< 2 Kings 25 >

1 On January 15 of the ninth year that Zedekiah had been ruling, King Nebuchadnezzar arrived with his whole army, and they surrounded Jerusalem. They built ramps [made of dirt against the walls of the city], so that they could climb up the ramps and attack the city.
Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
2 They did that for two years.
Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
3 After Zedekiah had been ruling for eleven years, the (famine/shortage of food) had become very bad. All their food was gone.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
4 On July 18 of that year, the Babylonian soldiers broke through part of the city wall, [and that enabled them to enter the city]. All the soldiers of Judah [wanted to escape]. But the Babylonian soldiers surrounded the city, so the [king and] the soldiers of Judah waited until it was nighttime. Then they fled through the gate that was between the two walls near the king’s park. They ran across the fields and started to go down to the Jordan [River] Valley.
Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
5 But the Babylonian soldiers chased/ran after them. They caught the king when he was by himself in the valley near the Jordan River. He was by himself because all his soldiers had abandoned him.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
6 The Babylonian soldiers took King Zedekiah to Riblah [city] in Babylon. There the king of Babylon decided what they would do to punish him.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
7 There the king of Babylon forced Zedekiah to watch as the Babylonian soldiers killed all of Zedekiah’s sons. Then they gouged out Zedekiah’s eyes. They put bronze chains on [his hands and feet] and then they took him to Babylon.
Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
8 On August 14 of that year, after Nebuchadnezzar had been ruling for 19 years, Nebuzaradan arrived in Jerusalem. He was one of king Nebuchadnezzar’s officials and captain of the men that guarded the king.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
9 He [commanded his soldiers to] burn down the temple of Yahweh, the king’s palace, and all the houses in Jerusalem. So they burned down all the important buildings in the city.
Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
10 Then Nebuzaradan supervised all the soldiers of the Babylonian army as they tore down the walls of Jerusalem.
Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
11 Then he and his soldiers took to Babylon the people who were still living in the city, the other people [who lived in that area], and the soldiers who had previously surrendered to the Babylonian army.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
12 But Nebuzaradan allowed some of the very poor people to stay in Judah to take care of the vineyards and [to plant crops in] the fields.
Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
13 The Babylonian soldiers broke into pieces the bronze pillars, the bronze carts with wheels, and the huge bronze basin, all of which were in the temple courtyard, and they took all the bronze to Babylon.
Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
14 They also took the pots, the shovels, the instruments for (snuffing out/extinguishing) [the wicks of] the lamps, the dishes, and all the other bronze items that the Israeli priests had used for offering sacrifices at the temple.
Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
15 The soldiers also took away the (firepans/trays for carrying burning coals), the basins, and [all the other] items made of pure gold or pure silver.
Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
16 The bronze from the two pillars, the carts with wheels, and the huge basin were very heavy; they could not be weighed. (Those things had been made/A man named Hiram had made these things) for the temple when Solomon [was the king of Israel].
Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
17 Each of the pillars was (27 feet/8 meters) tall. The bronze capital/top of each pillar was (7-1/2 feet/2.3 meters) high. They were each decorated all around with something that looked like a net made of bronze chains connecting bronze pomegranates.
Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
18 Nebuzaradan took with him to Babylon Seraiah the Supreme Priest, Zephaniah his assistant, and the three men who guarded the entrance [to the temple].
Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
19 And they found people who were still hiding in Jerusalem. From those people he took one officer from the Judean army, five of the king’s advisors, the chief secretary of the army commander who was in charge of recruiting men to join the army, and 60 other important Judean men.
Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
20 Nebuzaradan took them all to the king of Babylon at Riblah [city].
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
21 There at Riblah, in Hamath province, the king of Babylon commanded that they all be executed. That is what happened when the people of Judah were (taken forcefully/exiled) from their land [to Babylon].
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
22 Then King Nebuchadnezzar appointed Gedaliah, who was the son of Ahikam and grandson of Shaphan, to be the governor of the people who were still living in Judah.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
23 When all the army captains of Judah and their soldiers who had not surrendered to Nebuchadnezzar found out that the king of Babylon had appointed Gedaliah to be the governor, they met with him at Mizpah [town]. These army captains were Ishmael the son of Nethaniah, Johanan the son of Kareah, Seraiah the son of Tanhumeth from Netophah [town], and Jaazaniah from the Maacah region.
Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
24 Gedaliah solemnly promised them [that the officials from Babylon were not planning to harm them]. He said, “You may live in this land [without being afraid] and serve the king of Babylon, and [if you do], everything will go well for you.”
Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
25 But in October of that year, Ishmael, whose grandfather Elishama was one of the relatives of the descendants of King David, went to Mizpah along with ten other men and assassinated/killed Gedaliah and all the men who were with him. There were also men from Judah and men from Babylon whom they assassinated.
Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
26 Then many [HYP] of the people from Judah, important people and unimportant ones, and the army captains, were very afraid of [what] the Babylonians [would do to them], so they fled to Egypt.
Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
27 Thirty-seven years after King Jehoiachin of Judah was taken to Babylon, [Nebuchadnezzar’s son] Evil-Merodach became the king of Babylon. He was kind to Jehoiachin, and on April 2 of that year, he released/freed Jehoiachin from prison.
Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
28 He always spoke kindly to Jehoiachin and honored him more than the other kings who had been taken/exiled to Babylon.
Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
29 He gave Jehoiachin new clothes to replace the clothes that he had been wearing in prison, and he allowed Jehoiachin to eat at the king’s table every day for the rest of his life.
Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
30 The king of Babylon also gave him money every day, so that he could buy the things that he needed. The king continued to do that until Jehoiachin died.
Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.

< 2 Kings 25 >