wosandiwuza? Ukanandiwuza, bwezi titatsanzikana mwa chisangalalo ndi kuyimba nyimbo ndi zisekese ndi azeze.
28 (You did not even let me kiss my grandchildren and my daughters goodbye before they left!/Why did you not allow me to kiss my grandchildren and daughters goodbye before they left?) [RHQ] What you have done was foolish!
Sunandilole kuti ndingopsompsona adzukulu anga ndi ana anga aakazi motsanzikana nawo. Unachita zopusa.
29 My relatives and I have the power to harm you, but last night the God whom your father worships said to me in a dream, ‘Be sure that you do not say anything at all to Jacob in an angry way.’
Ndili nayo mphamvu yakukuchita choyipa; koma usiku wapitawu, Mulungu wa abambo ako wandiwuza ine kuti, ‘Usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.’
30 Now, I know you have left because you long to go back home. But why did you steal my [wooden] idols?”
Ndikudziwa kuti unachoka chifukwa unapukwa kufuna kubwerera kwanu kwa abambo ako. Koma nʼchifukwa chiyani unaba milungu yanga?”
31 Jacob replied to Laban, saying, “I did not tell you that we were planning to leave, because I was afraid. I thought that [if I told you], you would forcefully take your daughters away from me.
Yakobo anayankha Labani kuti, “Ine ndinkaopa chifukwa ndinkaganiza kuti mukhoza kundilanda anawa.
32 But if you find anyone here who has your wooden idols, we will execute that person. While our relatives are watching, search for yourself to see if there is anything that belongs to you that is here with me. If you find anything, you can take it!” When Jacob said that, he did not know that Rachel had stolen the wooden idols.
Koma mukapeza wina aliyense ndi milungu yanu, ameneyo sakhala ndi moyo. Anthu onse akupenya, lozani chilichonse chanu chimene chili ndi ine, ndipo ngati muchipeze tengani. Koma Yakobo sankadziwa kuti Rakele anabadi milunguyo.”
33 Laban went into Jacob’s tent, and then into Leah’s tent, and then into the tents of the two female slaves and searched for the idols, but he did not find them. After he left their tents, he entered Rachel’s tent.
Choncho Labani analowadi mu tenti ya Yakobo, ya Leya ndi mʼmatenti a adzakazi awiri aja, koma sanapeze kalikonse. Atatuluka mu tenti ya Leya, analowa ya Rakele.
34 But Rachel had previously taken the idols and put them in the saddle of a camel, and she was sitting on the saddle. So when Laban searched all over for them inside Rachel’s tent, he did not find them.
Koma Rakele anatengadi milungu ija ndi kuyiika mʼkati mwa chokhalira cha pa ngamira, iye nʼkukhalapo. Choncho Labani anafunafuna mu tenti monse koma wosapeza kanthu.
35 Rachel said to her father, “Do not be angry with me, sir, but I cannot get up in your presence [to show respect for you], because I am having my monthly menstrual period. [EUP]” So when Laban searched some more, he did not find the [wooden] idols.
Rakele anati kwa abambo ake, “Pepanitu musandikwiyire mbuye wanga chifukwa choti sinditha kuyimirira pamaso panu chifukwa ndili kumwezi.” Choncho Labani anafunafuna koma sanayipeze milungu ija.
36 Then Jacob became angry. He rebuked Laban, saying, “What crime did I commit? For what sin that I committed have you pursued me?
Yakobo anapsa mtima nafunsa Labani mwaukali kuti, “Kodi ndalakwa chiyani? Ndi tchimo lanji limene ndachita kuti muchite kundisaka chonchi?
37 Now you have searched through all my possessions, and what did you find from all these possessions that belongs to you? Put it here in front of my relatives and your relatives, so that they can decide who is right, you or me!
Chifukwa chiyani mwafunyulula katundu wanga? Ndipo mwapeza chiyani cha inu pamenepa? Chimene mwapezapo chiyikeni poyera pamaso pa abale anu ndi anga kuti atiweruze.
38 I was with you for 20 years. In all that time, your sheep and goats have (not miscarried/always given birth to animals safely). I have not [killed and] eaten any rams from your flocks.
“Ndakhala nanu kwa zaka makumi awiri tsopano ndipo nkhosa ndi mbuzi zanu sizinapoloze, kapena ine kudyapo nkhosa za mʼkhola mwanu.
39 When one of your animals was attacked and mauled/killed by a wild animal, I did not bring it to you. I replaced the dead animal with a living one of my own animals. Whenever one of your animals was stolen, during the day or during the night, you demanded that I replace it with one of my own animals.
Chiweto chikakhadzulidwa ndi chirombo, sindinkabwera nacho kwa inu. Ineyo ndinkalipira. Inuyo munkandilipiritsa kalikonse kobedwa masana kapena usiku.
40 I suffered from the heat during the day and from the cold at night. I was often not even able to sleep [PRS]!
Moyo wanga unali wotere: Dzuwa limanditentha masana ndipo usiku ndimazunzika ndi kuzizira. Tulo sindimalipeza konse.
41 I lived in your household for 20 years. I worked for you for 14 years to buy your two daughters, and for six more years to buy some of your sheep and goats. During that time, you changed and reduced my wages many times [HYP].
Zinthu zinali chonchi kwa zaka makumi awiri zimene ndinali mʼnyumba mwanu. Ndinakugwirirani ntchito kwa zaka khumi ndi zinayi chifukwa cha ana anu aakazi awiri ndipo zaka zina zisanu ndi chimodzi chifukwa cha ziweto zanu, ndipo munandisinthira malipiro kakhumi konse.
42 If God, the one whom my grandfather Abraham worshiped and before whom my father Isaac trembled in fear, had not been with me and helped me, you would have sent me away (with nothing in my hands/owning nothing)! But God saw how much I was suffering and how hard I was working, so last night he told you that what you have done to me was wrong.”
Akanapanda kukhala nane Mulungu wa abambo anga, Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu amene Isake ankamuopa, mosakayika inu mukanandichotsa chimanjamanja. Koma Mulungu waona zovuta zanga ndi kulimbikira ntchito kwanga, ndipo usiku wapitawu anakudzudzulani.”
43 Laban replied, “These two women are my daughters, and their children are my grandchildren, and the animals are my animals. Everything you see here is mine [HYP]! But what can I do today to keep my daughters or the children they have given birth to [RHQ]?
Labani anayankha Yakobo nati, “Ana aakaziwa ndi anga, ana awo ndi anganso. Ziwetozi ndi zanga. Chilichonse ukuona apa ndi changa. Koma tsopano ndingachite chiyani ndi ana anga aakaziwa kapena ndi ana awo?
44 I cannot do anything in order to keep them, so hey, we should make a peace agreement, you and I, and do something that will remind us about our agreement.”
Tsono, tiye tichite pangano pakati pa iwe ndi ine, ndipo likhale mboni pakati pathu.”
45 So Jacob took a [large] stone and set it on its end.
Choncho Yakobo anayimiritsa mwala ngati chipilala.
46 Then Jacob said to his relatives, “You also gather some stones.” So they gathered some rocks and put them in a heap, and they ate some food there near the heap.
Nati kwa abale ake, “Tutani miyala ina.” Choncho anawunjika miyalayo, ndipo anadya chakudya atakhala pa mbali pa muluwo.
47 Laban gave the heap the Aramaic name Jegar-Sahadutha, [which means ‘rock-pile to remind us’, ] but Jacob gave the rock-pile the Hebrew name Galeed, [which has the same meaning].
Labani anawutcha muluwo Yegara-sahaduta, ndipo Yakobo anawutcha Galeeda.
48 Laban said to Jacob, “This pile of rocks we have put here today will help us to remember our agreement.” That is why Jacob called it Galeed.
Labani anati, “Mulu uwu ndi mboni pakati pa inu ndi ine lero.” Ndi chifukwa chake unatchedwa Galeeda.
49 They also named the place Mizpah, [which sounds like the Hebrew word that means ‘watchtower’, ] because Laban said, “We will ask Yahweh to watch you and me while we are separated from each other, [so that we do not try to harm each other].
Unatchedwanso Mizipa, chifukwa iye anati, “Yehova aonetsetsa kuti palibe mmodzi mwa ife adzaswe panganoli ngakhale titatalikirana.
50 If you mistreat my daughters, or if you take other women to be your wives, even if no one tells me about it, don’t forget that God sees what you and I are doing!”
Ngati ukazunza ana anga kapena kukwatira akazi enanso, ngakhale kuti palibe wina amene ali nafe pano, koma kumbukira kuti Mulungu ndiye mboni pakati pathu.”
51 Laban also said to Jacob, “You see this large stone and this pile of rocks that we have set up to be between us.
Labani anatinso kwa Yakobo, “Taona pano pali miyala ndi chipilala chimene ndayimika pakati pa iwe ndi ine.
52 Both this pile of rocks and this large stone will remind us, that I will not go past these rocks to harm you, and you will not go past these rocks to harm me.
Mulu wa miyala uwu ndi chipilalachi ndi mboni. Ine sindidzadutsa mulu wa miyalawu kudzalimbana ndi iwe. Iwenso usadzadutse mulu wa miyalawu kudzalimbana nane.
53 We will ask the God whom [your grandfather] Abraham and [his father] Nahor worshiped to punish [MTY] either one of us, [if we harm the other one].” So Jacob solemnly promised to do what they said in their peace agreement. And he asked God, the one before whom his father Isaac trembled, to listen to what they promised.
Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori ndiye adzatiweruze.” Choncho Yakobo analumbira mʼdzina la Mulungu amene Isake, abambo ake ankamuopa.
54 He offered a sacrifice to God there in the hilly area, and he invited his relatives to eat with him. After they had eaten, they slept there that night.
Yakobo anapereka nsembe pa phiri paja, ndipo anayitana abale ake kuti adzadye chakudya. Atadya chakudya anagona pa phiri pomwepo.
55 The next morning Laban kissed his grandchildren and his daughters [goodbye] and asked God to bless them. Then he [and his men] left them and returned home.
Mmamawa wake, Labani anapsompsona zidzukulu zake ndi ana ake nawadalitsa. Kenaka ananyamuka kubwerera ku mudzi.