< Ezekiel 17 >
1 Yahweh gave me another message. [He said, ]
Yehova anayankhula nane kuti,
2 “You human, tell this story/parable [DOU] to the people [MTY] of Israel.
“Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
3 [Say to them, ] ‘This is what Yahweh the Lord says: A huge eagle that had strong wings and long beautiful feathers of many colors flew to Lebanon. It grasped the top of a cedar [tree]
Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
4 and broke it off. Then the eagle carried it away to [Babylonia], a country that had many merchants/businessmen, and planted it in one of the cities there.
Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
5 Then that eagle took a seedling from [your] country and planted it in a fertile field. He planted it like people plant a willow tree, alongside [a stream that had] plenty of water.
“‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
6 It grew and became a low grapevine that spread [along the ground]. Its branches turned up towards the eagle, but its roots grew down into the ground. So it became a [good] vine and produced [lots of] branches and leaves.
Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
7 But there was another huge eagle that had strong wings and beautiful feathers. And [some of] the roots of the vine grew toward that eagle, and its branches [also] turned toward it, hoping that the eagle would bring more water to it.
“‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
8 [That happened in spite of the fact that] the vine had [already] been planted in good soil, where there was plenty of water, with the result that it had produced branches and produced grapes and had become a very healthy/productive vine.’
Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
9 Then [after you have told that to the people, say to them, ‘This is what Yahweh the Lord says: That vine] will certainly not [RHQ] remain healthy/productive. It will be [RHQ] pulled up by its roots by the eagle [that planted it], and all its fruit will be stripped off and its leaves will wither. And it will not need someone with strong arms or many people to pull it out by its roots.
“Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
10 Even if that vine is transplanted, it certainly will not continue to grow [RHQ]. When the hot wind from the east blows against it, it will completely wither, there where it was planted! [RHQ]’”
Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
11 Then Yahweh gave this message to me:
Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
12 “Ask these rebellious [Israeli] people, ‘Do you know what this parable/story means?’ Tell them that it signifies that the King of Babylon went to Jerusalem [with his army] and captured the King of Judah and his officials, and took them back to Babylon.
“Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
13 Then he took one of the king’s close relatives [and appointed him to be the king], and made an agreement with him, forcing him to solemnly promise [to remain loyal]. The King of Babylon also took to Babylon the other important citizens of Judah,
Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
14 in order that the kingdom of Judah would not be able to become powerful again. The King of Babylon intended that the kingdom [of Judah] would not continue to exist if the people did not obey that agreement [that he made with the King of Babylon].
kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
15 But the King of Judah rebelled against the King of Babylon by sending officials to Egypt to request from them horses and a large army [to fight against the army of Babylonia]. But the King of Judah will certainly not [RHQ] be sucessful. Rulers who [rebel like that and] and refuse to obey solemn agreements will never [RHQ] escape.
Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
16 [I], Yahweh the Lord, declare that [as surely] as I am alive, the King of Judah will die in Babylon, in the city where the King of Babylon appointed him to be the King [MTY] [of Judah]. He will die because he despised the solemn agreement and refused to do what he promised to do.
“‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
17 The King of Egypt with all his very huge army [DOU] will not [be able to] help the King of Judah: [The soldiers from Babylonia] will build ramps up against the walls of Jerusalem and set up devices to batter the walls. They will [enter Jerusalem and] kill many of its people.
Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
18 The King of Judah despised the solemn agreement by disregarding the treaty. Although he had solemnly promised to be under the control of the King of Babylon, [he sent officials to request help from Egypt]. Therefore he will not escape being punished [by the King of Babylon].
Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
19 Therefore this is what I, Yahweh the Lord, say: 'Just as surely as I am alive, I will cause the King of Judah to be punished [IDM] for ignoring the solemn agreement that he made [with the King of Babylon] and then refusing to obey it.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
20 [It will be as though] I will spread a net to capture him, and he will be caught in it. He will [be captured and] taken to Babylon and punished because he rebelled against me.
Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
21 Most [HYP] of his soldiers who try to escape will be killed by [their enemies’] swords, and those who survive will be scattered in all directions. Then you will know that I, Yahweh, [have the power to do what I say that I will do].'”
Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
22 This is [also] what Yahweh the Lord says: “[It will be as though] I will take a shoot from the top of a very tall cedar [tree] and plant it [DOU] in another place. I will plant it on a very high [DOU] mountain.
“‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
23 [It will be as though] I will plant it on a mountain in Israel, and it will grow and become a beautiful cedar [tree]. Many [HYP] kinds of birds will make their nests in the tree, and they will have shade in its branches.
Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
24 And [it will be as though] all the trees in the field will know that I, Yahweh, get rid of tall trees and make little ones grow. I cause [big] green trees to wither, and I cause dry trees to become green. I, Yahweh have said this, and I will [certainly] do what I have said that I will do.”
Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”