< Daniel 9 >

1 [Now I am going to tell you about what happened] when Darius, who was from the Mede people-group and who was the son of Xerxes, ruled as the King of Babylonia.
Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
2 During the first year that he was the king, I, Daniel, was studying/reading the [holy] books/Scriptures the message that Yahweh had given to the prophet Jeremiah. In that message Jeremiah had written that Jerusalem would [be destroyed and] remain ruined for seventy years.
ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
3 [After I read that], I pleaded to Yahweh my God [to help us], praying and (fasting/abstaining from eating food). [While doing that, I was wearing] rough cloth and [sitting in] ashes [to show that I was very sad about what was going to happen to us].
Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
4 I confessed [the sins that we had committed], and [this is what I] prayed: Lord, you are great and awesome! You have faithfully done what you said that you would do for us. You faithfully love those who love you and who do what you have commanded [that they should do].
Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
5 But we [Israelis] have sinned. We have done things that are wrong. We have done wicked things, and we have rebelled [against you]. We have turned away from [obeying] your commands [DOU].
tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
6 Your prophets spoke for you [MTY], [giving your messages to] kings, to our other rulers, to our [other] ancestors, and to all the Israeli people, but we have refused to (pay attention to/heed) those prophets.
Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
7 Lord, you always do what is righteous/just/fair, but we have caused ourselves to be ashamed [IDM]. This is [still] true about all of the Israelis who live in Jerusalem and who live in other places in Judea. It is [also] true about all us Israelis whom you scattered, who [were taken to] other countries, some near [Israel] and some far away, because we were very unfaithful/disloyal to you.
“Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
8 Lord, we and our kings and our other rulers and our [other] ancestors have done very shameful things and have sinned against you.
Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
9 Although we have rebelled against you, you act mercifully [toward us] and you [are willing/ready] to forgive us.
Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
10 Yahweh our God, when you gave your laws to your prophets who served you, and they told us to conduct our lives according to those laws, we did not (listen to/heed) you.
Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
11 All [of us] Israeli people have disobeyed your laws, and we have turned away from [obeying] what you said. We have sinned against you. As a result, [you] have caused us to experience the terrible things that your servant Moses said/wrote [would happen to us] if we sinned against you.
Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
12 You warned us and our rulers that you would punish Jerusalem severely by causing a great disaster there, a disaster that would be worse than any disaster that any other city had ever experienced, and you have done what you said that you would do.
Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
13 [You] punished us just like Moses wrote [that you would do]. But, Yahweh our God, we still have not tried, by turning away from our sinning and by heeding your truth, to persuade you to act mercifully toward us.
Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
14 So, because we did not obey you, you prepared to punish us, and [then] you did punish us, because you always do what is righteous/just/fair.
Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
15 O Lord our God, you brought your people out of Egypt by your great power [MTY], and by doing that you have caused people from that time until the present time to know that you are great [IDM] [even though] we have sinned and done wicked things.
“Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
16 Lord, Jerusalem is your city, and [your temple was built there] on your sacred hill. Now all the people who live in nearby [countries/nations] despise Jerusalem and [us] your people because of our sins and because of the evil things that our ancestors did. But [now], because you do what is righteous/just, [we ask you to] not be angry with Jerusalem any longer.
Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
17 O Lord our God, listen to what I am praying and pleading [for you to do]. (For your own sake/In order that people will know that you are very great), act kindly [IDM] concerning your temple, which was destroyed [by the armies of Babylonia].
“Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
18 My God, listen [to my prayer]. Look [at us] and see our troubles, and see that this city that belongs to you [MTY] has been ruined/destroyed. We are praying to you because you are merciful, not because we have done what is right/good.
Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
19 Lord, listen [to us]! Lord, forgive us! Lord, this city and these people belong to you, so [we plead with you to] heed what we are saying and act [to help us] right now, (for your own sake/in order that people will know that you are very great)!
Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
20 I continued praying and confessing the sins that my people and I had committed, and pleading with Yahweh my God that he would restore [the temple on] the sacred hill [in Jerusalem].
Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
21 While I was praying, Gabriel, the angel/one whom I had seen in the vision previously, came flying rapidly to me, at the time in the evening when [the priests] offered sacrifices.
Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
22 He said to me, “Daniel, I have come to you to enable you to understand [DOU] clearly [the message that God gave to Jeremiah].
Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
23 When you began to plead [with God], he gave me a message [to pass on to you]. He loves you very much, so [he has sent me] to tell you what he said to me. So [now] (pay attention/listen carefully) in order that you may understand the meaning of what he revealed [to Jeremiah].
Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
24 [God] has determined/declared that there will be 490 years until he frees/saves your people from [the guilt of] their sins and to atone for the evil things that they have done. Then [God] will rule everyone justly, and he will do that forever. And [what you saw in] the vision and what [Jeremiah] prophesied will (come true/be fulfilled), and the sacred temple will be dedicated [to God again].
“Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
25 You need to know and understand this: There will be 49 years from the time that [the king] commands that Jerusalem should be rebuilt until the leader/king that God has chosen will come. Then 434 years later, Jerusalem will be rebuilt, and it will have streets and will have a (moat/deep ditch filled with water) around it [to protect the city]. But that will be a time when [God’s people] will have [a lot of] troubles/difficulties/suffering.
“Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
26 After those 434 years, the leader/king whom God has appointed will be killed [when it seems that] he will have accomplished nothing (unjustly/without having done anything wrong). After that, the temple will be destroyed by [the army of] a powerful ruler. The city and the temple will be destroyed like a flood [MET] [destroys everything]. That will be the beginning of the war and destruction that [God] has decreed [will happen].
Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
27 That ruler will make a strong agreement with many people. He will promise to do for seven years what he has said in that agreement. But when that time is half finished, he will prevent [priests from] giving any more offerings and sacrifices [to God]. A disgusting idol will be put on the highest part of the temple, and it will stay there until [God] gets rid of the one who put it there, which is what he said that he would do.”
Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”

< Daniel 9 >