< Acts 11 >

1 The apostles and [other] believers who lived in various towns in Judea [province] heard people say that [some] non-Jewish people had believed the message [from] God [about Jesus].
Atumwi ndi abale a ku Yudeya konse anamva kuti anthu a mitundu ina analandiranso Mawu a Mulungu.
2 So when Peter [and the six other believers] returned [from Caesarea] to Jerusalem, [some] Jewish believers criticized Peter, [because they thought that Jews should not associate with non-Jews] [MTY].
Tsono Petro atafika ku Yerusalemu, abale amene anali a mdulidwe anamutsutsa iye,
3 They said to him, “Not only was it wrong for you(sg) to visit non-Jewish people, you [even] ate with them!”
ndipo anati, “Iwe unalowa mʼnyumba ya anthu osachita mdulidwe ndi kudya nawo.”
4 So Peter began to explain exactly [what had happened concerning Cornelius].
Koma Petro anayamba kuwafotokozera zonse mwatsatanetsatane momwe zinachitikira kuti,
5 He said, “I was praying [by myself] in Joppa [town], and in a trance I saw a vision. I saw that something like a large sheet was being lowered from heaven. [It was tied with ropes] at its four corners, and it came down to where I was.
“Ine ndimapemphera mu mzinda wa Yopa ndipo ndili ngati wokomoka ndinaona masomphenya. Ndinaona chinthu chokhala ngati chinsalu chachikulu chikutsika kuchokera kumwamba chogwiridwa msonga zake zinayi, ndipo chinatsikira pa ine.
6 As I was looking intently into it, I saw some tame animals [but also animals that our laws forbid us to eat, including] wild animals, snakes, and wild birds.
Ine ndinayangʼana mʼkati mwake ndipo ndinaona nyama za miyendo inayi za mʼdziko lapansi, zirombo, zokwawa, ndi mbalame zamlengalenga.
7 Then I heard God [MTY] commanding me, ‘Peter, get up, kill [some of these], and [cook and] eat [their meat]!’
Kenaka ine ndinamva mawu akuti, ‘Petro, Imirira. Ipha, nudye.’
8 But I replied, ‘Lord, [you(sg)] surely do not [really want me to do that], because I have never eaten [MTY] meat [from any animal] that [our laws say] that we [(exc)] must not eat [SYN]!’
“Ine ndinayankha kuti, ‘Ayi, Ambuye! Pakuti chinthu chodetsedwa ndi chonyansa sindinadyepo pakamwa pangapa.’
9 God spoke from heaven [to me] a second time, ‘[I am] God, [so] if I have made something acceptable [to eat], do not say that it is not acceptable [to eat]!’
“Mawu ochokera kumwamba ananenanso kachiwiri kuti, ‘Chimene Mulungu wachiyeretsa usanene kuti ndi chodetsedwa.’
10 Then [after that happened three times, the sheet with] all [those animals and birds] was pulled up into heaven again.”
Zimenezi zinachitika katatu ndipo kenaka zonse zinatengedwa kupita kumwamba.
11 “At that exact moment, three men who had been {whom [Cornelius] had} sent from Caesarea arrived at the house where I was staying.
“Nthawi yomweyo anthu atatu amene anatumidwa kuchokera ku Kaisareya anayima pa nyumba yomwe ndimakhalayo.
12 [God’s] Spirit told me that I should be willing to go with them [even though they were not Jews]. These six [Jewish] believers [from Joppa] went with me [to Caesarea], and then we [(exc)] went into that [non-Jewish] man’s house.
Mzimu anandiwuza kuti ndisakayike, koma ndipite nawo. Abale asanu ndi mmodzi awa anapitanso nane ndipo tinalowa mʼnyumba ya munthuyo.
13 He told us that he had seen an angel standing in his house. The angel told him, ‘Tell some [men] to go to Joppa and bring back Simon whose other name is Peter.
Iye anatiwuza mmene anaonera mngelo atayimirira mʼnyumba mwake ndi kumuwuza kuti, ‘Tumiza anthu ku Yopa kuti akayitane Simoni wotchedwa Petro.
14 He will tell you [(sg)] how you and everyone [MTY] else in your house will be saved {how [God] will save you and everyone [MTY] else in your house}.’
Iye adzakuwuza uthenga umene udzapulumutsa iwe ndi a pa banja ako.’
15 After I started to speak, the Holy Spirit [suddenly] came down on them, just like he had first [MTY] come on us [during the Pentecost festival].
“Nditangoyamba kuyankhula, Mzimu Woyera anafika pa iwo monga momwe anafikira pa ife poyamba paja.
16 Then I remembered what the Lord had said: ‘John caused people to be baptized in water, but [God] will cause the Holy Spirit [to enter you and change your lives.’]
Kenaka ndinakumbukira zimene Ambuye ananena kuti, ‘Yohane anabatiza ndi madzi, koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.’
17 God gave those non-Jews the same Holy Spirit that he had given to us [(inc)] after we believed in the Lord Jesus Christ. So, ([I] could not [possibly] tell God that he did wrong [when he gave them the Holy Spirit!]/how could I [tell] God that he did wrong [when he gave them the Holy Spirit]?) [RHQ] [He was showing that he had received them]!”
Tsono ngati Mulungu anawapatsa iwo mphatso yomweyo imene anatipatsa ife, amene tinakhulupirira Ambuye Yesu Khristu, ndine yani kuti nditsutsane ndi Mulungu?”
18 After [those Jewish believers] heard what Peter said, they stopped criticizing [him. Instead], they praised God, saying, “Then it is [clear to us that] God has also accepted the non-Jews so that they will have eternal life, if they turn from their sinful behavior [and believe in Jesus]!”
Iwo atamva zimenezi analibenso chonena ndipo anayamika Mulungu nati, “Potero Mulungu wapatsa anthu a mitundu ina mwayi wotembenuka mtima ndi kulandira moyo.”
19 After [people had killed] Stephen, many of the believers left [Jerusalem and went] to other places, because people were causing them to suffer [there in Jerusalem. Some of] them went to Phoenicia [region], some went to Cyprus [Island], and others went to Antioch [city in Syria province. In those places] they were continually telling people the message [about Jesus], but they told only other Jewish people.
Tsopano amene anabalalika chifukwa cha mazunzo amene anayamba ataphedwa Stefano, anapita mpaka ku Foinike, ku Kupro ndi ku Antiokeya, ndipo ankalalikira kwa Ayuda okha.
20 Some of the believers were men from Cyprus and from Cyrene [city in north Africa]. They went to Antioch, and [although they told other Jews about] the Lord Jesus, they also told non-Jewish people [there].
Komabe, ena pakati pawo ochokera ku Kupro ndi ku Kurene anapita ku Antiokeya ndipo iwo anayamba kuyankhulanso kwa Agriki, nawawuza za Uthenga Wabwino wa Ambuye Yesu.
21 The Lord [God] [MTY] was powerfully enabling those [believers to preach effectively. As a result], very many [non-Jewish] people believed [their message and] trusted in the Lord [Jesus].
Mphamvu ya Ambuye inali nawo ndipo anthu ambiri anakhulupirira natembenukira kwa Ambuye.
22 The group of believers in Jerusalem heard [MTY] [people say that many people in Antioch were believing in Jesus. So] the [leaders] of the congregation in [Jerusalem] asked Barnabas to go to Antioch.
Mbiri imeneyi inamveka ku mpingo wa ku Yerusalemu ndipo iwo anatumiza Barnaba ku Antiokeya.
23 When he got [there], he realized that God had acted kindly toward [the believers. So] he was very happy, and he continually encouraged all of the [believers] to continue to trust completely in the Lord [Jesus].
Atafika ndi kuona chisomo cha Mulungu pa iwo, anakondwa ndi kuwalimbikitsa anthu onsewo kuti apitirire kukhala woona mu mtima mwa Ambuye.
24 Barnabas was a good man [whom] the Holy Spirit completely controlled, one who trusted [God] completely. [Because of what Barnabas did], many people [there] believed in the Lord [Jesus].
Barnabayo anali munthu wabwino, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi chikhulupiriro ndipo gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Ambuye.
25 Then Barnabas went to Tarsus [in Cilicia province to try] to find Saul.
Kenaka Barnaba anapita ku Tarisisi kukafuna Saulo,
26 After he found him, Barnabas brought him [back to] Antioch [to help teach the believers. So during] a whole year [Barnabas and Saul] met [regularly] with the congregation [there] and taught many of them [about Jesus. It was] at Antioch that the believers were first called Christians {[that people] first called the believers Christians}.
ndipo pamene anamupeza anabwera naye ku Antiokeya. Barnaba ndi Saulo anasonkhana ndi mpingo kwa chaka chimodzi naphunzitsa anthu ambirimbiri. Okhulupirirawo anayamba kutchedwa Akhristu ku Antiokeya.
27 During the time [that Barnabas and Saul were] at Antioch, some [believers who were] prophets arrived there from Jerusalem.
Masiku amenewo ku Antiokeya kunafika aneneri ena ochokera ku Yerusalemu.
28 One of them, whose name was Agabus, stood up [in order to speak]. [God’s] Spirit enabled him to prophesy (that there would soon be a famine in many countries/that [people] in many countries [HYP] would soon [suffer because they] would not have enough [food] to eat). (That famine happened when Claudius was the [Roman Emperor].)
Mmodzi wa iwo dzina lake Agabu, anayimirira ndipo Mzimu anamutsogolera kunenera zamʼtsogolo kuti padzakhala njala yayikulu pa dziko lonse lapansi. (Izi zinachitikadi nthawi ya ulamuliro wa Klaudiyo).
29 When the believers [there heard what Agabus said], they decided that they would send [money] to help the believers who lived in Judea. Each [of them decided to give as much money] as he was able [to give].
Ophunzirawo, aliyense monga mwakupata kwake, anatsimikiza kuthandiza abale okhala ku Yudeya.
30 They sent [the money] with Barnabas and Saul to the leaders of the congregation [in Jerusalem].
Izi anazichitadi ndipo anatuma Barnaba ndi Saulo kukapereka mphatsozo kwa akulu a mpingo.

< Acts 11 >