< Exodus 2 >
1 (There was a man who/My father) was descended from [Jacob’s son] Levi. He married a woman who was [also] descended from Levi.
Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
2 She became pregnant and gave birth to (a baby boy/me). When she saw that he/I was a good-looking baby, she hid him/me for three months, [because she was not willing to do what the king commanded].
Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
3 When she was unable to (hide him/me/keep it a secret) any longer, she got a basket made from tall reeds. She covered the basket with tar ([to make it waterproof/so water could not get in]). Then she put him/me in the basket and put the basket in [the water] in the middle of the tall grass at the edge of the Nile [River].
Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
4 His/My older sister was standing not far away, [watching to see] what would happen to him/me.
Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
5 [Soon] the king’s daughter went down to the river to bathe. Her female servants were walking along the riverbank. She saw the basket amid the tall grass [in the river]. So she sent [one of] her servants to get it.
Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
6 When [the servant brought the basket to her], she opened it, and was surprised to see (a baby that was/me), crying. She felt sorry for him/me, and said, “This [must] be one of the Hebrews’ babies.”
Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
7 Then (the baby’s/my) [older] sister [approached] the king’s daughter and said, “Do you want me to go and find someone from among the Hebrew women who will [be able to] nurse the baby for you?”
Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
8 The king’s daughter said to her, “[Yes], go [and find one].” So the girl went and summoned (the baby’s/my) mother.
Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
9 The king’s daughter said to her, “[Please] take this baby and nurse him for me. I will pay you [for doing that].” So (the woman/my mother) took him/me and nursed him/me.
Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
10 ([A few years later]/when (the child/I) grew [older]), she brought him/me to the king’s daughter. She adopted him/me [as though I was] her own son. She named him/me Moses, [which sounds like the Hebrew words ‘pull out’], because she said “I pulled him out of the water.”
Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
11 One day, after Moses/I had grown up, he/I went out [of the palace area] to see his/my people, [the Hebrews]. He/I saw how they were being [forced to work] very hard. He/I [also] saw an Egyptian [man] beating one of his/my Hebrew people.
Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
12 He/I looked around [to see if anyone was watching]. Seeing no one, he/I killed the Egyptian man and buried his [body] in the sand.
Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
13 The next day he/I returned [to the same place]. He/I was surprised to see two Hebrew men who were fighting [each other]. He/I said to the man who started the fight, “Why are you (you should not be) striking your fellow [Hebrew].”
Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
14 The man replied, “(Who made you our ruler and judge?/No one made you our ruler and judge!) [RHQ] [You have no right to interfere with us] Are you going to kill me just like you killed that Egyptian man [yesterday]?” Then Moses/I was afraid, [because] he/I thought, “[Since that man knows what I did], surely [other people] know, [too].”
Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
15 [And that was correct]. The king heard about what he/I had done [to that Egyptian. So he ordered his soldiers to] execute/kill Moses/me. But he/I fled from the king [and left Egypt. He/I traveled east to] the Midian [region] and started to live there.
Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
16 The man who was the (priest/one who offered the people’s gifts to God) for the Midian people, [whose name was Jethro], had seven daughters. [One day] as Moses/I sat down beside a well, those girls came [to the well] and got water, and filled the troughs in order to give water to their father’s flock [of sheep].
Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
17 Some (shepherds/men who took care of other sheep) came and started to chase away the girls. But Moses/I helped/rescued the girls, and got water for their sheep.
Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
18 When the girls returned to their father [Jethro], [whose other name is] Reuel, he asked them, “How is it that you were able to [give water to the sheep and] come home so quickly today?”
Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
19 They replied, “A man from Egypt kept [MTY] other shepherds from sending us away. He also got water for us [from the well] and gave water to the flock [of sheep].”
Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
20 He said to his daughters, “Where is he? (Why did you leave him [out there]?/You should not leave him [out there]!) [RHQ] Invite him [in], so he can have something to eat [MTY]!”
Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
21 [So they did], and Moses/I [accepted and ate with them]. And Moses/I decided to live there. Later Jethro gave him/me his daughter Zipporah [to be his/my wife].
Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
22 Later she gave birth to a son, and Moses/I named him Gershom, [which sounds like the Hebrew words that mean ‘foreigner’], because he/I said, “I am living as a foreigner in [this] land.”
Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
23 Many years later the king of Egypt died. The Israeli people [in Egypt] were still groaning because of the [hard work they had to do as] slaves. They called out for [someone to] help them, and God heard them call out [PRS].
Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
24 He heard them groaning. And he (thought about/did not forget) that he had solemnly promised to Abraham, Isaac, and Jacob [to bless their descendants].
Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
25 God saw how the Israeli people were [being badly treated], and he was concerned about them.
Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.