< Ezekiel 18 >

1 Yahweh gave me another message. [He said, ]
Yehova anandiyankhula nati:
2 “You people quote [RHQ] this proverb [and say that it is] about Israel: ‘Parents/People eat sour grapes, but it is their children who have a very sour taste in their mouths', [which means that you think that it is not fair for you to be punished for your ancestors’ sins].
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 But [I], Yahweh the Lord, declare that [as surely] as I am alive, you Israeli people will no longer quote that proverb.
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Everyone [who is alive] belongs to me. That includes children and their parents; they all belong to me. And it is those who sin who will [because of their sins].
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 [So, ] suppose there is a righteous person [always] does what is fair and right [DOU].
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 He does not [meat sacrificed to idols] on the hilltops, he does not request help from idols. He does not have sex with someone else’s wife or have sex with a woman during her monthly menstrual period.
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 He does not mistreat/oppress people; if [borrows money from him and gives him his cloak to guarantee that he will pay the money back], he always gives the cloak back to that [before the sun goes down]. He does not rob people. He gives food to hungry people. He gives clothing to people who need clothes.
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 When he lends money to people, he does not [do it just to] charge big interest. He does not do [SYN] things that are evil. He [always] decides things fairly.
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 He faithfully obeys all [DOU] my laws. That man is truly righteous; he will remain alive. [That is what I, ] Yahweh the Lord, promise.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 But suppose that man has a son who acts violently, who murders people and does any of these other things, even though his father has not done any of them:
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 He [meat sacrificed to idols] on the hilltops. He has sex with other people’s wives.
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 He mistreats/oppresses poor and needy people. He robs people. If someone gives him his cloak to [that he will pay the money back], he never gives the cloak back to [before the sun goes down]. He seeks help from idols. He does [other] detestable things.
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 When he lends money, he [very big] interest. If you think that such a person [be allowed to] remain alive [RHQ], you are certainly wrong. Because he has done those detestable things, he will surely be executed, and it will be his own fault [IDM].
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 But suppose that man has a son who sees all the sins that his father commits, but he does not do those things:
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 He does not [meat sacrificed to idols] on the hilltops. He does not request help from idols. He does not have sex with other people’s wives.
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 He does not mistreat/oppress people. If he lends money to someone, he does not require that person to give him his cloak to guarantee that he will pay the money back. He does not rob anyone. He gives food to those who need it. He gives clothes to those who need clothes.
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 He does not commit sins, [like his father did], and does not charge big interest [DOU] when he lends money. He faithfully obeys [all] [DOU] my laws. That person will not be executed for his father’s sins; he will surely remain alive.
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 But his father will be executed for the sins that he committed, because he cheated people and robbed people and did [other] things that are evil.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 [If] you ask, ‘Why should the [man’s] son not (suffer/be punished) for the evil things that his father did?’, [I will answer that] the son has done what is fair and right [DOU] and has obeyed all my laws, so he will surely remain alive.
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 It is those who sin who will [because of their sins]. People will not be punished for the sins of their parents, or for the sins of their children. Good/Righteous people will be rewarded for their being good/righteous, and evil people will be punished for [doing] evil.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 But if a wicked person (turns away from/quits) doing all the evil things that he did previously, and if he starts to obey faithfully all my laws, and does what is fair and right [DOU], he will surely remain alive; he will not be executed.
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 He will not be punished for the sins he committed [previously]. Because of the good/righteous things that he has done [since that time], he [be allowed to] remain alive.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 [I], Yahweh the Lord, declare that I certainly am not [RHQ] happy about wicked people dying. Instead, I am happy when they turn away from their wicked behavior, [because of that, they] remain alive.
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 But if a righteous person stops doing righteous things and [starts to] commit sins and does the same detestable things that wicked people do, he will certainly not [RHQ] [be allowed to] remain alive. I will not think about the righteous things that he did previously. Because he did not [do what pleases me], and because of [all] the sins that he has committed, he will be executed.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 But you say, ‘Yahweh does not act fairly!’ You Israeli people, listen to what I say: It is certainly not [RHQ] what I do that is unfair, it is what you continually do that is not fair/right!
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 If a righteous person (turns away from/quits) doing what is righteous and commits sins, he will [for committing those sins].
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 But if a wicked person turns away from doing wicked things and does what is just and right [DOU], he will save [from being executed/punished].
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 Because he has thought about all the evil things that he did and has turned away from doing them, he will [be allowed to] live. He will not be executed [for having done evil things].
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 But [you] Israeli people [MTY] say, ‘Yahweh does not act fairly.’ You people of Israel, my behavior is certainly not [RHQ] unfair! It is your behavior that is not right.
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 Therefore, you Israeli people [MTY], I, Yahweh the Lord, will judge each of you according to what you have done. Repent! Turn [away] from all your wicked behavior! Then you will not be destroyed [PRS] because of your sins.
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 Get rid of all your wicked behavior, and get a new way of thinking [IDM, DOU]. You Israeli people [MTY], (do you really want to be executed for your sins?/you act as though you want to be executed [for your sins]) [RHQ].
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 [I], Yahweh the Lord, declare that I am not pleased about your dying. So repent, and remain alive!”
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

< Ezekiel 18 >