< 2 Kings 8 >

1 After Elisha caused the son of the woman from Shunem [town] to become alive again, he told her that she should leave with her family and live somewhere else for a while, because Yahweh was going to (send a famine/cause food to become very scarce) in the land. He said that the famine would last for seven years.
Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
2 So the woman did what Elisha told her to do. She and her family went to live in [the] Philistia [region] for seven years.
Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
3 After the seven years were ended, they returned to their home. The woman went to the king to request that her house and her land be given back to her.
Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
4 When she arrived, the king was talking with Gehazi, Elisha’s servant. The king was saying to him, “Tell me all the great things that Elisha has done.”
Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
5 While Gehazi was telling the king that Elisha had caused the son of a woman [from Shunem] to become alive again, that woman came in and requested the king to enable her to get her house and land back again. Gehazi exclaimed, “Your Majesty, this is the woman whose son Elisha caused to become alive again!”
Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
6 When the king asked her about it, she told him [that what Gehazi had said was true]. The king summoned one of his officials and said to him, “[I want] everything that this woman possessed previously, including the value of all the crops that have been harvested during these last seven years while she was away from her land, [to] be given back to her.” [So the official did that].
Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
7 Elisha went to Damascus, [the capital of Syria], when Ben-Hadad, the king of Syria, was [very] sick. When someone told the king that Elisha was in Damascus,
Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
8 the king told [one of his officials named] Hazael, “Go and talk to that prophet and take a present/gift with you to give to him. Request him to ask Yahweh if I will recover from my illness.”
inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
9 So Hazael went to talk with Elisha. He took with him forty camels that were carrying many kinds of goods that were produced in Damascus. When Hazael met him, he said to him, “Your friend Ben-Hadad, the king of Syria, sent me to ask you whether [you think] he will recover from his illness.”
Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
10 Elisha said to Hazael, “Go and say to him, ‘Yes, you will certainly not die from this illness,’ but Yahweh has shown me that he will certainly die [before he recovers].”
Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
11 Then Elisha stared at him and had a terrified look on his face. That caused Hazael to feel uneasy/embarrassed. Then [suddenly] Elisha started to cry.
Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
12 Hazael said, “Sir, why are you crying?” Elisha replied, “Because [Yahweh has enabled] me [to] know the terrible things that you will do to the people of Israel: You will burn their cities with walls around them, you will kill their fine young men with a sword, you will bash the heads of their children, and you will rip open the bellies of their pregnant women [with a sword].”
Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
13 Hazael replied, “I am [as insignificant as] [MET] a dog; (how could I do such things?/I would never do such terrible things!)” [RHQ] Elisha replied, “Yahweh has also revealed to me that you will become the king of Syria.”
Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
14 Then Hazael left and returned to his master/boss [the king], who asked him, “What did Elisha say?” He replied, “He told me that you would certainly recover.”
Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
15 But the next day, [while the king was sleeping, ] Hazael took a blanket and soaked it in water. Then he spread it on the king’s face [in order that he could not breathe], and he died. Then Hazael became the king of Syria instead of Ben-Hadad.
Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
16 After King Joram, the son of Ahab, had been ruling in Israel for almost five years, Jehoshaphat’s son Jehoram became the king of Judah.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
17 He was thirty-two years old when he became the king, and he ruled in Jerusalem for eight years.
Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
18 His wife was the daughter of King Ahab. And like everyone in Ahab’s family, he continually did the evil things that the previous kings of Israel had done. He did things that Yahweh considered to be evil.
Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
19 But Yahweh did not want to get rid of the people of Judah, because of what he had promised David, who served him [very well]. He had promised David that his descendants [MET] would always rule Judah.
Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
20 During the time that Jehoram ruled, [the king of] Edom rebelled against Judah, and they appointed their own king.
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
21 So Jehoram went with his army and all their chariots to Zair [city near the border of Edom]. There the army of Edom surrounded them. But during the night, Jehoram and the commanders in their chariots were able to get through the enemy lines and escaped. And all his soldiers also fled to their homes.
Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
22 So after that, Edom was no longer controlled by Judah, and it is still like that. During that same time, the people of Libnah [city] also freed themselves from being controlled by Judah.
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
23 [If you want to read about] the other things that Jehoram did, they are written in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah’.
Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
24 Jehoram died [EUP] and was buried where the other kings of Judah had been buried in [the part of Jerusalem called] ‘The City of David’. Then Jehoram’s son Ahaziah became the king.
Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 After Ahab’s son Joram has been ruling in Israel for almost twelve years, Jehoram’s son Ahaziah became the king of Judah.
Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
26 Ahaziah was twenty-two years old when he started to rule. He ruled in Jerusalem for [only] one year. His mother’s name was Athaliah, [the daughter of King Ahab and] the granddaughter of King Omri of Israel.
Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
27 King Ahab conducted his life just like the members of Ahab’s family had done. He did things that Yahweh considered to be very evil.
Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
28 Ahaziah’s army joined the army of King Joram of Israel to fight against the army of King Hazael of Syria. Their armies started fighting at Ramoth [city] in [the] Gilead [region], and the soldiers of Syria wounded Joram.
Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
29 King Joram returned to Jezreel [city] to recover from his wounds. King Ahaziah went to visit him there.
Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.

< 2 Kings 8 >