< Deuteronomy 4 >

1 “Now, you Israeli people, obey all the rules and regulations [DOU] that I will teach you. If you do that, you will remain alive and you will enter and occupy/capture the land that Yahweh, the God whom your ancestors [worshiped], is giving to you.
Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
2 Do not add anything to what I command you, and do not take anything away from what I tell you. Obey all the commands of Yahweh our God that I am giving to you.
Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
3 “You have seen what Yahweh did at Baal-Peor [Mountain]. He got rid of all the people who worshiped [the god] Baal there,
Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
4 but you who faithfully [continued to worship] Yahweh our God are still alive today.
Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
5 “Note that I have taught you all the rules and regulations, just like Yahweh our God told me to do. He wants you to obey them [when you are living] in the land that you are about to enter and occupy.
Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
6 Obey them faithfully because, [if you do that], you will show the people of other nations that you are very wise. When they hear about all these laws, they will say, ‘The people of this great nation [of Israel] are certainly very wise [DOU]!’
Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
7 Even if other nations are great, there is none [RHQ] of them that has a god who is as near to them as Yahweh our God is to us! Whenever we call out to him [to help us, he answers/helps us]
Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
8 And there is no [RHQ] other nation, even if it is a great nation, that has laws that are as just/fair as the laws that I am telling to you today.
Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
9 “But be very careful! [DOU, IDM] Do not forget what you [SYN] have seen [God do]. Remember those things as long as you are alive. Tell them to your children and your grandchildren.
Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
10 Tell them about the day that your ancestors stood in the presence of Yahweh our God at Sinai [Mountain], when he said to me, ‘Gather the people together, in order that they can hear what I say. I want them to learn to have an awesome respect for me as long as they are alive, and I want them to teach their children to do that also.’
Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
11 [Tell them that] your ancestors came near the bottom of the mountain, while the mountain burned with a fire that went up to the sky, and the mountain was covered with dark clouds and black [smoke].
Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
12 Then Yahweh spoke to your ancestors out of the middle of the fire. Your ancestors heard him speak, but they did not see him. They only heard his voice.
Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
13 And he declared to them his agreement. That agreement contained the Ten Commandments that he wants you to obey. He wrote those on two stone tablets.
Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
14 Yahweh commanded me to teach all the rules and regulations to you, in order that you would obey them in the land that you are about to enter and occupy.”
Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
15 “On the day that Yahweh spoke to your ancestors at Sinai [Mountain], he was invisible. So, be careful
Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
16 that you do not sin by making for yourselves any idol [of something that can be seen!] not make an idol that resembles any person, either a man or a woman,
kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
17 or that resembles any animal or any bird
kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
18 or any (reptile/creature that scurries across the ground) or any fish in the deep ocean.
Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
19 And be careful to not look up toward the sky and be tempted to worship anything that you see there—the sun or the moon or the stars. Yahweh our God has given those to [be a blessing to] all people everywhere, [but you must not worship them].
Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
20 Yahweh has brought your ancestors out of Egypt, where [they were suffering as though] they were in a blazing furnace, in order that they would be people who belong to him, which is what you are today.
Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
21 “But Yahweh was angry with me because of [what] your ancestors [made me do]. He vowed that I would not cross the Jordan [River] to enter the good/fertile land that he is giving to you.
Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
22 He said that I must die here in this land and never cross the Jordan [River]. But you will go across it, and you will occupy that land.
Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
23 Be sure that you do not forget the agreement that Yahweh our God made with you. He commanded you to not make any kind of idol, because he has forbidden that.
Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
24 [You must not do that] because Yahweh your God will destroy [anyone who worships idols, ] like [MET] a fire completely destroys things. He [wants people to worship only him, he] (cannot accept/will punish) people who worship anyone or anything else.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
25 “When you have been in the land [of Canaan] for a long time and you have children and grandchildren, do not sin by making an idol that represents anything at all, because Yahweh says that is evil, and if you do that, you will cause him to become angry with you [and punish you].
Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
26 Today I am requesting everyone who is in heaven and everyone who is on the earth [MTY] to watch what you are doing. [If you disobey what I am telling you], you will soon all die in the land that you will be crossing the Jordan [River] to occupy. You will not live very long there; Yahweh will completely get rid of many [HYP] of you.
ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
27 And [the rest of you], Yahweh will force you to go and live among the people of many other nations. Only a few of you will (survive/remain alive) there.
Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
28 When you are in those nations, you will worship gods that are made of wood and stone, gods made by humans, gods that cannot see anything or hear anything or eat anything or smell anything.
Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
29 But while you are there, if you will try to know Yahweh your God, and if you try with your entire inner being to know him, he will (answer/reveal himself to) you.
Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
30 In the future, after you have been mistreated there and all those bad things happen to you, you will again worship only Yahweh and obey him.
Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
31 Yahweh is a God who acts mercifully. [If you continue to obey him], he will not abandon you or destroy you or forget the agreement that he solemnly made with your ancestors.”
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
32 “Now think about the past, about the time before you were born, about all the time since God first created people here on the earth. You could search everywhere, in heaven and on the earth. (Has anything like this ever happened that is as great as [what Yahweh did for the Israeli people]?/Certainly nothing has ever happened that is as great [as what Yahweh did for the Israeli people].) [RHQ] (Has anyone ever heard of anything like this?/Certainly no one has ever heard of anything like this.) [RHQ]
Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
33 (Has any group ever remained alive after they heard a god speak to them from the middle of a fire, like we did?/Certainly no group has ever remained alive after they heard a god speak to them from the middle of a fire, like we did.) [RHQ]
Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
34 Certainly no other god has ever tried to take a [huge] group of people from one nation [to another location], like he did for us when he brought us out of Egypt. We saw Yahweh our God use great power [MTY, DOU] when he performed many kinds of [DOU] miracles, and sent plagues, and did many other very terrifying things in Egypt for us, [and rescued us when the army of Egypt tried to fight against us].
Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
35 “Yahweh showed all these things to you, in order that you would know that only he is truly God, and that there is no other God.
Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
36 He allowed your ancestors to hear him speak from heaven in order that he could discipline them. Here on the earth he allowed them to see his great fire [on Sinai Mountain], and he spoke to them from the middle of the fire.
Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
37 Because he loved our ancestors, he chose you Israelis who are their descendants, and by his great power he brought your ancestors out of Egypt.
Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
38 [As they advanced], he expelled the people of nations that were greater and more powerful than they were, in order that he could allow them to capture their land and cause it to become yours, which is [what is happening] now.
kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
39 “So today you should (meditate on/think about) the fact that Yahweh is God, that he is/rules in heaven and also on the earth, and that there is no other god.
Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
40 Obey all the rules and regulations that I am giving to you today, in order that things will go well for you and for your descendants, and that you will live a long time in the land that Yahweh our God is giving to you, [to belong to you] forever.”
Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
41 Then Moses/I set apart three cities that are on the east side of the Jordan [River].
Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
42 If someone accidentally killed another person, a person who had not been his enemy previously, he could escape to one of those cities. He would be safe/protected in one of those cities [because the people there would protect him].
kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
43 For the tribe of Reuben, Moses/I set apart Bezer [city] in the (plateau/high level) area. For the tribe of Gad, Moses/I set apart Ramoth [city] in the Gilead [area]. For the tribe of Manasseh, Moses/I set apart Golan [city] in the Bashan [region].
Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
44 Moses/I gave [God’s] laws to the Israeli people.
Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
45 They included all the rules and instructions and commands that Moses/I gave to them, after they/we had come out of Egypt,
Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
46 when they/we were in the valley east of the Jordan [River]. They/We were across from Beth-Peor [town], in the land that [previously] was ruled by Sihon, the king of the Amor people-group, who lived in Heshbon [city]. Moses/I and the other Israelis had defeated his [army] when they/we came out of Egypt.
Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
47 They/We captured Sihon’s land and the land that Og, the king of the Bashan [region], ruled. They were the two kings who ruled the Amor people-group [in the area] east of the Jordan [River].
Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
48 Their land extended from Aroer [town in the south] along the Arnon [River], as far [north] as Sirion Mountain, which [most people] call Hermon Mountain.
Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
49 It also included all the area east of the Jordan [River] Valley, all the way south to the Dead Sea and east to the slopes of Pisgah [Mountain].
ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.

< Deuteronomy 4 >