< Deuteronomy 21 >
1 “Suppose someone has been murdered in a field in the land that Yahweh our God is giving to you, and you do not know who killed that person.
Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha,
2 [If that happens], your elders and judges must go out to where that person’s corpse was found and measure the distance from there to each of the nearby towns.
akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira.
3 Then the elders in the town that is closest to where the corpse was found must select a young cow that has never been used for doing work.
Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli
4 They must take it to a place near a stream where the ground has never been plowed or planted. They must break its neck there in that valley.
ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo.
5 The priests must go there also, because Yahweh our God has chosen them from the tribe of Levi to serve him and to be his representatives [MTY] when they bless people. And he has also chosen them to settle disputes in which someone has been injured.
Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana.
6 The elders from the closest town must wash their hands over the young cow whose neck was broken,
Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija,
7 and they must say, ‘We did not murder this person [MTY], and we did not see who did it.
nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako.
8 Yahweh, forgive us, your Israeli people whom you rescued [from Egypt]. Do not consider (us to be guilty/that we should be punished because) of murdering someone who (is innocent/had not done something that is wrong). Instead, forgive us.’
Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa.
9 By doing that, you will be doing what Yahweh considers to be right, and you will not be considered to be guilty for murdering that person.”
Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.
10 “When you [soldiers] go to fight against your enemies, and Yahweh our God enables you to defeat them [IDM], and (they become your prisoners/you capture them),
Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo,
11 one of you may see among them a beautiful woman that he likes, and he may want to marry her.
ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu.
12 He should take her to his home, and there she must shave [all the hair off] her head and cut her fingernails [to signify that now she does not belong to her people-group any more, but instead she is becoming an Israeli].
Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake
13 She must take off the clothes that she was wearing when she was captured, [and put on Israeli clothes]. She must stay in that man’s house and mourn for a month because of [leaving] her parents. After that, he will be allowed to marry her.
ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu.
14 Later, if he no longer is pleased with her, he will be permitted to allow her to leave him. But because she was forced to have sex with him, he will not be allowed to treat her like a slave [and sell her to someone else].”
Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.
15 “Suppose that a man has two wives, but he likes one of them and dislikes the other one. And suppose that they both give birth to sons, and the oldest son is the child of the woman that he does not like.
Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo,
16 On the day when that man decides how he will divide his possessions for his sons to possess [after he dies], he must not favor the son of the wife that he loves by giving him [a bigger share, ] the share that the older son should receive.
akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda.
17 He must give to the older son, the son of the wife whom he does not like, twice as much of his possessions. That son is his firstborn son, and he must be given the share that he should receive because of his being that man’s firstborn son.”
Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.
18 “Suppose there is a boy who is very stubborn and always (rebelling against/disobeying) [his parents], and who will not heed what they say to him. And suppose that they punish him but he still does not pay attention to what they tell him [MTY].
Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza,
19 If that happens, his parents must take him to the (gate of/central meeting place in) the city where he lives and have him stand in front of the elders of the city.
abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo
20 Then the parents must say to the elders of that city, ‘This son of ours is stubborn and always rebelling against us. He will not pay attention to what we tell him [MTY]. He wastes a lot of money (OR, eats too much food) and gets drunk.’
akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.”
21 Then all the elders of that city must execute him by throwing stones at him. By doing that, you will get rid of this evil practice among you. And everyone in Israel will hear [about what happened] and they will be afraid [to do what he did].”
Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.
22 “If someone is executed for having committed a crime for which he deserves to die, and you hang his corpse on a post,
Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo,
23 you must not allow his corpse to remain there all night. You must bury it on the day that he died, because [God] has cursed anyone whose corpse is allowed to remain on a post. [You must bury the corpse that day], in order that you do not defile the land that Yahweh our God is giving to you.”
musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.