< Acts 20 >
1 After the people at Ephesus had stopped rioting, Paul summoned the believers. He encouraged them [to continue to trust in the Lord Jesus. Soon] after that, he told them goodbye and left to go to Macedonia [province].
Litatha phokoso, Paulo anayitanitsa ophunzira ndipo atawalimbikitsa anawatsanzika ndipo ananyamuka kupita ku Makedoniya.
2 [After he arrived] there, he visited [each town where there were believers], and encouraged them. Then he arrived in Greece [province], [which is also called Achaia].
Iye anayendera madera a kumeneko, nalimbitsa mtima anthu, ndipo pomaliza pake anapita ku Grisi.
3 He stayed there for three months. Then he planned to return to Syria by ship, but [he heard that] some of the Jews [SYN] [in that area] were planning to kill him [as he traveled. So] he decided instead to go [by land, and he traveled] again through Macedonia.
Kumeneko anakhala miyezi itatu. Popeza kuti Ayuda anakonza zomuchita chiwembu pamene amati azinyamuka kupita ku Siriya pa sitima ya pamadzi, iye anaganiza zobwereranso kudzera ku Makedoniya.
4 The men who were going to travel with him [to Jerusalem were] Sopater, [who was] a son of Pyrrhus, who grew up in Berea [town]; Aristarchus and Secundus, who were from Thessalonica [city; ] Gaius, [who was] from Derbe [town; ] Timothy, [who was from Galatia province; ] and Tychicus and Trophimus who were from Asia [province].
Iye anapita pamodzi ndi Sopatro mwana wa Puro wa ku Bereya, Aristariko ndi Sekundo a ku Tesalonika, Gayo wa ku Derbe ndi Timoteyo, ndipo a ku Asiya anali Tukiko ndi Trofimo.
5 Those [seven] men went ahead of [Paul and me, Luke, by ship from Macedonia, so] they got to Troas [before we did and] waited for [the two of] us there.
Anthu amenewa anatsogola ndipo anakatidikira ku Trowa.
6 [But we two(exc) traveled by land as far as] Philippi [city]. After the Jewish festival [when they eat] unleavened bread, we got on a ship [that was going from] the port near [Philippi to Troas city]. After five days we [(exc)] arrived at Troas and we met the other men who had traveled there [ahead of us]. Then we [all] stayed in Troas for seven days.
Koma ife tinayenda pa sitima ya pamadzi kuchokera ku Filipi chitatha Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Patapita masiku asanu tinakumana nawo enawo ku Trowa, ndipo tinakhala kumeneko masiku asanu ndi awiri.
7 (On Sunday evening/On the evening of the first day of the week), we [(exc) and the other believers there] gathered together to celebrate the Lord’s Supper [and to eat other food] [SYN]. Paul spoke to the believers. He continued teaching them until midnight, because he was planning to leave [Troas] the next day.
Pa tsiku loyamba la Sabata, tinasonkhana kuti tidye mgonero. Paulo analalikira kwa anthu chifukwa anaganiza zoti achoke tsiku linalo, ndipo analalika mpaka pakati pa usiku.
8 Many [oil] lamps were burning in the upstairs room in which we [(exc)] had gathered, [so the fumes caused some people to become sleepy].
Munali nyale zambiri mʼchipinda chammwamba mʼmene tinasonkhanamo.
9 A young man whose name was Eutychus was there. He was seated on [the sill of] an [open] window [on the third story of the house]. As Paul continued talking for a long time, Eutychus became sleepier and sleepier. Finally, he was sound/really asleep. He fell [out of the window] from the third story down [to the ground. Some of the believers went down] immediately and picked him up. [But he was] dead.
Pa chipinda chachitatu chammwamba cha nyumbayo, pa zenera, panakhala mnyamata wina dzina lake Utiko, amene ankasinza pomwe Paulo amayankhulabe. Atagona tulo, iye anagwa pansi kuchokera pa chipinda chammwamba ndipo anamutola atafa.
10 Paul [also] went down. He lay down and stretched out on top of the young man and put his arms around him. Then he said [to the people who were standing around], “Do not worry, he is alive [again now]!”
Paulo anatsika, nadziponya pa mnyamatayo, namukumbatira. Paulo anati, “Musadandaule, ali moyo!”
11 Then Paul, [along with the others], went upstairs again and they ate the Lord’s Supper and other food [SYN]. Afterwards, Paul conversed with the believers until dawn. Then he left.
Kenaka Paulo anakweranso, mʼchipinda muja nanyema buledi nadya. Atayankhula mpaka kucha, anachoka.
12 The [other] people took the young man [home], and were greatly encouraged because he was alive [again].
Anthu anatenga mnyamatayo kupita kwawo ali moyo ndipo anatonthozedwa mtima kwambiri.
13 We then went to the ship. Paul did not get on the ship [with us in Troas], because he preferred to go [more quickly] overland to Assos [town]. The rest of us got on the ship and sailed for Assos.
Ife tinatsogola kukakwera sitima ya pa madzi kupita ku Aso, kumene tinayembekeza kukatenga Paulo. Iye anakonza motero chifukwa amayenda wapansi.
14 We [(exc)] met Paul in Assos. He got on [the ship] with us, and we sailed to Mitylene [town].
Pamene anakumana nafe ku Aso tinamutenga ndipo tinapita ku Mitilene.
15 The day after [we reached Mitylene], we [sailed from there and] arrived [at a place] near Kios [Island]. The day after that, we sailed to Samos [Island]. The next day we [left Samos and] sailed to Miletus [town].
Mmawa mwake tinachoka kumeneko pa sitima ya pamadzi ndipo tinafika pafupi ndi Kiyo. Tsiku linalo tinawolokera ku Samo, ndipo tsiku linanso tinafika ku Mileto.
16 [Miletus was just south of Ephesus city]. Paul had [earlier] decided that he would not get on a ship that would stop at Ephesus, because he did not want to spend [several] days in Asia [province]. If possible, he wanted to arrive in Jerusalem by the [time of the] Pentecost festival, [and the time of that festival was near].
Paulo anali atatsimikiza kuti alambalale Efeso kuopa kutaya nthawi ku Asiya, pakuti ankafulumira kuti akafike ku Yerusalemu kuti ngati nʼkotheka kuti tsiku la Pentekosite akakhale ali ku Yerusalemu.
17 [When the ship arrived at] Miletus, Paul sent [a messenger] to Ephesus to ask the elders of the congregation to come to talk with him.
Paulo ali ku Mileto, anatumiza mawu ku Efeso kuyitana akulu ampingo.
18 When the elders arrived, Paul said to them, “You personally know how I [conducted myself among you the entire time] that I was with you, from the first day when I arrived [here] in Asia [province until the day I left].
Iwo atafika, Paulo anati, “Inu mukudziwa mmene ndinakhalira nanu nthawi yonse imene ndinali nanu kuyambira tsiku loyamba limene ndinafika ku Asiya.
19 [You know how] I was serving the Lord [Jesus] very humbly and how I sometimes wept [about people. You also know how] I suffered because the Jews [SYN] [who were not believers often] tried [to harm me].
Ndinatumikira Ambuye modzichepetsa kwambiri ndiponso ndi misozi, ngakhale ndinayesedwa kwambiri ndi ziwembu za Ayuda.
20 You also know that, as I preached [God’s message] to you, I never left out anything that would help you. You know that I taught you [God’s message] when many people were present, and I [also went to your] homes and taught it there.
Inu mukudziwa kuti, sindinakubisireni kanthu kalikonse kopindulitsa koma ndinakuphunzitsani poyera komanso nyumba ndi nyumba.
21 I preached both to Jews and to non-Jews, telling them [all] that they must turn away from their sinful behavior. [I also told them they should] believe in our Lord Jesus.”
Ine ndinawuza Ayuda komanso Agriki kuti ayenera kutembenukira kwa Mulungu polapa ndikuti akhulupirire Ambuye athu Yesu.
22 “And now note this: I am going to Jerusalem, because [God’s] Spirit has clearly shown me that I must go there. I do not know what will happen to me [while I am there].
“Ndipo tsopano, mokakamizidwa ndi Mzimu, ndikupita ku Yerusalemu, sindikudziwa zimene zikandichitikire kumeneko.”
23 But I do know that in each city [where I have stopped], the Holy Spirit has (told me/[caused the believers to] tell me) that [in Jerusalem] people will put me in prison [PRS] and will cause me to suffer [PRS].
Chimene ndikudziwa ndi chakuti Mzimu Woyera wandichenjeza mu mzinda uliwonse kuti ndende ndi mavuto zikundidikira.
24 But I do not care even if people kill me, if first I am able to finish the work [MET] that the Lord Jesus has told me [to do. He appointed me] to tell people the good message that God [saves us] by doing for us what we do not deserve.
Koma sindilabadira konse za moyo wanga ngati kuti ndi wa mtengo wapatali kwa ine, malingana ndikatsirize ntchito yanga ndi utumiki umene Ambuye Yesu anandipatsa, ntchito yochitira umboni Uthenga Wabwino wachisomo cha Mulungu.
25 I have preached to you the message about how God desires to rule [people’s lives]. But now I know that today is the last time that you fellow believers will see me [SYN].
“Tsopano ndikudziwa kuti inu nonse amene ndinakuyenderani ndi kumakulalikirani ufumu wa Mulungu simudzaonanso nkhope yanga.
26 So I want you all to understand that if anyone [who has heard me preach] dies [without trusting in Jesus], it is not my fault [MTY],
Chifukwa chake, ine ndikukuwuzani lero kuti ndilibe mlandu ndi munthu aliyense.
27 because I told you [LIT] everything [HYP] that God has planned for us [(inc)].
Pakuti sindinakubisireni pokulalikirani chifuniro chonse cha Mulungu.
28 [You leaders] must continue to believe and obey [God’s message. You must also help] all the other believers [MET] for whom the Holy Spirit has caused you to be responsible [MTY]. Watch over [MET] yourselves and the other believers [as] a shepherd [watches over his sheep]. God bought them with the blood [that flowed from] his [Son’s body on the cross].
Mudziyangʼanire nokha ndiponso muyangʼanire gulu lankhosa limene Mzimu Woyera anakuyikani kuti mukhale oyangʼanira ake. Khalani abusa a mpingo wa Mulungu umene Iye anawugula ndi magazi ake.
29 I know [very well] that after I leave, [people who teach] [MET] [false doctrines] will come among you and will do great harm to the believers. [They will be like] fierce wolves [that kill sheep].
Ndikudziwa kuti ndikachoka ine, padzafika mimbulu yolusa pakati panu imene sidzalekerera gulu lankhosalo.
30 Even in your own group of believers there will be some who will deceive [other] believers by teaching them messages that are false. They will teach those messages so that some people [will believe them and] will become their followers.
Ngakhale pakati pa inu nokha padzapezeka anthu oyankhula zonama ndi cholinga chofuna kukhala ndi ophunzira kuti awatsate.
31 So watch out [that none of you stops believing the true message about our Lord Jesus]. Remember that day and night for [about] three years I repeatedly taught you that message, and warned you with tears [in my eyes not to believe any other message].”
Tsono inu, samalani! Kumbukirani kuti kwa zaka zitatu, usana ndi usiku ndiponso ndi misozi sindinaleke kuchenjeza aliyense wa inu.
32 “[Now as I leave you], I ask God to protect you and to keep you believing the message [that he saves us(inc)] by doing for us what we do not deserve. [If you continue believing] the message [that I told you], you will become [spiritually mature], and God will give you the blessings that he has promised to give to all of those who belong to him.
“Tsopano ine ndikukuperekani kwa Mulungu ndiponso kwa mawu a chisomo chake, amene ali ndi mphamvu zokulitsa inu ndi kukupatsani chuma pakati pa onse amene anayeretsedwa.
33 [As for myself], I have not desired anyone’s money [MTY] or [fine] clothing.
Ine sindinasirire siliva kapena golide kapena zovala za munthu aliyense.
34 You yourselves know that I have worked [with my hands] [MTY] to earn the money that my companions and I needed.
Inu nomwe mukudziwa kuti manja angawa ananditumikira kuti tipeze zimene ine ndi anzanga tinkazifuna.
35 In everything that I did, I showed you that we [(inc)] should work hard in order [to have enough money] to give some to those who are needy. We [(inc)] should remember that our Lord Jesus himself said, ‘You are happy when people give you what you need, but God will be happy with you when you give other people what they need.’”
Pa zonse zimene ndinachita, ndinakuonetsani kuti pogwira ntchito molimbika motere tiyenera kuthandiza ofowoka, pokumbukira mawu a Ambuye Yesu akuti, ‘Kupereka kumadalitsa kuposa kulandira.’”
36 When Paul had finished speaking, he knelt down with all of the elders and prayed.
Atanena zimenezi, anagwada pansi pamodzi ndi ena onse, napemphera.
37 They all cried a lot, and they hugged Paul and kissed him.
Onse analira pamene amamukumbatira ndi kupsompsona.
38 They were especially sad because he had said that they would never see him [SYN] again. Then they [all] went with him to the ship.
Chimene chinamvetsa chisoni kwambiri ndi mawu ake akuti sadzaonanso nkhope yake. Kenaka iwo anamuperekeza ku sitima yapamadzi.