< Exodus 9 >
1 Then Yahweh said to Moses/me, “Go to the king and say to him, ‘This is what Yahweh, the God [we] Hebrews [worship], says: “Allow my people to go, in order that they may worship me.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao ndipo ukamuwuze kuti Yehova, Mulungu wa Ahebri akuti alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
2 If you still keep refusing to let them go [DOU],
Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,
3 I warn you that I will punish you with my power [MTY] by sending a terrible disease on all your animals—on your horses, donkeys, camels, on your cattle, and on your flocks [of sheep and goats].
dzanja la Yehova lidzakantha ziweto zako zimene zili ku munda, pamodzi ndi akavalo, abulu, ngamira, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi ndi mliri woopsa kwambiri.
4 But I, Yahweh, will distinguish between [what I do to] the animals that belong to the Israeli people and [what I do to] your animals. The result will be that no animal that belongs to the Israeli people will die.”’
Koma Yehova adzasiyanitsa pakati pa ziweto za Israeli ndi ziweto za Igupto, kotero kuti palibe chiweto nʼchimodzi chomwe cha Aisraeli chimene chidzafe.”
5 [Tell him that] I have determined/decided that tomorrow is the day that I will do this in this land.”
Yehova anayika nthawi ndipo anati, “Yehova adzachita zimenezi mmawa mʼdziko muno.”
6 The next day Yahweh did just what he said [that he would do]. A terrible disease afflicted all of the Egyptians’ animals, and many of them [HYP] died. But none of the Israeli people’s animals died.
Ndipo mmawa mwake Yehova anachitadi zimenezi. Ziweto zonse za Aigupto zinafa, koma palibe chiweto ndi chimodzi chomwe cha Aisraeli chomwe chinafa.
7 The king sent [men to investigate], and they were surprised [to see] that none of the Israeli people’s animals had died. But [after they reported that to] the king, he continued to be stubborn [IDM], and he did not let the [Israeli] people go.
Farao anatuma anthu kuti akafufuze ndipo anapeza kuti palibe chiweto chilichonse cha Aisraeli chomwe chinafa. Komabe mtima wake sunagonje ndipo iye sanalole kuti anthu apite.
8 Then Yahweh said to Aaron and Moses/me, “Take a few handfuls of ashes/soot from (a furnace/an oven where they burn lime), and let Moses throw them up into the air, in front of the king.
Kenaka Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Tapani phulusa la pa moto lodzaza dzanja ndipo Mose aliwaze mmwamba pamaso pa Farao.
9 The [ashes/soot] will spread all over the country of Egypt like fine dust. And the ashes/soot will cause boils to afflict both the Egyptian people and their animals, all over the land.”
Phulusalo lidzasanduka fumbi pa dziko lonse la Igupto. Tsono fumbilo lidzasanduka zithupsa zomaphulika nʼkukhala zilonda pa munthu aliyense ndi pa nyama zomwe mʼdziko lonse la Igupto.”
10 So they/we both got some ashes/soot and [went and] stood in front of the king. Moses/I threw the ashes/soot up into the air. The ashes/soot spread all over, causing boils to afflict the [Egyptian] people and their animals. All the boils became open sores.
Kotero anatenga phulusa la pa moto ndi kuyima pamaso pa Farao. Mose analiwaza mmwamba, ndipo panabuka zotupa zophulika zokha pa munthu aliyense ndi pa ziweto.
11 Even the men who worked magic had boils. The result was that [they were suffering so much that] they were not able to come to Moses/me, because the men who worked magic had boils just like all [the rest of] the Egyptian people.
Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse.
12 But Yahweh caused the king to [continue to] be stubborn [IDM]. He did not pay any attention to what they/we [said], just as Yahweh had told Moses/me [would happen].
Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo iye sanamvere Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
13 Then Yahweh said to Moses/me, “Get up early [tomorrow] morning. Go and stand in front of the king and tell him that Yahweh God, the one that the Hebrew people [worship], says this: ‘Let my people go, in order that they may worship me [in the desert].
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mawa mmawa upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso ndipo ukamuwuze kuti Yehova Mulungu wa Ahebri akuti ulole anthu anga apite kuti akandipembedze.
14 [If you do not let them go], this time I will [punish] with plagues [not only] your officials and the rest of your people, but I will punish you yourself [SYN], in order that you will know there is no [god] like me anywhere in the world.
Ngati suwalola, tsopano ndidzagwetsa miliri yanga yonse pa iwe ndi nduna zako ndiponso pa anthu ako, kuti udziwe kuti palibe wina wofanana nane pa dziko lonse lapansi.
15 By this time I could have used my power [MTY] to strike you and your people with terrible diseases that would have wiped you all from the earth.
Pakuti ndikanakhala nditatukula kale dzanja langa ndikupheratu iwe pamodzi ndi anthu ako onse pa dziko lapansi.
16 But I have let you live. The reason I have let you live is to show you my power, with the result that [people] all over the earth [HYP] will know how great I [MTY] am.
Koma ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga kwa iwe ndiponso kuti dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.
17 You are still acting proudly and refusing to let my people go.
Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.
18 So listen [to this]: About this time tomorrow I will cause very heavy hail to fall [in Egypt]. From the time Egypt first became [a country], there has never been a hailstorm [as bad as this one will be].
Nʼchifukwa chake mawa, nthawi ngati ino, ndidzagwetsa matalala amphamvu amene sanagwepo pa Igupto, kuyambira pachiyambi mpaka lero.
19 So you should send [a message to everyone] to put their cattle, and everything else that they own that is [out] in the fields, under shelters. The hail will fall on every person and every animal that is out in the fields and that is not put under a shelter, and they will all die.’” [So Moses/I did what Yahweh said].
Tsopano lamula kuti ziweto zanu zonse ndi zinthu zonse zomwe zili ku minda kuti zilowetsedwe mʼkhola, chifukwa matalala adzagwera munthu aliyense ndi chiweto chilichonse chimene sichidzalowetsedwa mʼkhola ndipo zimene zidzakhala zili ku munda zidzafa.”
20 Some of the king’s officials who heard what Yahweh had said became very afraid. So they put all their animals and their slaves under shelters.
Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.
21 But those who did not pay any attention to what Yahweh had said left their slaves and their animals in the fields.
Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.
22 Then Yahweh said to Moses/me, “Raise your hand up toward the sky, in order that hail will fall all over the land of Egypt—on the people and on their animals and on all the plants in the fields.”
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”
23 So Moses/I lifted his/my stick up toward the sky. And Yahweh sent down hail, all over the land of Egypt. There was also thunder and lightning.
Mose ataloza ndodo yake kumwamba, Yehova anatumiza mabingu ndi matalala ndi ziphaliwali zongʼanima pa nthaka. Kotero Yehova anagwetsa matalala pa dziko la Igupto.
24 While very heavy hail was falling, there was thunder, and lightning struck the ground. There had never been a hailstorm like that since Egypt first became a country.
Matalala anagwa ndipo ziphaliwali zinangʼanima. Inali mphepo ya mkuntho yoopsa kwambiri imene sinakhaleponso mʼdziko lonse la Igupto chiyambire pamene Aigupto anakhala mtundu woyima pa okha.
25 The hail struck everything that was in the fields all over Egypt—every person and every animal. The hail destroyed the plants in the fields and stripped [the leaves off] the trees.
Matalala anawononga dziko lonse la Igupto, munthu aliyense pamodzi ndi ziweto. Matalala aja anawononga zomera zonse za mʼmunda ndi kukhadzula mtengo uliwonse.
26 Only in the Goshen region, where the Israeli people were [living], was there no hail.
Ku malo kokhako kumene matalala sanafikeko ndi dera la Goseni kumene kunali Aisraeli.
27 Then the king sent [someone] to summon Aaron and Moses/me. [When they/we came to the king], he said to them/us, “This time [I admit that] I have sinned. What Yahweh [has done] is right, and what I and my people [have done] is wrong.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati kwa iwo, “Tsopano ndachimwa, Yehova ndi wolungama, ine ndi anthu anga ndife olakwa.
28 (Pray to/Plead with) Yahweh [to cause it to stop]! [We] cannot [endure any more] of this thunder and hail! I will let your people go; they do not have to stay [here in Egypt] any longer.”
Upemphere kwa Mulungu chifukwa mabingu ndi matalala atikwana. Ine ndidzakulolani kuti mupite. Simuyenera kukhalabe kuno.”
29 Moses/I replied, “As soon as I go out of this city, I will lift up my hands [and pray] to Yahweh. Then the thunder will cease, and no more hail [will fall]. [This will happen] in order that you will know that Yahweh, [not your gods], controls everything [that happens] on the earth.
Mose anayankha, “Ndikangotuluka mu mzinda muno, ine ndidzakweza manja anga kwa Yehova ndi kupemphera. Mabingu ndi matalalawa adzaleka ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova ndiye akulamulira dziko lapansi.
30 But as for you and your officials, I know that you do not yet fear Yahweh God.”
Koma ine ndikudziwa kuti inu ndi nduna zanu simukuopabe Yehova Mulungu.”
31 When the hail fell, the flax was ruined because the buds were forming, and the barley was ruined because its grain was ripe.
Thonje ndi barele zinawonongeka, popeza barele anali atakhwima ndi thonje linali ndi maluwa.
32 But none of the wheat crops was ruined, because their shoots were still very small.
Koma tirigu ndi mchewere sizinawonongeke chifukwa zimakhwima mochedwa.
33 So Moses/I left the king and went outside the city. He/I lifted up his/my hands toward Yahweh [and prayed]. Then the thunder and the hail stopped, and the rain also stopped falling on the land [of Egypt].
Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.
34 But when the king saw that the rain and the hail and the thunder had stopped, he sinned again. He and his officials continued to be stubborn [IDM].
Farao ataona kuti mvula, matalala ndi mabingu zaleka, anachimwanso. Iye ndi nduna zake anawumitsanso mitima yawo.
35 So, just as Yahweh had predicted by what he told Moses/me, the king did not allow the Israeli people to leave.
Choncho Farao sanalole kuti Aisraeli apite monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.