< Daniel 2 >

1 [One night] during the second year that Nebuchadnezzar ruled, he had a dream. The dream worried him very much; and [as a result] he could not sleep.
Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
2 [The next morning] he summoned his men who worked magic, fortune-tellers, those who worked sorcery, and those who studied the stars. [Because he had forgotten what he had dreamed, ] he insisted that they tell him what he had dreamed. As they stood there in front of the king,
Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
3 he said, “I had a dream [last night] that worries me. [Tell me what I dreamed, because] I want to know what the dream [means].”
mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
4 The men who studied the stars replied to the king, speaking in the Aramaic [language]. They said, “King Nebuchadnezzar, we hope that you will live a long time! Tell us what you dreamed, and [then] we will tell you what it means!”
Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
5 But the king replied, “I have firmly decided that you must tell me the dream, and [also tell me] what it means. If you do not do that, I will [order my soldiers to] cut you into pieces, and to cause your houses to become only piles of stones!
Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
6 But if you tell me what I dreamed and what it means, I will reward you. I will give you wonderful gifts and greatly honor you. So tell me what I dreamed and what it means!”
Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
7 But again they said, “Tell us what you dreamed, and [then] we will tell you what it means.”
Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
8 The king replied, “I know that you are just trying to get more time, because you know that I will do to you what I said that I would do.
Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
9 If you do not tell me what I dreamed, you will be punished. [I think that] you have all agreed to tell me lies and [other] wicked things, because you hope that I will change ([my mind/what I am thinking]). But tell me the dream, and [then] I will know that you can [also] tell me what it means.”
Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
10 The men who studied the stars replied, “There is no one on the earth who can do what you ask! There is no king, [even] a great and mighty king, who has [ever] asked his men who work magic or his fortune-tellers or men who study the stars to do something like that!
Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
11 What you are asking [us to do] is impossible. Only the gods can tell you what you dreamed, and they do not live among us!”
Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
12 The king was very angry when he heard that, so he commanded [his soldiers] that they execute all such wise men in Babylon.
Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
13 And because of what the king commanded, they sent some men to find me and my [three] friends, to execute us [also].
Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
14 Arioch, the commander of the king’s guards, came to kill us. But I spoke to him very wisely and tactfully/skillfully.
Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
15 I asked Arioch, “Why has the king made such a harsh/terrible decree?” So Arioch told me all that had happened [because of the king’s dream].
Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
16 I [immediately] went to talk to the king and requested that the king give me some time, so that I could find out [what the dream was and] what the dream meant.
Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
17 Then I went home, and I told my friends, Hananiah, Mishael, and Azariah, what had happened.
Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
18 I urged them to ask God, who lives/rules in heaven, to have mercy on us by telling us the secret [meaning of what the king dreamed], in order that we and the other wise men in Babylon would not be executed.
Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
19 And that night [God] gave to me a vision in which he revealed the secret. Then I praised God,
Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
20 saying, “We should praise God [MTY] forever, because [only] he truly is wise and powerful.
ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
21 He determines what events will happen through the years. He removes [some] kings and gives their authority to [new] kings. He is the one who causes people to become wise and enables those who study to understand [many] things.
Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
22 He reveals things that are very mysterious; he is surrounded by light, but he knows things that are hidden [as though they were] in the darkness.
Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
23 God, whom my ancestors [worshiped], I thank you and I praise you, because you have caused me to be wise and made me strong. You have told me what my friends and I asked you to tell us; and you have revealed to us what the king demanded to know.”
Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
24 Then I went to Arioch, the man whom the king had appointed to execute the wise men in Babylon. I said to him, “Do not kill those wise men. Take me to the king, and I will tell him what his dream means.”
Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
25 So Arioch quickly took me to the king. He said to the king, “I have found [this man], one of the men whom we brought from Judah who [says he can] can tell you what your dream means!”
Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
26 The king said to me, whose [new] name was Belteshazzar, “[Is this true]? Can you tell me what I dreamed and what it means?”
Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
27 I replied, “There are no wise men or fortune-tellers or men who work magic or men who work sorcery who can tell such things to you.
Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
28 But there is a God in heaven who reveals secrets. And he has shown in [your dream] what will happen in the future. Now I will tell you what you dreamed, the vision you saw [as you were lying] on your bed.
koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
29 O King, while you were sleeping, you dreamed about events that will happen in the future. The one who reveals mysteries has shown you what is going to happen.
“Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
30 And it is not because I am wiser than anyone else on earth that I know the meaning of this mysterious dream. It is because God wanted you to understand what you were thinking.
Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
31 O King, [in your vision] you saw in front of you a huge and terrifying statue [of a man. It was] shining very brightly, and it was frightening and awesome.
“Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
32 The head of the statue was [made] of pure gold. Its chest and arms [were made of] silver. Its belly and thighs [were made of] bronze.
Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
33 Its legs [were made of] iron, and its feet were a mixture of clay and iron.
Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
34 As you watched, something cut a rock [from a mountain, but it was] not a human [who cut it]. The rock [tumbled down and] smashed the feet of the statue, feet [that were made of] iron and clay. It smashed them to bits.
Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
35 Then the rest of the statue collapsed into a big heap of iron, clay, bronze, silver, and gold. The pieces of the statue were as small as bits of chaff on the ground where it is threshed, and the wind blew away all the tiny pieces. There was nothing left. But the rock that smashed the statue became a large mountain that covered the whole earth.
Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
36 That was what you dreamed. Now I will tell you what it means.
“Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
37 You are a king [who rules] over [many other] kings. The God who rules in heaven has caused you to rule over them and has given you great power [DOU] and has honored you.
Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
38 He has caused you to be the ruler over all people, and [even] the animals and birds are controlled by you. [So] the head [of the statue] represents you.
Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
39 But after your [kingdom/rule] ends, there will be another [great] kingdom, [but it] will not be as great as yours. [The silver parts of the statue represent that kingdom]. Then there will be a third [great] kingdom [whose king] will rule over the whole earth. The bronze parts [of the statue represent] that kingdom.
“Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
40 After that kingdom ends, there will be a fourth [great] kingdom. The iron [parts of the statue represent that kingdom]. [The army of] that kingdom will smash the previous kingdoms, just like iron smashes everything that it strikes.
Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
41 The feet and toes of the statue that you saw, that were a mixture of iron and clay, indicate that the kingdom they represent will [later] be divided.
Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
42 Some parts of that kingdom will be as strong as iron, but some parts will not remain together, just as iron and clay do not stick together.
Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
43 The mixture of iron and clay [in the statue] shows also that the rulers of those kingdoms that separate from each other will try to form alliances with each other as a result of members of the royal families of those kingdoms marrying each other. But that will not succeed, just as iron and clay do not stick together.
Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
44 But while those kings are ruling, God who rules in heaven will establish a kingdom that will never end. No one will ever defeat its king. He will completely destroy all those kingdoms, but his kingdom will remain forever.
“Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
45 That is the meaning of the rock that something cut from the mountain, the rock that will crush to tiny bits the statue that is made of iron, bronze, silver, and gold. O king, the great God has shown you what will truly happen in the future. And you can trust [what I told you about] the meaning of the dream.”
Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
46 Then King Nebuchadnezzar prostrated himself in front of me [in great respect]. He commanded [his people] that they burn incense and burn an offering of grain to honor me.
Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
47 The king said to me, “[Your God has enabled] you to tell me the meaning of this dream/mystery, so now I truly know that your God is greater than all the other gods and all other kings. He reveals [to people] things that they cannot know.”
Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
48 Then the king gave many gifts to me, and he [also] appointed me to rule over the entire province of Babylon, and [also] to be the boss of all his wise men.
Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
49 I asked the king to appoint Shadrach, Meshach, and Abednego to [also] have important positions in Babylon province, and the king did what I asked him to do. But [I did my work while] I stayed at the king’s palace.
Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.

< Daniel 2 >