< Amos 9 >
1 Yahweh [showed me another vision. In the vision, ] I saw him standing next to the altar. He said, “Shake the tops of the pillars [of the temple], until they become loose and fall down, so that even the foundation will shake. Then cause the [pieces of the temple] to fall down on the people [who are inside]. I will kill with a sword anyone who [tries to] flee; no one will escape.
Ine ndinaona Ambuye atayima pambali pa guwa lansembe, ndipo anati: “Kantha mitu ya nsanamira kuti ziwundo za nyumba zigwedezeke. Muzigwetsere pa mitu ya anthu onse, onse amene atsalira ndidzawapha ndi lupanga. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzathawe, palibe amene adzapulumuke.
2 If they dig deep pits in the ground, or if they try to climb up to the sky [in order to escape], I will reach out and grab them. (Sheol )
Ngakhale atakumba pansi mpaka ku malo a anthu akufa, dzanja langa lidzawatulutsa kumeneko. Ngakhale atakwera kumwamba Ine ndidzawatsakamutsa kumeneko. (Sheol )
3 If they go to the top of Carmel [Mountain] to escape, I will search for them and seize them. If they [try to] hide from me at the bottom of the sea, I will command the [huge] sea monster to bite them.
Ngakhale atakabisala pamwamba pa phiri la Karimeli, Ine ndidzawasaka kumeneko ndi kuwagwira. Ngakhale atakabisala pansi pa nyanja yayikulu, ndidzalamula njoka kuti iwalume kumeneko.
4 If their enemies [capture them and] force them to go to other countries, I will command that they be killed there with swords. I am determined [IDM] to get rid of them, not to help them.”
Ngakhale adani awo awakusire ku ukapolo, ndidzalamula lupanga kuti liwaphe kumeneko. Ndidzawayangʼanitsitsa kuti zoyipa ziwagwere; osati zabwino.”
5 When the Commander of the armies of angels touches the earth, it melts, and all over the earth [many people die, and the others] mourn for them. [It is as though] Yahweh causes the earth repeatedly to rise and fall like [SIM] the Nile [River] rises and falls.
Ambuye Yehova Wamphamvuzonse amene amakhudza dziko lapansi ndipo dzikolo limasungunuka, onse amene amakhala mʼmenemo amalira. Dziko lonse lidzadzaza ngati mtsinje wa Nailo, kenaka nʼkuphwera ngati mtsinje wa ku Igupto.
6 He builds his [beautiful] palace in heaven, and sets/causes the sky to be like a dome over the earth. He scoops up the water from the ocean and [puts it into clouds], and then empties [the clouds] onto the earth. His name is Yahweh.
Iye amene amamanga malo ake okhalamo kumwamba, ndi kuyika maziko ake pa dziko lapansi, Iye amene amayitana madzi a ku nyanja ndikuwakhuthulira pa dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova.
7 And Yahweh says, “You people of Israel, you are certainly [RHQ] [now no more important to me] than the people of Ethiopia. I brought your [ancestors] here from Egypt, but I also brought the people of Philistia from Crete [Island], and I brought the people of Syria from the Kir [region].
“Kodi kwa Ine, inu Aisraeli, simuli chimodzimodzi ndi Akusi?” Akutero Yehova. “Kodi sindine amene ndinatulutsa Israeli ku Igupto, Afilisti ku Kafitori ndi Aaramu ku Kiri?
8 I [SYN], Yahweh the Lord, have seen that you people in the kingdom [of Israel] are very sinful, so I will (destroy you/wipe you off the earth). But I will not get rid of all you descendants [MTY] of Jacob. [That is what will surely happen because] I, Yahweh, have said it.
“Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawu. Ndidzawufafaniza pa dziko lapansi. Komabe sindidzawononga kotheratu nyumba ya Yakobo,” akutero Yehova.
9 When I command it, [it will be as though] I will shake you Israeli people [who are living] in various nations, like [MET] [a farmer] shakes a sieve [to separate] the stone pebbles [from the grain], in order that they do not fall on the ground [with the grain].
“Pakuti ndidzalamula, ndipo ndidzagwedeza nyumba ya Israeli pakati pa mitundu yonse ya anthu monga momwe amasefera ufa mʼsefa, koma palibe nʼkamwala kamodzi komwe kamene kadzagwe pansi.
10 From among my people, all you sinful people who say, ‘We will not experience disasters; nothing evil will happen to us,’ will be killed by [your enemies’] swords.”
Anthu onse ochimwa pakati pa anthu anga adzaphedwa ndi lupanga, onse amene amanena kuti, ‘Tsoka silidzatigwera ife kapena kutiwononga.’
11 “The kingdom [over which King] David [ruled has been destroyed, like] [MET] a house that collapsed and then became ruins. But some day I will cause it to be a kingdom again. I will cause it to prosper again just like it did previously.
“Tsiku limenelo ndidzabwezeretsa nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso monga inalili poyamba,
12 When that happens, your [armies] will seize/capture the remaining part of Edom [region] again, and they will also seize the land in other nations that previously belonged to me [MTY]. I, Yahweh, have said [that I will do these things], and I will certainly cause them to happen.
kuti adzatengenso otsala a Edomu ndi mitundu yonse imene imatchedwa ndi dzina langa,” akutero Yehova amene adzachita zinthu izi.
13 There will be a time [when your crops will grow very well]. Very soon after the crops are harvested, farmers will plow the ground [to plant more crops in it again], and soon after the vineyards are planted, [farmers will harvest] grapes and tread on them [to make wine]. [And because there will be a lot of] wine, [it will seem as though] wine is flowing down from the hills [DOU].
Yehova akunena kuti “Nthawi ikubwera pamene mlimi wotipula adzapyola wokolola ndipo woponda mphesa adzapyola wodzala mbewu. Mapiri adzachucha vinyo watsopano ndi kuyenderera pa zitunda zonse.
14 I will cause you, my Israeli people, to prosper again. You will rebuild your towns and live in them. You will plant vineyards and then drink the wine [made from the grapes that grows in them].
Ndidzawabwezeranso pabwino anthu anga Aisraeli; mizinda imene inali mabwinja idzamangidwanso ndipo azidzakhalamo. Adzalima minda ya mpesa ndipo adzamwa vinyo wake; adzalima minda ndipo adzadya zipatso zake.
15 I will enable you to live [MET] in your land again, the land that I gave to [your ancestors], and never again will you be forced to leave it. [That is what will surely happen because] I, Yahweh, have said it.”
Ndidzakhazika Aisraeli mʼdziko mwawo, ndipo sadzachotsedwamonso mʼdziko limene Ine ndawapatsa,” akutero Yehova Mulungu wako.