< 2 Kings 3 >

1 After Jehoshaphat had been ruling Judah for almost 18 years, Ahab’s son Joram became the king of Israel. He ruled in Samaria [city] for twelve years.
Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
2 He did things that Yahweh considered to be evil, but he did not do as much evil as his father and mother had done, and he got rid of the pillar [for worshiping] Baal which his father had made.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
3 But he committed the sins that [King] Jeroboam had committed and which led the Israeli people to sin, and he did not stop committing those sins.
Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
4 Mesha, the king of Moab, raised sheep. [Every year] he was forced to give 100,000 lambs and the wool from 100,000 rams to the king of Israel, [because his kingdom was controlled by the king of Israel].
Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
5 But after King Ahab died, Mesha rebelled against the king of Israel.
Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
6 So King Joram left Samaria and gathered together all his soldiers.
Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
7 Then he sent this message to Jehoshaphat, the king of Judah: “The king of Moab has rebelled against me. So will your army join my army and fight against the army of Moab?” Jehoshaphat replied, “Yes, we will help you. We are ready to do whatever you want us to. My soldiers and my horses are ready to help you.”
Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
8 He asked, “On which road shall we march to attack them?” Joram replied, “We will go [south to Jerusalem, where your army will join us. Then we will all go south of the Dead Sea, and then turn north] through the Edom Desert.”
Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
9 So the king of Israel [and his army] went with the kings of Judah and Edom [and their armies]. They marched for seven days. Then there was no water left for their soldiers or for their animals that carried supplies.
Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
10 The king of Israel exclaimed, “This is a terrible situation! [It seems that] Yahweh will allow the three of us to be captured by [the army of] [MTY] Moab!”
Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
11 Jehoshaphat said, “Is there a prophet here who can ask Yahweh for us [what we should do]?” One of Joram’s army officers said, “Elisha, the son of Shaphat, is here. He was Elijah’s assistant.” [IDM]
Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
12 Jehoshaphat said, “[It will be good to ask him, because] he speaks what Yahweh tells him to say.” So those three kings went to Elisha.
Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
13 Elisha said to the king of Israel, “Why do you come to me [RHQ]? Go and ask those prophets that your father and mother consulted!” But Joram replied, “No, [we want you to ask Yahweh, because it seems that] Yahweh is going to allow us three kings to be captured by the army of Moab.”
Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
14 Elisha replied, “I serve Yahweh, the commander of the armies of angels in heaven. As surely as he lives, if I did not respect Jehoshaphat the king of Judah, I would not even think about doing anything to help you.
Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
15 But, bring a musician to me.” [So they did that]. And when the musician played [on his harp], the power of Yahweh came on Elisha.
Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
16 He said, “Yahweh says that he will cause this dry stream-bed to be full of water.
ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
17 The result will be that your soldiers and your animals that carry supplies and your livestock will have plenty of water to drink.
Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
18 That is not difficult for Yahweh to do. [But he will do more than that]. He will also enable you to defeat [the army of] Moab.
Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
19 You will conquer all their beautiful cities, cities that have high walls around them. You must cut down all their fruit trees, stop water from flowing from their springs, and ruin their fertile fields by covering them with rocks.”
Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
20 The next morning, at the time when they offered the sacrifices [of grain], they were surprised to see water flowing from Edom and covering the ground.
Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
21 When the people of Moab heard that the three kings had come [with their armies] to fight against them, all the men who were able to fight in battles, from the youngest men to the oldest ones, were summoned, and they (took their positions/prepared to fight) at the [southern] border of their land.
Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
22 But when they rose early the next morning, they saw that the water across from them appeared to be as red as blood.
Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
23 They exclaimed, “It is blood! The three enemy armies must have fought and killed each other! So let’s go and take everything that they have left!”
Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
24 But when they reached the area where the Israeli soldiers had set up their tents, the Israelis attacked the soldiers from Moab and forced them to retreat. The Israeli soldiers pursued the soldiers from Moab and killed many of them.
Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
25 The Israelis also destroyed their cities. And whenever they passed fertile fields, they threw rocks on those fields, until the fields were covered with rocks. They stopped water from flowing from the springs and cut down the fruit trees. Finally, only [the capital city, ] Kir-Hareseth, remained. The Israeli soldiers who threw stones with slings surrounded the city and attacked it.
Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
26 When the king of Moab realized that his army was being defeated, he took with him 700 men who fought with swords, and they tried to force a way through the Israeli lines of soldiers to escape to [get help from] the king of Syria, but they were unable to escape.
Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
27 Then the king of Moab took his oldest son, who would have become the next king, and killed him and offered him for a sacrifice [to their god Chemosh], burning him on top of the city wall. The Israeli soldiers were horrified, with the result that they left that city and returned to their own country.
Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.

< 2 Kings 3 >