< Ecclesiastes 8 >
1 [I will tell you about] those who are truly wise [RHQ] with the result that they can explain why everything happens. Being wise enables people to be happy [MTY] and enables them to smile.
Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
2 You solemnly promised God that you would obey what the king commands, so do that.
Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
3 Do not quickly disobey the king. And do not join those who want to rebel against him, because the king will do what he wants to do.
Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
4 We need to obey what the king says more than we need to obey what anyone else says; no one can say to the king, “(Why are you doing that?/You should not be doing that.) [RHQ]”
Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
5 If you obey what the king commands, he will not harm you. [So] be wise, and know the correct/right time to do things and the right way to do them.
Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
6 Although people experience many troubles/difficulties, there is a right/correct time to do things, and there is a right/correct way [to do them].
Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
7 No one knows what will happen in the future, so there is no one [RHQ] who can tell us what is going to happen.
Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
8 We cannot control the wind, and we cannot control when we will die. Soldiers are not permitted to go home during a battle, and evil people will not be saved by [doing what is] evil.
Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
9 I thought about all those things, and I thought about all [HYP] the other things that happen on this earth. I saw that [sometimes] people cause those whom they control to suffer.
Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
10 I also saw that [sometimes] after evil [people] die, they are highly honored at their funerals by the people in the cities where they had done [evil] deeds. It seemed to be difficult to understand why that happens.
Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
11 If evil people are not immediately punished, it causes [other] people [SYN] to [also] want to do evil things.
Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
12 But even if sinful people commit 100 crimes, and [even if they] live for a long time, I know that things will go better for those who greatly respect and revere God.
Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
13 [I also know] that things will not go well go for those who are evil, because they do not revere God. Shadows [do not last a long time]. Similarly [SIM], evil people will not live a long time.
Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
14 Another thing that [sometimes] happens on this earth is that bad things happen to righteous people, and good things happen to evil people. It is difficult to understand why that happens.
Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
15 [So] I decided that I would recommend that people be happy while they are alive, because the best thing that people can do here on this earth is to eat and drink and be happy. Enjoying doing those things will help people while they do their work, all the time that God has given to them to remain alive here on the earth.
Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
16 I thought about being wise and about people who work very hard, working day and night and not taking time to sleep.
Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
17 Then I thought about everything [HYP] that God has done, and I realized that no one can understand everything that happens here on this earth. Truly, people are not able to fully understand everything [that God understands], even if they try hard to do that. Even if wise people claim that they understand it all, they cannot.
pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.