< Ezekiel 29 >
1 Almost ten [after we had been taken to Babylonia], on the twelfth day of the tenth [of that year], Yahweh gave me another message. [He said to me],
Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 “You human, turn toward Egypt and proclaim the terrible things that will happen to the king of Egypt and all his people.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake.
3 Give the king this message from [me], Yahweh the Lord: ‘You king of Egypt, I am your enemy; [you are like] [MET] a great monster/crocodile that lies in the [along the Nile River]. You say, “The Nile [River] is mine; I made it [for myself].”
Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto, iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako. Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinadzipangira ndekha.’
4 But [it will be as though] I will put hooks in your jaws and drag you out [from the river] onto the land, with fish sticking to your scales.
Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako. Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.
5 I will leave you and all those fish to die in the desert; you will fall onto the ground, and your [corpse] will not be picked up and buried, because I have declared that your flesh will be food for the wild animals and birds.
Ndidzakutaya ku chipululu, iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako. Udzagwera pamtetete kuthengo popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.
6 When that happens, all the people of Egypt will know that it is I, Yahweh, [who have the power to do what I say that I will do]. The Israeli people [trusted that you would help them]. But you have been [like] [MET] a reed pole in their hands.
Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli.
7 And when they leaned on that pole, it splintered and tore open their shoulders. When they leaned on you, [it was as though] you were a pole that broke, and as a result you wrenched their backs.
Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.
8 Therefore, this is what [I], Yahweh the Lord, say: “I will bring [your enemies to attack] you with their swords, and they will kill your people and your animals.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe.
9 Egypt will become an empty desert. Then the people of Egypt will know that I, Yahweh, [have the power to do what I say that I will do].” You [proudly] said, “The Nile [River] is mine; I made it!”
Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova. “‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’
10 Therefore I am opposed to you and your streams, and I will cause Egypt to be ruined, and cause it to be an empty desert, from Migdol [in the north] to Aswan [in the south], as far [south] as the border of Ethiopia.
nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi.
11 For 40 years no one will walk through that area, and no one will live there.
Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi.
12 Egypt will be barren/empty, and it will be surrounded by other desolate nations. The cities in Egypt will be empty and deserted for 40 years, surrounded by ruined cities in nearby nations. I will cause the people of Egypt to be scattered to countries [far away].
Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.
13 But this is what [I], Yahweh the Lord, [also] say: “At the end of 40 years, I will enable the people of Egypt to return home [again] from the nations to which they were scattered.
“‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako.
14 I will bring back the people of Egypt who had been captured, and I will enable them to live again in the Pathros area [in the south], where they lived previously. But Egypt will be a very unimportant [DOU] kingdom.
Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika.
15 It will be the least important of [all] the nations; it will never again be greater than the nearby countries. I will cause Egypt to be very weak, with the result that it will never again rule over other nations.
Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu.
16 [When that happens, the leaders of] Israel will no longer be tempted to ask Egypt to help them. Egypt will be punished, and that will cause the Israeli people to not forget that they previously sinned by trusting that Egypt could help them. And the people of Israel will know that I, Yahweh the Lord, [have the power to do what I say that I will do].” '”
Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’”
17 Almost twenty-seven years [after we had been taken to Babylonia], on the first day [of the new year], Yahweh gave me this message:
Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti:
18 “You human, the army of king Nebuchadnezzar of Babylon fought very hard against Tyre, with the result that their heads were rubbed bare and their shoulders became (raw/full of blisters). But Nebuchadnezzar and his army did not get any valuable things from Tyre to reward them for their hard work [to destroy Tyre].
“Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo.
19 Therefore, this is what [I], Yahweh the Lord, say: 'I will enable King Nebuchadnezzar’s army to conquer Egypt. They will carry away from there all the valuable things, in order that the king can give them to his soldiers.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo.
20 I will enable them to conquer Egypt as a reward for what they did [to Tyre], because [I], Yahweh say that [it was as though] his army was working for me, [doing what I wanted them to do, when they destroyed Tyre].
Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.
21 And some day Israel will become a glorious nation [MET] again. When that happens, I will cause the Israeli people to respect what you say [MTY]. And then they will know that [it has happened because] I, Yahweh, [have the power to do what I say that I will do].'”
“Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”