< Deuteronomy 12 >
1 “(I will now tell you again/These, [again], are) the rules and regulations that you must faithfully obey in the land that Yahweh, the God whom our ancestors [worshiped], is giving to you to occupy. You must obey these laws all the time that you are alive.
Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo.
2 You must destroy all the places where the people-groups that you will expel worship their gods, on the tops of mountains and hills and under big green trees.
Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo.
3 You must tear down their altars and smash their sacred pillars. Completely burn the statues of their goddess Asherah in fires, and chop down their wooden idols, in order that no one will ever worship them [MTY] in those places again.
Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.
4 “Do not worship Yahweh like [the people in Canaan worship their gods].
Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa.
5 Instead, you must go to the place that Yahweh will choose. It will be in the area where one of your tribes will live. That is where you must go to worship Yahweh.
Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako.
6 That is the place where you must bring your sacrifices that will be completely burned on the altar, and your other sacrifices, (your tithes/ten percent of all of your crops), other offerings that you decide to give, and the firstborn animals from your cattle and sheep.
Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu.
7 There, in the presence of Yahweh our God, who has [greatly] blessed you, you and your families will eat the good things that you have worked to produce, and you will be happy.
Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.
8 “[When you are in that land], you must not do some of the things that we have been doing. Until now, you have all been worshiping [Yahweh] the way you wanted to,
Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera,
9 because you have not yet arrived in the land which Yahweh is giving to you, where you will be able to live peacefully.
pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
10 But when you cross the Jordan [River], you will start to live in the land that Yahweh our God is giving to you. He will protect you from all your enemies that will surround you, and you will live peacefully/safely.
Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa.
11 “Yahweh will choose one place where he wants you to worship him. That is the place to which you must bring all the offerings that I command you to bring: The sacrifices that must be completely burned [on the altar], your other sacrifices, other offerings that you yourselves decide to give, (your tithes/ten percent of all your crops), and all the special offerings that you will solemnly promise to give to Yahweh.
Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova.
12 Rejoice there in the presence of Yahweh, along with your children, your male and female servants, and the descendants of Levi who live in your towns. Do not forget that the descendants of Levi will not have their own land, like you will have.
Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo.
13 Be sure that you do not offer sacrifices anywhere you want to.
Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune.
14 You must offer them only in the place that Yahweh will choose for you, in an area that belongs to one of your tribes. That is the only place where he wants you to offer sacrifices that will be completely burned [on the altar], and to do the other things that I am commanding you to do [when you worship him].
Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.
15 “However, you will be permitted to kill and eat the meat of your animals in the places where you live. As often as you want to, you may eat the meat of the animals that Yahweh our God will bless you by giving them to you. Those who have done things that cause them to become unacceptable to God and those who have not done things like that may all eat that meat, just like you would eat the meat of a deer or an antelope.
Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya.
16 But you must not eat the blood [of any animals]; you must let the blood drain onto the ground [before you cook the meat].
Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi.
17 In the places where you live, you must not eat the things that you are offering [to Yahweh]: You must not eat the (tithes/ten percent) of your grain or of your wine, or of your [olive] oil, or the firstborn of your cattle and sheep, or the offerings that you yourselves decide to give to Yahweh, or any other offerings.
Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera,
18 Instead, you and your children and your male and female servants and the descendants of Levi who live in your towns must go to the place that he has chosen and eat those things there in the presence of Yahweh. And you should rejoice in the presence of Yahweh about everything that you do.
mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza.
19 Be sure that you take care of the descendants of Levi all during the time that you live in your land.
Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.
20 “When Yahweh our God gives you much more land [than you will have when you first occupy it], which is what he has promised to do, and you say ‘I would like some meat to eat’ because you are craving/wanting some meat, you will be permitted to eat meat whenever you want to.
Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire.
21 If the place that Yahweh our God chooses to be the place for you to worship him is far [from where you live], you are permitted to kill some of your cattle or sheep that Yahweh has given to you, and you may eat that meat at the places where you live, just like I have told you to do.
Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire.
22 Those who have done things that cause them to become unacceptable to God, and those who have not done things like that, are all permitted to all eat that meat, just like you would eat the meat of a deer or an antelope.
Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya.
23 But be sure that you do not eat the blood [of any animal], because it is the blood that sustains life in living beings, and so you must not eat the life along with the meat.
Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama.
24 Do not eat the blood; instead, let it drain onto the ground.
Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi.
25 If you obey this command and do what Yahweh says is right [for you to do], things will go well for you and for your descendants.
Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.
26 “But the sacred offerings that Yahweh has told you to give and the other offerings that you yourselves decide to give, you must take to the place that Yahweh will choose.
Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe.
27 You must offer there the sacrifices that will be completely burned [on Yahweh’s altar]. You must also offer there the sacrifices from which you may eat some of meat after you [kill the animals and] drain out the blood and some of it is thrown on the [sides of the] altar.
Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya.
28 Faithfully obey all these things that I have commanded you. If you do that, things will go well forever for you and your descendants, because you will be doing what Yahweh our God says is right [for you to do] and what pleases him.
Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 “When you enter the land that you will occupy, as you advance, Yahweh our God will get rid of the people-groups that live there.
Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo,
30 After he does that, be sure that you do not [worship the gods] that they have been worshiping, because if you do that, you will be caught in the same trap [that they were caught in] [MET]. Do not ask anyone about those gods, saying, ‘Tell me how they worshiped their gods, in order that I can [worship them] also.’
ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.”
31 Do not try to worship Yahweh our God like they have worshiped their gods, because when they worship them, they do disgusting things, things that Yahweh hates. [The worst thing that they do is] that they sacrifice their own children and burn them [on their altars].
Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.
32 “Be sure to do everything that I have commanded you to do. Do not add anything to these commands, and do not take anything away from them.”
Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.