< 3 John 1 >
1 [You(sg) know me as] the [chief] Elder. [I am writing this letter to you], my dear friend Gaius, whom I truly love.
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.
2 Dear friend, I ask [God that things may go] well for you in every way, [specifically], that you will be physically healthy just like you are spiritually healthy [MTY].
Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu.
3 I am very happy because some fellow believers have come [here] and told me that you conduct your life in a manner [that is consistent with God’s] true message.
Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi.
4 I am very happy when I hear that (people whom I helped to believe in Christ/my [spiritual] children) are conducting their lives like you are!
Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.
5 Dear friend, you are [serving Jesus] loyally/faithfully whenever you do things to help fellow believers, [even those whom you] do not know, who are traveling [around doing God’s work].
Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo.
6 [Some of] them have reported before the congregation [here how] you have showed that you love them. You should continue to help such people in their travels in a way that is pleasing to God.
Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu.
7 When those fellow believers went out [to tell people about Jesus] [MTY], the people who do not believe in Christ did not give them anything [to help them].
Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira.
8 So we [who believe in Christ] ought to give food and money to such people to help [them as they teach others God’s] true message.
Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.
9 I wrote [a letter] to the congregation [telling them to help those fellow believers]. However, Diotrephes does not (acknowledge my authority/[pay any attention to what] I wrote), because he (desires to be in charge/wants to be the leader) of [the congregation].
Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera.
10 So, when I arrive [there], I will [publicly] tell what he does: He tells others evil nonsense about us [in order to] harm [us by what he] says, and he is not content with only doing that. He himself refuses to receive the fellow believers who are traveling around doing God’s work, and he also stops those who want to receive them by expelling them from the congregation.
Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.
11 Dear friend, do not imitate a bad [example like that]. Instead, [keep imitating] good [examples. Remember that] people who do good deeds ([truly] belong to God/are [spiritual children] of God), [but] those who do [what is] evil do not (know/have fellowship with) God.
Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu.
12 All [the believers who know Demetrius] say that he [is a good person]. The fact [that he conducts his life in a way that is consistent/in accordance with God’s] true [message] shows [that he is a good person], and we also say the same thing [about him]. You know that what we say [about him] is true. [So it will be good if you welcome him and help him. He is the one who will be bringing this letter to you].
Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.
13 [When I began] to write this letter, I had much more [that I intended] to tell you. But [now] I do not want to say [it] in a letter [MTY].
Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata.
14 Instead, I expect to [come and] see you soon. Then we will talk directly with one another. [I pray that God will enable] you [to experience inner] peace. Our friends [here] (send you their greetings/say that they are thinking affectionately about you) [MTY]. Tell our friends [there] that we (send our greetings to/are thinking fondly about) them.
Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso. Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.