< Deuteronomy 8 >

1 “You must faithfully obey all the commandments that I am giving you today. If you do that, you will live [a long time], you will become very numerous, and you will occupy the land that Yahweh solemnly promised your ancestors that he would give [to you].
Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
2 And do not forget how Yahweh our God led us as we traveled through the desert during these past 40 years. He [caused you to have many problems/difficulties], because he wanted to cause you to realize that you needed to trust him and not yourselves. And he wanted to test you, to find out what you intended to do [IDM], whether you would obey his commandments or not.
Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
3 So he caused you to have/experience difficulties. He allowed you to become hungry. Then he gave you manna [food from heaven], food that you and your ancestors had never eaten before. He did that to teach you that people need food [for their bodies]; but [they also need food for their spirits, which comes from paying attention to] everything that Yahweh says [MTY].
Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
4 During those 40 years [of walking through the desert], our clothes did not wear out and our feet did not swell [from walking a very long way through the desert].
Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
5 Do not forget that Yahweh our God disciplines us, like parents discipline their children.
Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
6 “Do obey the commandments of Yahweh our God, and conduct your lives as he wants you to do, and revere him.
Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
7 He is about to bring you into a good/fertile land, which has streams which flow down from the hills and pour/flow out of springs in the valleys.
Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
8 It is a land on which wheat and barley grow, a land where there are fig trees and pomegranates, and a land where there are olive trees and honey.
dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
9 It is a land where there will be plenty of food for you, where you will (not lack anything/have everything that you need) [LIT], a land which has iron [ore] in its rocks and from which you can dig copper [ore] from its hills.
dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
10 [Every day] you will eat until your stomachs are full, and you will thank Yahweh our God for the fertile/good land that he has given you.
Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
11 But, [when that happens], be sure not to forget Yahweh our God by disobeying his commandments and rules and regulations that I am giving to you today.
Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
12 When your stomachs are full [every day], and when you have built good houses and are living in them,
kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
13 and when the number of your cattle and sheep has greatly increased, and when you have accumulated a large amount of silver and gold, and the amount of all your other possessions has greatly increased,
ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
14 be sure that you do not become proud [IDM] and forget Yahweh our God, who rescued your ancestors from being slaves in Egypt and brought them out from there.
mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
15 Do not forget that he led them [while they traveled] through that huge and terrible desert, where there were poisonous snakes and scorpions. And do not forget that where the ground was very dry and there was no water, he caused water to flow for them out of (solid/very hard) rock.
Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
16 Do not forget that in that desert he gave your ancestors manna to eat, food that they had never eaten before. He [caused them to have/experience many problems/difficulties], because he wanted them to realize that they needed to trust him and not themselves. And he wanted to test them, to find out whether they intended to obey him, in order that when [those difficulties] ended, he would do many good things for them.
Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
17 Be sure that you do not think to yourselves, ‘I have acquired all these things by my own power [MTY] and ability.’
Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
18 Do not forget that it is Yahweh our God who has enabled you to become rich. He does this because he faithfully does what he solemnly promised our ancestors that he would do.
Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
19 “solemnly warn you that if you forget Yahweh our God and turn to other gods and start to serve them and worship them, you will certainly be destroyed.
Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
20 If you do not obey Yahweh our God, he will certainly destroy you just like he will destroy the people-groups that you will fight against.”
Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.

< Deuteronomy 8 >