< Deuteronomy 24 >

1 “Suppose a man marries a woman and later decides that he does not want her because there is something about her that he doesn’t like. And suppose he writes on paper that he is divorcing her, and he gives the paper to her [SYN] and sends her away from his house.
Ngati mwamuna wakwatira mkazi amene sakukondwera naye chifukwa wapeza vuto pa mkaziyo, namulembera mkaziyo kalata ya chisudzulo, namupatsa ndi kumutulutsa mʼnyumba mwake,
2 Then suppose that she goes and marries another man,
mkaziyo ndi kukakwatiwa ndi mwamuna wina,
3 and that man [later also] decides that he does not like her, and he also writes on paper that he is divorcing her, and he sends her away from his house. Or, suppose that the second husband dies.
ndipo mwamuna wachiwiriyo nʼkuyipidwa nayenso ndi kumulemberanso kalata ya chisudzulo nʼkumutulutsa mʼnyumba mwake, kapena ngati mwamunayo amwalira,
4 If either of those things happens, her first husband must not marry her again. He must consider that she has become unacceptable to Yahweh. Yahweh would consider it to be disgusting [if he married her again]. You must not sin [MTY] by doing that in the land that Yahweh our God is giving to you.”
mwamuna wake woyamba uja, amene anamuleka saloledwanso kumukwatira kachiwiri popeza mkaziyo wadetsedwa. Chimenechi ndi chonyansa pamaso pa Yehova. Musalowetse tchimo mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu.
5 “When some man has recently become married, he must not [be required to] become a soldier in the army or be required to do any other work [for the government] for one year [after being married]. He should stay happily at home with his wife for that year.
Mwamuna akangokwatira kumene asamatumizidwe ku nkhondo kapena kupatsidwa ntchito ina iliyonse. Kwa chaka chathunthu akhale ndi ufulu wokhala pa khomo pake kumasangalatsa mkazi wakeyo.
6 “Anyone who lends money to someone else [is allowed to require that person to give him something] to guarantee [that he will pay back the money that he borrowed. But] he must not take from him his (millstone/stone for grinding grain). That would be taking [the millstone that his family needs to grind the grain to make the bread] they need to stay alive.
Munthu akakhala nanu ndi ngongole musamutengere mwala wake wa mphero ngati chikole, chifukwa kutero nʼkumutengera moyo kukhala chikole cha ngongole.
7 “If someone kidnaps/steals a fellow Israeli to cause that person to become his slave or to sell him [to become someone else’s slave], you must execute the person who did that. By doing that, you will get rid of this evil among you.
Ngati munthu agwidwa akuba mʼbale wake wa Chiisraeli namamuzunza ngati kapolo kapena kumugulitsa, wogulitsa mnzakeyo ayenera kuphedwa. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
8 “If you are suffering from (leprosy/a dreaded skin disease), be sure to do everything that the priests, who are from the tribe of Levi, tell you to do. Obey carefully the instructions that I have given to them.
Pakagwa matenda a khate, samalitsani kuchita zonse zimene ansembe, amene ndi Alevi, anakulangizani. Mutsatire mosamalitsa zimene ndinawalamula.
9 Do not forget what Yahweh our God did to Miriam, [when she became a leper], after your ancestors left Egypt.
Kumbukirani zimene Yehova Mulungu wanu anachita kwa Miriamu muli paulendo mutatuluka mu Igupto.
10 “When you lend something to someone, do not go into his house to take the cloak that he says that he will give you to guarantee [that he will return what he has borrowed].
Ukabwereketsa mnzako kanthu kena kalikonse, usalowe mʼnyumba mwake kukatenga chimene wachipereka ngati chikole.
11 Stand outside his house, and the man to whom you are lending something will bring the cloak out to you.
Uziyima kunja kwa nyumba kuti munthu amene wamubwereketsa kanthuyo akubweretsere kunja komweko.
12 But if he is poor, do not keep that cloak all night.
Ngati munthuyo ndi wosauka, usamutengere chikolecho mpaka kukagona nacho kwanu.
13 When the sun sets, take the cloak back to him, in order that he may wear it while he sleeps. If you do that, he will [ask God to] bless you, and Yahweh our God will be pleased with you.
Pomalowa dzuwa ukhale utamubwezera mkanjo wakewo kuti akafunde. Pamenepo adzakuthokoza, ndipo amenewa adzawerengedwa ngati machitidwe olungama kwa iweyo pamaso pa Yehova Mulungu wako.
14 “Do not mistreat any servants whom you have hired who are poor and needy [DOU], whether they are Israelis or foreigners who are living in your town.
Osamapezera mwayi pa anthu aganyu osauka ndi aumphawi, kaya ndi Mwisraeli kapena mlendo wokhala mu umodzi mwa mizinda yanu.
15 Every day, before sunset, you must pay/give them the money that they have earned. They are poor and they need to get their pay. If you do not pay them right away, they will cry out against you to Yahweh, and he will punish [MTY] you for having sinned like that.
Mumulipire malipiro ake a tsiku dzuwa lisanalowe chifukwa ndi wosauka ndipo akudalira malipirowo. Kupanda kutero adzakudandaulirani kwa Yehova ndipo mudzapezeka ochimwa.
16 “Parents must not be executed for crimes that their children have committed, and children must not be executed for crimes that their parents have committed. People should be executed only for the crimes that they themselves have committed.
Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.
17 “You must [LIT] do for foreigners [who live] among you and for orphans what the laws state must be done for them. And [if you lend something to] a widow, do not take her coat from her as a guarantee [that she will return it].
Musachitire mlendo kapena mwana wamasiye zoyipa, kapena kulanda mkazi wamasiye chovala ngati chikole cha ngongole.
18 Do not forget that [you had great hardships/troubles when] you were slaves in Egypt, and Yahweh our God rescued you from there. That is why I am commanding you [to help others who have troubles].
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwombolani kumeneko. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.
19 “When you harvest your crops, if you have forgotten [that you left] one bundle in the field, do not go back to get it. [Leave it there] for foreigners, orphans, and widows. If you do that, Yahweh will bless you in everything that you do.
Mukamakolola mʼmunda mwanu ndipo zokolola zina zikasiyidwa, musamabwerere kukazitola. Muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochita zanu zonse.
20 And when you have harvested/picked all your olives from the trees once, do not go back [to pick the ones that are still] on the trees.
Mukathyola zipatso mu mtengo wa olivi, musamabwererenso kachiwiri ku mtengo womwewo. Zotsalazo zilekereni alendo, ana ndi akazi amasiye.
21 [Similarly], when you pick the grapes in your vineyard, do not go back a second time [to try to find more]. Leave them for the foreigners, orphans, and widows [among you].
Mukakolola mphesa mʼmunda mwanu musamabwereremonso kachiwiri. Zotsalazo muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye.
22 Do not forget that [Yahweh was kind to you when] you were slaves in Egypt. That is why I am commanding you [to be kind to those who are needy].”
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.

< Deuteronomy 24 >