< Genesis 17 >

1 When Abram was 99 years old, Yahweh appeared to him again and said to him, “I am God Almighty. I want you to live in a way that I will regard you as someone that cannot be criticized.
Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
2 If you do that, I will make an agreement with you in which I will promise to enable you to have very many descendants.” [MTY]
Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
3 Abram prostrated himself with his face on the ground. Then God said to him,
Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
4 “Listen to this agreement that I am making with you: People of many nations will be your descendants.
“Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
5 And no longer will your name be Abram. Instead, your name will be Abraham, [which means ‘father of many nations,’] because the people of many nations will descend from you.
Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
6 I will enable you to have very many descendants, and I will cause them to become great nations/people-groups, and some of your descendants will become kings.
Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
7 I will make this agreement between me and you and your descendants. It will be an everlasting agreement to be in effect for many generations. This agreement is that I will be your God, and the God of your descendants.
Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
8 I will give to you and to your descendants the land through which you are now traveling, all of the Canaan region. It will be an everlasting possession for your descendants, and I will be the God that they [will worship].”
Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
9 Then God said to Abraham, “Now you must obey [your part of] the agreement that I am making with you, and your descendants must also obey it, for all generations.
Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
10 This is the agreement that I am making, between myself and you and all your descendants: Every male among you must be circumcised.
Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
11 (Cutting the foreskins of/Circumcising) them will be the sign [that you have accepted] the agreement I am making with you.
Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
12 Every male child among you must be circumcised when he is eight days old, in all future generations. That includes baby boys in your household or those born from slaves that have been bought, and baby boys of foreigners who live among you but do not belong to your household.
Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
13 It does not matter whether their parents are members of your household or slaves that have been bought; they must all be circumcised. Your bodies will have this mark to show [you have accepted] this everlasting agreement I am making.
Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
14 You must expel from your community any male who has not been circumcised, because [by not being circumcised] that person has disobeyed my agreement.”
Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
15 God also said to Abraham, “As for Sarai, your wife, you must not call her Sarai any longer. [Since I changed your name, I will change her name also]. Her name will now be Sarah.
Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
16 I will bless her, and she will surely give birth to a son for you. And I will bless her so much that she will be the ancestor of people of many nations. Kings of some people-groups will be descended from her.”
Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
17 Abraham prostrated himself with his face on the ground [to show respect to God]. But then he laughed as he said to himself, “Can a man who is a 100 years old become a father of a son? And since Sarah is 90 years old, how can she bear a child?”
Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
18 Then Abraham said to God, “Perhaps you will let Ishmael receive your blessing [and inherit all I possess].”
Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
19 Then God replied, “[No!] Your wife Sarah will bear a son for you. You must name him Isaac. I will establish my agreement with him, one which will be an everlasting agreement for him and his descendants.
Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
20 As for Ishmael, I have heard what you asked me to do for him. I will bless him so that he also will have many descendants. Among his descendants will be rulers of twelve nations. And I will cause his [descendants] [MTY] to also become a great nation.
Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
21 But Isaac, the son whom Sarah will give birth to at this time next year, is the one with whom I will establish my agreement.”
Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
22 When God finished talking to Abraham, God disappeared from his sight.
Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
23 On that same day, Abraham took his son Ishmael and all the males that were in his household, including the sons of all the slaves he had bought, and circumcised them. He cut off their foreskins, just as God told him to do.
Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
24 Abraham was 99 years old when (he was circumcised/someone circumcised him),
Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
25 and Ishmael was thirteen years old when Abraham circumcised him.
ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
26 On that very day Abraham and his son, Ishmael were circumcised.
Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
27 And all the males in his household, the ones who had been born there and those who had been bought from foreigners, were also circumcised.
Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.

< Genesis 17 >