< 2 Kings 24 >
1 While Jehoiakim was ruling [Judah, the army of] King Nebuchadnezzar of Babylon invaded Judah. [They defeated the Judean army, and as a result, ] Jehoiakim was required to pay a lot of tribute/taxes to King Nebuchadnezzar. But after three years, Jehoiakim rebelled.
Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
2 Then Yahweh sent raiders from Babylonia and Syria, and from the Moab and Ammon people-groups, to attack the people of Judah and get rid of them, just as Yahweh had told his prophets to warn the people would happen.
Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
3 These things happened to the people of Judah according to what Yahweh commanded. [He had decided] to get rid of the people of Judah because of the many sins that King Manasseh [had committed].
Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
4 Manasseh had even caused many innocent people in Jerusalem to be killed, and Yahweh would not forgive that.
kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
5 The other things that happened while Jehoiakim was king, and all the things that he did, are written in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah’.
Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
6 When Jehoiakim died, his son Jehoiachin became the king.
Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
7 [The army of] the king of Babylon [defeated the army of Egypt, and] took control of all the area that the Egyptians formerly controlled, from the brook [at the border] of Egypt [in the south] to the Euphrates River [in the north]. So [the army of] the king of Egypt did not return [to attack Judah] again.
Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
8 Jehoiachin was 18 years old when he became the king of Judah. His mother’s name was Nehushta; she was the daughter of a man from Jerusalem named Elnathan. Jehoiachin ruled in Jerusalem for [only] three months.
Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
9 Jehoiachin did many things that Yahweh considered to be evil, just as his father had done.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
10 [While Jehoiachin was king, ] some officers of King Nebuchadnezzar of Babylon came [along with the whole Babylonian army] to Jerusalem, and they surrounded the city.
Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
11 While they were doing that, Nebuchadnezzar himself came to the city.
ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
12 Then King Jehoiachin and his mother and his advisors and important officers and palace officials all surrendered to the Babylonian army. These thngs happened when Nebuchadnezzar had been king for eight years. He arrested Jehoiachin and took him to Babylon.
Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
13 Just as Yahweh had said would happen, Nebuchadnezzar’s [soldiers] took [to Babylon] all the valuable things from Yahweh’s temple and from the king’s palace. They cut apart all the gold items that King Solomon had put in the temple.
Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
14 They took from Jerusalem [to Babylon] 10,000 people, including the important officials and the best soldiers and the people who made and repaired things that were made of metal. Only the very poor people were left in Judah.
Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
15 Nebuchadnezzar’s soldiers also took to Babylon Jehoiachin’s wives and officials, his mother, and [all] the important people.
Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
16 They also took to Babylon 7,000 of the best soldiers and 1,000 men who knew how to make and repair things that are made from metal. All of these people whom they took were strong and able to fight in wars.
Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
17 Then the king of Babylon appointed Jehoiachin’s uncle, Mattaniah, to be the king [of Judah], and he changed Mattaniah’s name to Zedekiah.
Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
18 When Zedekiah was twenty-one years old, he became king, and he ruled in Jerusalem for eleven years. His mother’s name was Hamutal; she was the daughter of a man named Jeremiah from Libnah [town].
Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
19 But Zedekiah did many things that Yahweh considered to be evil, just as Jehoiakim had done.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
20 Yahweh was very angry. So (and finally/after he had been patient a long time) he expelled the people of Jerusalem and [the other places in] Judah and sent them to Babylon. [That is what happened when] Zedekiah rebelled against the king of Babylon.
Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.