< Deuteronomy 29 >
1 These are the things that the Israelis were required to do to keep the agreement that Yahweh was making with them. Moses/I commanded them to keep this agreement [when they/we were] in the Moab region [on the east side of the Jordan River]. This was in addition to the agreement that Yahweh had made with them/us at Sinai [Mountain].
Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
2 Moses/I summoned all the Israeli people and said to them, “You saw [SYN] for yourselves what Yahweh did to the king of Egypt and to his officials and to his entire country.
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
3 You [SYN] saw all the plagues [that Yahweh caused them to experience], and all the various miracles [DOU] [that Yahweh performed].
Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
4 But until now, Yahweh has not enabled you to understand [the meaning of] all that you have seen and heard.
Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
5 For 40 years Yahweh has led you while you traveled/walked through the desert. During that time, your clothes and your sandals have not worn out.
Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
6 You did not have bread to eat or wine or other fermented/strong drinks to drink, but Yahweh [took care of you], in order that you would know that he is your God.
Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
7 “And when we came to this place, Sihon, the king who ruled in Heshbon [city], and Og, the king who ruled the Bashan [region], came [with their armies] to attack us, but we defeated them.
Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
8 We took/conquered their land and divided it among the tribes of Reuben and Gad, and half of the tribe of Manasseh.
Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
9 “So faithfully keep all of this agreement, in order that you will be successful in everything that you do.
Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
10 Today all of us are standing in the presence of Yahweh our God. The leaders of all our tribes, our elders, our officials, all you Israeli men,
Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
11 your wives, your children, and the foreigners who live among you and cut wood for you and carry water for you, are here.
pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
12 [We are here] today to promise to keep this solemn agreement with Yahweh.
Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
13 [He is making this agreement with you] in order to confirm that you are his people, and that he is your God. This agreement is what he promised you, and which is what he vowed to give to your ancestors Abraham, Isaac and Jacob.
kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
14 This agreement is not only with you.
Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
15 He is making this agreement with us [who are here today] and also with our descendants who are not yet born.
amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
16 “You remember [the things that our ancestors suffered] in Egypt, and how they traveled through the land that belonged to other nations [after they came out of Egypt].
Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
17 In those countries they saw those disgusting idols made of wood and stone and [decorated with] silver and gold.
Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
18 So be sure that no man or woman or family or tribe that is here [today] turns away from Yahweh our God, to worship/serve the gods of those nations. Doing that would be like a root [of a plant that would grow] among you and bear poisonous and bitter fruit [MET].
Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
19 “Be sure that no one here today who hears this agreement thinks, ‘Everything will go well with me, even if I stubbornly do what I want to.’ If you are stubborn like that, the result will be that Yahweh will eventually get rid of all of you, both good people and evil people [MET].
Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
20 Yahweh will not forgive anyone who is [stubborn] like that. Instead, he will be extremely angry [DOU] with that person, and that person will experience all the curses that I have told you about, until Yahweh gets rid of that person and his family [IDM].
Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
21 From all the tribes of Israel, Yahweh will separate that individual. Yahweh will cause him to experience all the disasters that I have listed in the agreement that states the things that Yahweh will do to curse [those who disobey] the laws [that I have written] in this scroll/book.
Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
22 “In the future, your descendants and people from other countries will see the disasters and the illnesses that Yahweh has caused to happen to you.
Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
23 They will see that all your land has been ruined by burning sulfur and salt. Nothing will have been planted. Not even weeds will grow there. Your land will resemble Sodom and Gomorrah [cities], and Admah and Zeboiim [cities], which Yahweh destroyed when he was very angry [DOU] [with the people who lived there].
Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
24 And the people from those other nations will ask, ‘Why did Yahweh do this to this land? Why was he very angry [with the people who lived here]?’
Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
25 “Then other people will reply, ‘It is because they refused to keep the agreement that Yahweh, the God whom their ancestors [worshiped], had made with them when he brought them out of Egypt.
Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
26 Instead, they served/worshiped other gods that they had never worshiped before, gods that Yahweh had told them not to worship.
Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
27 So, Yahweh became very angry with the Israeli people in this land, and he caused them to experience all the disasters that their leader warned them about.
Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
28 Yahweh became extremely angry [DOU] with them and took/yanked them [MET] out of their land and banished them into another land, and they are still there.’
Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
29 “[There are some] things that Yahweh our God has (kept secret/not revealed), but he has revealed his laws to us, and [he expects] us and our descendants to obey them forever.”
Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.