< Exodus 8 >
1 Then Yahweh said to Moses/me, “Go back to the king and tell him, ‘Yahweh says that you must let my people go, in order that they can worship me [in the desert].
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 But if you refuse to let them go, I will punish you by sending frogs to cover your country.
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 [Not only] will the Nile [River] be full of frogs, [but] the frogs will come up [out of the river] into your palace. They will come into your bedroom and onto your bed. They will be in the houses of your officials and all [the rest of] your people. They will even get into your ovens and your pans for mixing the materials for baking bread.
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 The frogs will jump up on you and your officials and [all the rest of] your people.’”
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 Yahweh [also] said to Moses/me, “Say this to Aaron: ‘Hold your stick in your hand and stretch it out [as though you were stretching it] over the river, the canals, and over the pools, and cause frogs to come up [from all this water and] cover the land of Egypt.’”
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 [After Moses/I told that to] Aaron, he stretched out his hand [as though he were stretching it] over all the water in Egypt. And the frogs came up [from the water and] covered Egypt.
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 But the men who performed magic did the same thing, and they caused [more] frogs to come up [from the water onto the land].
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Then the king summoned Moses/me and said, “Ask Yahweh to take away these frogs from me and my people. After that happens, I will allow your people to go, in order that they can offer sacrifices to Yahweh.”
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 Moses/I said to the king, “I will be glad to pray for you and for your officials and for [the rest of] your people. [I will ask Yahweh] to get rid of the frogs from all your houses. The only frogs left will be [those] in the Nile [River]. Just tell me when I should pray.”
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 He replied, “Tomorrow.” So Moses/I said, “[I will do] what you say, and then you will know that Yahweh God, the one we [worship, is the only true god], and that there is no other god like him.
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 The frogs will leave you and your officials and all [the rest of] your people. The only ones left will be in the Nile [River].”
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 Aaron and Moses/I left the king. Then Moses/I prayed to Yahweh, [asking him to take away] all the frogs he had [brought to the king’s land].
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 And Yahweh did just what Moses/I [asked him to do]. As a result, all the frogs in the houses, in their courtyards, and in the fields died.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 The people gathered together all the dead frogs into big piles, and the land stank [from the smell].
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 But when the king saw that [the problem] was ended, he became stubborn [IDM] [again]. And just as Yahweh had predicted, he would not pay attention to what Aaron and Moses/we told him.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 Then Yahweh said to Moses/me, “Tell Aaron to strike the ground with his stick. [When he does that], all the fine particles of ground/dust will become gnats, all over the land of Egypt.”
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 So they/we did that. Aaron struck the ground with his stick, and all over Egypt, the fine particles of ground/dirt became gnats. The gnats covered the people and all [their] animals.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 The men who worked magic tried to cause gnats to appear, but they were unable to do it. So the gnats [stayed] on the Egyptian people and on their animals.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 The men who worked magic said to the king, “It is God who has done this with his power [MTY]!” But the king continued to be stubborn [IDM], and he would not pay attention to us, just as Yahweh had predicted.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 Then Yahweh said to Moses/me, “Get up early [tomorrow] morning. [Go down] to the river and wait for the king. [When he comes to bathe] [MTY], say to him, ‘This is what Yahweh says to you: “Let my people go, in order that they may worship me [in the desert].
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 [I warn you that] if you do not let my people go, I will send swarms of flies to you. They will come down on you and on your officials and on [the rest of] your people. The houses of all you Egyptians will be full of flies. They will [even] cover the ground.
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 But when that happens, I will treat the Goshen region, where my people live, differently. There will be no swarms of flies there. In that way, you will know that I, Yahweh, am doing these things [here] in this land.
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 I will distinguish clearly between [how I act toward] my people and [how I act toward] your people. And this plague is going to happen tomorrow!”’”
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 [Early the next morning, Moses/I told that to the king, but the king would not pay any attention]. So Yahweh did what he said he would do. He sent great swarms of flies into the palace of the king and into the houses of his officials. The whole country of Egypt was ruined by the flies.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 Then the king summoned Aaron and Moses/me and said, “You Israeli people can go and offer sacrifices to your god, [but you must do it] here in [this] land.”
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 But Moses/I replied, “It would not be right [for us] to do that, because we will be offering sacrifices that are very offensive to the Egyptian people. If we offer sacrifices that the Egyptian people think are disgusting, they will kill us by throwing stones at us [RHQ]!
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 No, we need to travel for three days into the desert. There we will offer sacrifices to Yahweh, the God we worship, just as he commands (OR, has commanded) us.”
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 So the king said, “I will let your people go to offer sacrifices to Yahweh, your god, in the desert. But you must not go very far. [Now] pray for me!”
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 Moses/I said, “Listen [to me]! After I leave you, I will pray to Yahweh, [asking] that tomorrow [he will cause] the swarms of flies to leave you and your officials and [the rest of] your people. But do not deceive us again by refusing to let our people go to offer sacrifices to Yahweh!”
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 Then Moses/I left the king and prayed to Yahweh.
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 And Yahweh did what Moses/I asked, and he got rid of the swarms of flies from [around] the king and his officials and [the rest of] his people. No flies remained.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 But the king was stubborn [IDM] this time also, and he did not allow the Israeli people to go.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.