< Daniel 6 >
1 King Darius decided to divide his kingdom into 120 provinces. He appointed a governor to rule each province.
Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
2 He also appointed me and two other men to be administrators, to supervise the governors and to be sure that they did the king’s work [properly], in order that the king would not have to worry about anything.
ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
3 I soon showed that I was (more capable/able to do the work better) than all the other administrators and the governors. Because of that, the king planned to appoint me to be in charge of the entire empire.
Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
4 Then, the [other] administrators and the governors [became jealous. So they began to] try to find something that they could criticize about the way I was working for the king. But I always did my work faithfully and honestly, and was never lazy. So they could not find anything to criticize.
Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
5 They concluded, “The only way we can find something for which we can criticize Daniel will be something concerning the laws that his god [his given him].”
Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
6 So the administrators and governors went as one group to the king and said, “(Your Majesty/O king), we wish that you will live a long time!
Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
7 [We] administrators and governors and district governors and advisors and other officials have all agreed that you should make a law that everyone must obey. We want you to command that for the next thirty days people may pray only to you. If anyone prays to anyone else, either to a human or to a god, he must be thrown into [a pit of] lions.
Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
8 And because laws made by [our governments of] Media and Persia cannot be changed, [we want] you, [the head of our government], to sign it.”
Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
9 So King Darius [wrote] the law and signed it.
Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
10 But when I found out that [the king] had [written and] signed that law, I went home. I knelt down in my upstairs room and prayed. I looked toward Jerusalem, and the windows were open [with the result that everyone could see me while I was praying]. I prayed three times each day, just as I always did, thanking God.
Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
11 The officials went together [to my house] and they saw me praying and requesting God to help me.
Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
12 So they returned to the king and said to him, “[Do you remember] that you wrote a law stating that for the next thirty days people may pray only to you, and if anyone prays to anyone else, either to a human or to a god, he will be thrown into [a pit of] lions?” The king replied, “[Yes, that is the law that I wrote]. It is a law of [our governments of] Media and Persia, which cannot be canceled.”
Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
13 Then they said to the king, “Well, that [man] Daniel, one of the men who were brought from Judah, is not paying any attention to you or the law that you [signed]. He prays [to his god] three times each day!”
Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
14 When the king heard that, he was very distressed. He tried to find a way to save me. All the rest of that day he tried to think of a way to rescue me.
Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
15 [In the evening, many of] [HYP] the officials went together to the king and said, “(Your Majesty/O king), you know that [our governments of] Media and Persia have declared that no law that the king signs can be canceled/changed. [So Daniel must be thrown to the lions!]”
Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
16 So the king gave the order, and his servants brought me and threw me into a pit where the lions [were]. [Before they threw me in], the king said to me, “I hope/wish that your God, whom you worship regularly, will rescue you!”
Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
17 They rolled a huge stone across the entrance to the pit. Then the king [fastened a string across the entrance and put wax at each end, and stamped the wax with] the seal from his [ring] and the seals [of the rings] of his officials, in order that no one could [secretly] rescue me.
Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
18 Then the king returned to his palace. That night he refused to eat any food. He would not allow anyone to entertain him [because he did not want to be happy, with the result that he would forget about me. And that night] he was unable to sleep [because he was worried about me].
Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
19 At dawn the next morning, the king got up and went quickly to the pit where the lions were.
Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
20 When he came near it, he was very worried. He called out, “Daniel, you who serve the all-powerful God! Was your God, whom you worship regularly, able to save you from the lions?”
Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
21 I answered, “(Your Majesty/O king), I hope that you will live a long time!
Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
22 [Yes], my God sent his angel to shut the lions’ mouths, in order that they would not harm me! [He did that] because [he knows that] I have done nothing that he thinks is wrong. And, (Your Majesty/O king), I never did anything wrong to you!”
Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
23 The king was extremely happy, and he commanded [his servants] to lift me out of the pit. [When they did that, they] saw that the lions had not wounded me at all. [God had protected me] because I trusted in him.
Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
24 Then the king commanded that the men who had accused me should be seized and be thrown, along with their wives and children, into the pit where the lions were. [When they were thrown into the pit], the lions leaped on them and crushed their bones before they fell onto the bottom of the pit!
Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
25 Then King Darius wrote [this message and sent it throughout his kingdom] to the people of every people-group and nation and from all language groups: “I wish/hope that everything is going very well with you!
Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
26 I command that everyone in my kingdom should fear and revere the God that Daniel [worships]. He is the all-powerful God, and he will live forever. His kingdom will never be destroyed; he will rule forever.
“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
27 He rescues and saves [his people]. He performs all kinds of miracles in heaven and on the earth. He rescued Daniel from the power of the lions!”
Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
28 So I was successful [all] during the time that Darius ruled and during the time that Cyrus, [the King] of Persia, ruled.
Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.