< 2 Samuel 24 >
1 Yahweh was angry with the Israeli people again, so he incited David to cause trouble for them. He said to David, “Send [some men] to count the people of Israel and Judah.”
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 So the king said to Joab, the commander of his army, “Go [with your officers] through all the tribes of Israel, from Dan [city in the far north] to Beersheba [town in the far south], and count the people, in order that I may know how many people [there are who are able to be soldiers in the army].”
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 But Joab replied to the king, “Your Majesty, I wish/desire that Yahweh our God will cause there to be 100 times as many people [in Israel] as there are now, and I wish/desire that you would see that happen [before you die]. But why do you want us to do this?”
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 But the king commanded Joab and his officers to do it. So they left the king and went out to count the people of Israel.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 They crossed the Jordan [River] and set up their tents south of Aroer [town], in the middle of the valley, in the territory [that was given to the tribe] of Gad. From there they went [north] to Jazer [city]
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 Then they went [north] to [the] Gilead [region] and to Kadesh [city], in the land where the Heth people-group lived. Then they went to Dan [city in the far north of Israel], and then further west, to Sidon [city near the Mediterranean Sea].
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 Then they went [south] to Tyre, a city with high walls around it, and to all the cities where the Hiv and Canaan people-groups live. Then they went [east] to Beersheba, in the southern part of Judah.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 After nine months and 20 days, when they had finished going throughout the land [and counting the people], they returned to Jerusalem.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 They reported to the king the number of people that they had counted. There were 800,000 men in Israel and 500,000 men in Judah who were able to become soldiers in the army [MTY].
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 But after David’s men had counted the people, David regretted [IDM] that he had told them to do that. [One night] he said to Yahweh, “I have committed a very big sin. Please forgive me, because what I have done is very foolish.”
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 When David got up the next morning, Yahweh gave a message to the prophet Gad. He said to him,
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 “Go and tell this to David: ‘I am allowing you to choose one of three things [to punish you]. I will do whichever one you choose.’”
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 So Gad went to David and told him [what Yahweh had said]. He said to David, “You can choose whether there will be three years of famine in your land, or three months of your [army] running away from your enemies, or three days when there will be a (plague/very severe illness) in your land. You think about it and choose [which one you want, and tell me], and I will return to Yahweh and tell him what your answer is.”
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 David said to Gad, “All those are very terrible things for me to choose between! But allow Yahweh to punish [MTY] me, because he is very merciful. Do not allow humans to punish me, [because they will not be merciful].”
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 So Yahweh sent a plague on the Israeli people. It started that morning and did not stop until the time that he had chosen/set. All over the land, from Dan to Beersheba, there were 70,000 Israelis who died [because of the plague].
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 When [Yahweh’s] angel stretched out his hand toward Jerusalem to destroy [the people by this plague], Yahweh changed his mind about punishing [any more] people. He said to the angel who was killing them [with the plague], “Stop what you are doing [IDM]! That is enough!” [When he said that, ] the angel was standing at the ground where Araunah, from the Jebus people-group, threshed grain.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 When David saw the angel who was causing the people to become sick and die, he said to Yahweh, “Truly, I am the one who has committed the sin. I have done a very wicked thing, but these people are [as innocent as] sheep [MET]. They have certainly not [RHQ] done anything [that is wrong]. So you should punish [IDM] me and my family, [not these people]!”
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 That day Gad came to David and said to him, “Go up to the place where Araunah threshes grain, and build an altar to [worship] Yahweh there.”
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 So David did what Gad told him to do, which was what Yahweh had commanded, [and he went up there].
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 When Araunah looked down and saw the king and his officials coming toward him, he prostrated himself on the ground in front of the king, with his face touching the ground.
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 Araunah said, “Your Majesty, why have you come to me?” David replied, “[I have come] to buy this ground where you thresh grain, in order to build an altar to Yahweh [and offer sacrifices on it], in order that he will stop the plague.”
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 Araunah replied to David, “Your Majesty, offer to Yahweh whatever you wish/want. Here, take my oxen to use for the offering that will be completely burned on the altar. And here, take their yokes and the boards [that I use] for the threshing, [and use them] for the wood that you will burn.
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 I, Araunah, am giving all this to you, the king.” Then he said, “I desire/hope that Yahweh our God will accept your offering.”
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 But the king said to Araunah, “No, [I will not take these things as a gift.] I will pay you for it. I will not take sacrifices that have cost me nothing, and offer them to Yahweh to be completely burned on the altar.” So he paid 50 pieces of silver to Araunah for the oxen and the ground.
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 Then David built an altar to Yahweh, and he offered [the oxen] to be completely burned on the altar, and he also offered sacrifices to maintain fellowship with Yahweh. Then, Yahweh answered David’s prayers, and he caused the plague in Israel to end.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.