< Ezekiel 39 >

1 [Yahweh said to me], “You human, prophesy about [more terrible things that will happen] to Gog, and say this [to him]: ‘Gog, I am opposed to you who rule Meshech and Tubal.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 I will turn you around and drag you [and your armies] from far north [of Israel] and send you to [fight on] the mountains in Israel.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 When you are there, I will snatch your bows from your left hands and cause your arrows to fall from your right hands.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 You and all the soldiers that are with you will die on the mountains in Israel. I will give your [corpses] to be food for the birds that eat [dead] flesh, and to the wild animals.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 You will die in the open fields. [That will surely happen because] I, Yahweh the Lord, [have said that it will happen].
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 I will cause [many] fires to burn in Magog and among [all] those who live safely in the areas along their coasts, and they will know that it is I, Yahweh, [who have the power to do what I say that I will do].
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 I will enable my Israeli people to know that I am holy. I will no longer allow people to damage my reputation, and [people in other] nations will know that I, Yahweh the Lord, am the Holy One in Israel.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 [I], Yahweh the Lord, declare that it will soon be the day that those things will happen. It will be the day that I have spoken [to you] about.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 At that time, those Israelis who live in the towns will go out and gather the weapons [from your dead soldiers], and use them to make fires [to cook their food]. They will burn the small and large shields, the bows and arrows, the war clubs, and spears. There will be enough weapons to use as firewood for seven years.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 They will not need to gather firewood in the fields or cut wood from trees in the forests, because those weapons will be all the firewood [that they will need]. And they will take valuable things from those who took valuable things from them, and steal things from people who stole things from them. [That is what I], Yahweh the Lord, declare [will happen].
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 At that time I will create a graveyard for you, Gog, [and your soldiers], in the valley east of the [Dead] Sea. That graveyard will block the road that travelers [usually walk on], because you, Gog and all [the soldiers] of your huge army will be buried there. [So] it will be named ‘the Valley of Gog’s Huge Army’.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 For seven months the people of Israel will be burying those corpses. [It will be necessary to bury all of them], in order that the land will not be (defiled/considered unacceptable to me) [because of any unburied corpses].
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 All the people of Israel will [do the work of] burying them. The day when I [win that victory] they will honor me.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 After those seven months are ended, the Israeli people will appoint men to go throughout the land to bury corpses, in order that the land will not remain defiled.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 When they go through the land, when one of them sees a human bone, he will set up a marker beside it. [When] the gravediggers [see the markers, they will pick up the bones] and bury them in the Valley of Gog’s Huge Army.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 There will be a city there named Hamonah, [which means ‘huge army’]. And by doing this [work of burying the corpses], they will (cleanse the land/cause the land to be acceptable to me again).’”
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 [Yahweh said to me], “You human, this is what [I], Yahweh the Lord, say: Summon every kind of bird and wild animal. Say to them, ‘Gather together from everywhere and come to the feast that Yahweh is preparing for you. [It will be] a great feast on the mountains in Israel. [There] you will eat [men’s] flesh and drink their blood.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 You will eat the flesh of strong soldiers and drink the blood of kings [as if they were] fat animals—rams and lambs, goats and bulls—from the Bashan [region].
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 At that feast that Yahweh is preparing for you, you will eat fat until your [stomachs] are full, and you will drink blood until [it is as though] you are drunk.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 [It will be as though] you are eating at a table that I [have set up for you. You will eat all you want of the flesh] of horses and their riders, strong soldiers [DOU] of every kind.’ [That is what I], Yahweh the Lord, declare.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 I will show [people of] many nations that I am glorious, and all those nations will see how I punish them [DOU].
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 After that time, the Israeli people will know that I, Yahweh their God, [have the power to do what I say that I will do].
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 And the [people of other] nations will know that the Israeli people had been forced to go to other countries because they sinned by not being faithful to me. I (turned away from/abandoned) them, and allowed their enemies to capture them [IDM], and many [HYP] of them were killed by [their enemies’] swords.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 I punished them like they deserved to be punished because of their disgusting behavior and sins, and I turned away from them [MTY].
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Therefore, this is [now] what I, Yahweh the Lord, say: I will now bring back from exile/Babylonia [the descendants of] Jacob; I will pity all the Israeli people, and I will [also] jealously protect my reputation.
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 When the Israeli people [are back in their own country, they will] live safely in their land, with no one to cause them to be afraid, but they will be ashamed when they think about the disgraceful and unfaithful things that they did [previously].
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 When I have brought them back from their enemies’ countries and gathered them together [in Israel], the people of many nations will know that I am holy.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 And the Israeli people will know that I, Yahweh their Lord, [have the power to do what I say that I will do]. They will know that because [even though] I forced them to go to [other] countries, I will gather them together in their own country. I will not leave any of them in those countries.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 I will no longer turn away from them; I will pour out my Spirit on the Israeli people. [That will surely happen because I], Yahweh, have said it.”
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 39 >