< Ezra 1 >

1 During the first year that Cyrus ruled [the] Persian [Empire], he did something that fulfilled what Jeremiah had prophesied. Yahweh motivated Cyrus to write this message, and then Cyrus sent this message throughout his empire:
Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
2 “I, King Cyrus, who rule [the] Persian [Empire], declare this: 'Yahweh, the God [who is in/rules] from heaven, has caused me to become the ruler of all the kingdoms [that I know about] on the earth. And he has appointed me [to enable his people] to build a temple for him in Jerusalem, in Judah [land].
Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
3 All you people who belong to God may go up to Jerusalem to rebuild this temple for Yahweh, the God who lives in Jerusalem, the God [who is worshiped by you] Israeli people. I desire/hope that your God will be with you [and help those who go there].
Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
4 Those people who are in places where Israelis are living, whose ancestors were exiled here, should contribute silver and gold to those who go. They should also give them supplies [that they will need for the journey to Jerusalem]. They should also give them some livestock, and gifts of money to help build the temple of God in Jerusalem.'”
Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
5 Then God motivated some of the priests and (Levites/men who did work in the temple) and some of the leaders of the tribes that were descended from Judah and Benjamin to return to Jerusalem. Those whom God motivated got ready to return to Jerusalem and build the temple for Yahweh there.
Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
6 All of their neighbors helped them by giving them things made of silver and things made of gold, and supplies for the journey, and livestock. They also gave them other valuable gifts, and also gave them money [to buy things for building the temple].
Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
7 King Cyrus brought out the valuable things that King Nebuchadnezzar’s [soldiers] had taken from the temple of Yahweh in Jerusalem and put in the temple of Nebuchadnezzar’s gods [in Babylon].
Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
8 Cyrus commanded Mithredath, the treasurer of [the] Persian [Empire], to count all these items and then give them to Sheshbazzar, the leader of [the group that was going to return to] Judah.
Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
9 This is a list of the items that Cyrus donated: 30 large gold dishes 1,000 large silver dishes 29 silver (censers/incense burning pans)
Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
10 30 gold bowls 410 silver bowls 1,000 other items.
timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
11 All together, there were 5,400 items made of silver or gold, that [were given to] Sheshbazzar [to] take with him when he and the others returned to Jerusalem.
Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.

< Ezra 1 >